Le cantique du nouvel exode
1Et tu diras en ce jour-là :
Je te loue, Eternel,
car même si tu as été ╵irrité contre moi,
ta colère s’apaise,
tu me consoles.
2Oui, Dieu est mon Sauveur,
je me confie en lui ╵et je n’ai plus de crainte,
car l’Eternel, ╵l’Eternel est ma force, ╵il est le sujet de mes chants,
il m’a sauvé12.2 Citation d’Ex 15.2..
3C’est pourquoi, avec joie, ╵vous puiserez de l’eau
aux sources du salut,
4et vous direz en ce jour-là :
Célébrez l’Eternel, ╵invoquez-le,
annoncez aux nations ses œuvres
et proclamez ╵qu’il est sublime.
5Chantez pour l’Eternel,
car il a accompli ╵des œuvres magnifiques ;
que, dans le monde entier, ╵on les connaisse !
6Poussez des cris de joie, ╵exultez d’allégresse, ╵habitants de Sion !
Car, au milieu de vous, ╵il est très grand, ╵lui, le Saint d’Israël.
Nyimbo za Mayamiko
1Tsiku limenelo aliyense wa inu adzati:
“Ndikukuyamikani, Inu Yehova;
chifukwa ngakhale munandipsera mtima,
mkwiyo wanu wachoka,
ndipo mwanditonthoza.
2Zoonadi, Mulungu ndiye Mpulumutsi wanga;
ndidzamudalira ndipo sindidzachita mantha.
Yehova ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga;
Iye wakhala chipulumutso changa.”
3Mudzakondwera popeza Yehova
ali ngati chitsime cha chipulumutso chanu.
4Tsiku limenelo mudzati:
“Yamikani Yehova, tamandani dzina lake;
mulengeze ntchito zake pakati pa mitundu ya anthu,
ndipo mulalike kuti dzina lake ndi lopambana.
5Imbirani Yehova, pakuti wachita ntchito zazikulu;
zimenezi zidziwike pa dziko lonse lapansi.
6Fuwulani ndi kuyimba mwachimwemwe, inu anthu a ku Ziyoni;
pakuti Woyerayo wa Israeli ndi wamkulu pakati panu.”