Забур 126 – CARS & CCL

Священное Писание

Забур 126:1-5

Песнь 126

Песнь восхождения, Сулеймана.

1Если не Вечный созидает дом,

то напрасно трудятся его строители.

Если не Вечный охраняет город,

то напрасно бодрствуют стражники.

2Напрасно вы встаёте рано

и сидите допоздна,

тяжёлым трудом добывая себе еду,

тогда как тем, кого любит, Он посылает сон126:2 Или: «ведь тем, кого любит, Он даёт всё необходимое даже во сне»..

3Дети – наследие от Вечного,

они – награда от Него.

4Что стрелы в руке воина,

то сыновья, родившиеся у тебя в дни юности твоей.

5Благословен человек,

чей колчан наполнен ими.

Не постыдятся они,

когда будут говорить с неприятелями

в воротах города126:5 Ворота города были центром всей общественной жизни, около них проходили и судебные разбирательства..

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 126:1-6

Salimo 126

Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.

1Yehova atabwezera akapolo ku Ziyoni,

tinali ngati amene akulota.

2Pakamwa pathu panadzaza ndi kuseka;

malilime athu ndi nyimbo zachimwemwe.

Pamenepo kunanenedwa pakati pa anthu kuti,

“Yehova wawachitira zinthu zazikulu.”

3Yehova watichitira zinthu zazikulu,

ndipo tadzazidwa ndi chimwemwe.

4Tibwezereni madalitso athu, Inu Yehova,

monga mitsinje ya ku Negevi.

5Iwo amene amafesa akulira,

adzakolola akuyimba nyimbo zachimwemwe.

6Iye amene amayendayenda nalira,

atanyamula mbewu yokafesa,

adzabwerera akuyimba nyimbo zachimwemwe,

atanyamula mitolo yake.