1Awurade asɛm a ɛbaa Petuel babarima Yoel so ni.
Mmoadabi San Tue
2Muntie saa asɛm yi, mo mpanyimfo;
muntie, mo a mote asase no so nyinaa.
Asɛm bi a ɛte sɛɛ asi mo mmere so
anaa mo mpanyimfo mmere so pɛn?
3Monka nkyerɛ mo mma,
na mo mma nso nka nkyerɛ wɔn mma
na wɔn mma nso nka nkyerɛ awo ntoatoaso a edi so no.
4Nea mmoadabikuw no gyawee no,
mmoadabi akɛse no awe;
nea mmoadabi akɛse no gyawee no,
mmoadabi nkumaa no awe;
nea mmoadabi nkumaa no gyawee no,
mmoadabi afoforo awe.
5Mo asabowfo, munnyan, na munsu!
Mo a monom bobesa nyinaa, muntwa adwo;
muntwa adwo, nsa foforo no nti,
efisɛ wɔahuam afi mo ano.
6Ɔman bi atu mʼasase so sa;
dɔm a wɔyɛ den na wontumi nkan wɔn;
wɔn se te sɛ gyata se
na wɔwɔ gyatabere sebɔmmɔfo.
7Wasɛe me bobe
ne me borɔdɔma nnua.
Wawaawae nnua no ho bona,
atow agu
agyaw ne mman ho fitaa.
8Di awerɛhow sɛ ababaa a ofura atweaatam
na ɔresu ne kunu a ɔwaree no ne mmabaabere mu.
9Aduan ne ahwiesa afɔrebɔde,
wɔayi afi Awurade fi.
Asɔfo no retwa adwo,
wɔn a wɔsom wɔ Awurade anim no.
10Mfuw asɛe,
asase no so awo wosee
aduan no asɛe
nsa foforo no ayow
ngo nyinaa asa.
11Mo ani nwu, mo akuafo,
muntwa adwo, mo a mudua bobe;
Munsi apini mma awi ne atoko,
efisɛ otwabere no asɛe.
12Bobe no akisa
na borɔdɔma nnua no awuwu.
Atoaa nnua, mmedua, aprɛ ne
nnua a ɛwɔ mfuw no so nyinaa ahyew.
Nokware, anigye a nnipa wɔ no
atu ayera.
13Mumfura atweaatam na munni awerɛhow, asɔfo;
mo a mosom wɔ afɔremuka anim, muntwa adwo.
Mumfura atweaatam mmesi pɛ,
mo a mosom wɔ Onyankopɔn anim;
efisɛ aduan ne ahwiesa afɔrebɔde no
to atwa wɔ Onyankopɔn fi.
14Mommɔ mmuadadi kronkron ho dawuru;
momfrɛ nhyiamu kronkron.
Momfrɛ mpanyimfo
ne wɔn a wɔte asase no so nyinaa
mmra Awurade mo Nyankopɔn fi
na wommesu mfrɛ Awurade.
15A, da no de!
Awurade da no abɛn;
Ɛbɛba sɛ ɔsɛe a efi Otumfo hɔ.
16So aduan ho nkɔɔ wɛn, a yɛani tua,
anigye ne ahosɛpɛw to atwa
wɔ yɛn Nyankopɔn fi ana?
17Aba no wu wɔ asase wosee mu,
adekoradan abubu,
aburowpata nso so nni mfaso,
efisɛ nnuan no ahyew.
18Sɛnea anantwi su!
na anantwikuw kyinkyin kwa.
Nguankuw mpo rebrɛ
efisɛ wonni didibea.
19Awurade, wo na misu frɛ wo,
efisɛ ogya ahyew sare so adidibea,
na ogyatannaa ahyew mfuw no so nnua nyinaa.
20Wuram mmoa mpo pere hwehwɛ wo.
Nsuwansuwa ayoyow,
na ogya ahyew sare so adidibea.
1Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.
Kubwera kwa Dzombe
2Inu akuluakulu, imvani izi;
mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko.
Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu,
kapena mʼnthawi ya makolo anu?
3Muwafotokozere ana anu,
ndipo ana anuwo afotokozere ana awo,
ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.
4Chimene dzombe losamera mapiko lasiya
dzombe lowuluka ladya;
chimene dzombe lowuluka lasiya
dzombe lalingʼono ladya;
chimene dzombe lalingʼono lasiya
chilimamine wadya.
5Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire!
Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo;
lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano,
pakuti wachotsedwa pakamwa panu.
6Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa,
wamphamvu ndi wosawerengeka;
uli ndi mano a mkango,
zibwano za mkango waukazi.
7Wawononga mphesa zanga
ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu.
Wakungunula makungwa ake
ndi kuwataya,
kusiya nthambi zake zili mbee.
8Lirani ngati namwali wovala chiguduli,
chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.
9Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa
sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova.
Ansembe akulira,
amene amatumikira pamaso pa Yehova.
10Minda yaguga,
nthaka yauma;
tirigu wawonongeka,
vinyo watsopano watha,
mitengo ya mafuta yauma.
11Khalani ndi nkhawa, inu alimi,
lirani mofuwula inu alimi a mphesa;
imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele,
pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.
12Mpesa wauma
ndipo mtengo wamkuyu wafota;
makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi,
mitengo yonse ya mʼmunda yauma.
Ndithudi chimwemwe cha anthu
chatheratu.
Mulungu Ayitana Anthu kuti Atembenuke
13Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani;
lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe.
Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse,
inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga;
pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa
sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.
14Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya,
itanani msonkhano wopatulika.
Sonkhanitsani akuluakulu
ndi anthu onse okhala mʼdziko
ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu
ndipo alirire Yehova.
15Kalanga ine tsikulo!
Pakuti tsiku la Yehova layandikira;
lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
16Kodi chakudya chathu sichachotsedwa
ife tikuona?
Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu
simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?
17Mbewu zikunyala
poti pansi ndi powuma.
Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka;
nkhokwe zapasuka
popeza tirigu wauma.
18Taonani mmene zikulirira ziweto;
ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku
chifukwa zilibe msipu;
ngakhalenso nkhosa zikusauka.
19Kwa Inu Yehova ndilirira,
pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo,
malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.
20Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu;
timitsinje tonse taphwa
ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.