Yoɛl 1 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Yoɛl 1:1-20

1Awurade asɛm a ɛbaa Petuel babarima Yoel so ni.

Mmoadabi San Tue

2Muntie saa asɛm yi, mo mpanyimfo;

muntie, mo a mote asase no so nyinaa.

Asɛm bi a ɛte sɛɛ asi mo mmere so

anaa mo mpanyimfo mmere so pɛn?

3Monka nkyerɛ mo mma,

na mo mma nso nka nkyerɛ wɔn mma

na wɔn mma nso nka nkyerɛ awo ntoatoaso a edi so no.

4Nea mmoadabikuw no gyawee no,

mmoadabi akɛse no awe;

nea mmoadabi akɛse no gyawee no,

mmoadabi nkumaa no awe;

nea mmoadabi nkumaa no gyawee no,

mmoadabi afoforo awe.

5Mo asabowfo, munnyan, na munsu!

Mo a monom bobesa nyinaa, muntwa adwo;

muntwa adwo, nsa foforo no nti,

efisɛ wɔahuam afi mo ano.

6Ɔman bi atu mʼasase so sa;

dɔm a wɔyɛ den na wontumi nkan wɔn;

wɔn se te sɛ gyata se

na wɔwɔ gyatabere sebɔmmɔfo.

7Wasɛe me bobe

ne me borɔdɔma nnua.

Wawaawae nnua no ho bona,

atow agu

agyaw ne mman ho fitaa.

8Di awerɛhow sɛ ababaa a ofura atweaatam

na ɔresu ne kunu a ɔwaree no ne mmabaabere mu.

9Aduan ne ahwiesa afɔrebɔde,

wɔayi afi Awurade fi.

Asɔfo no retwa adwo,

wɔn a wɔsom wɔ Awurade anim no.

10Mfuw asɛe,

asase no so awo wosee

aduan no asɛe

nsa foforo no ayow

ngo nyinaa asa.

11Mo ani nwu, mo akuafo,

muntwa adwo, mo a mudua bobe;

Munsi apini mma awi ne atoko,

efisɛ otwabere no asɛe.

12Bobe no akisa

na borɔdɔma nnua no awuwu.

Atoaa nnua, mmedua, aprɛ ne

nnua a ɛwɔ mfuw no so nyinaa ahyew.

Nokware, anigye a nnipa wɔ no

atu ayera.

13Mumfura atweaatam na munni awerɛhow, asɔfo;

mo a mosom wɔ afɔremuka anim, muntwa adwo.

Mumfura atweaatam mmesi pɛ,

mo a mosom wɔ Onyankopɔn anim;

efisɛ aduan ne ahwiesa afɔrebɔde no

to atwa wɔ Onyankopɔn fi.

14Mommɔ mmuadadi kronkron ho dawuru;

momfrɛ nhyiamu kronkron.

Momfrɛ mpanyimfo

ne wɔn a wɔte asase no so nyinaa

mmra Awurade mo Nyankopɔn fi

na wommesu mfrɛ Awurade.

15A, da no de!

Awurade da no abɛn;

Ɛbɛba sɛ ɔsɛe a efi Otumfo hɔ.

16So aduan ho nkɔɔ wɛn, a yɛani tua,

anigye ne ahosɛpɛw to atwa

wɔ yɛn Nyankopɔn fi ana?

17Aba no wu wɔ asase wosee mu,

adekoradan abubu,

aburowpata nso so nni mfaso,

efisɛ nnuan no ahyew.

18Sɛnea anantwi su!

na anantwikuw kyinkyin kwa.

Nguankuw mpo rebrɛ

efisɛ wonni didibea.

19Awurade, wo na misu frɛ wo,

efisɛ ogya ahyew sare so adidibea,

na ogyatannaa ahyew mfuw no so nnua nyinaa.

20Wuram mmoa mpo pere hwehwɛ wo.

Nsuwansuwa ayoyow,

na ogya ahyew sare so adidibea.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoweli 1:1-20

1Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.

Kubwera kwa Dzombe

2Inu akuluakulu, imvani izi;

mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko.

Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu,

kapena mʼnthawi ya makolo anu?

3Muwafotokozere ana anu,

ndipo ana anuwo afotokozere ana awo,

ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.

4Chimene dzombe losamera mapiko lasiya

dzombe lowuluka ladya;

chimene dzombe lowuluka lasiya

dzombe lalingʼono ladya;

chimene dzombe lalingʼono lasiya

chilimamine wadya.

5Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire!

Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo;

lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano,

pakuti wachotsedwa pakamwa panu.

6Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa,

wamphamvu ndi wosawerengeka;

uli ndi mano a mkango,

zibwano za mkango waukazi.

7Wawononga mphesa zanga

ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu.

Wakungunula makungwa ake

ndi kuwataya,

kusiya nthambi zake zili mbee.

8Lirani ngati namwali wovala chiguduli,

chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.

9Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa

sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova.

Ansembe akulira,

amene amatumikira pamaso pa Yehova.

10Minda yaguga,

nthaka yauma;

tirigu wawonongeka,

vinyo watsopano watha,

mitengo ya mafuta yauma.

11Khalani ndi nkhawa, inu alimi,

lirani mofuwula inu alimi a mphesa;

imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele,

pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.

12Mpesa wauma

ndipo mtengo wamkuyu wafota;

makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi,

mitengo yonse ya mʼmunda yauma.

Ndithudi chimwemwe cha anthu

chatheratu.

Mulungu Ayitana Anthu kuti Atembenuke

13Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani;

lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe.

Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse,

inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga;

pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa

sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.

14Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya,

itanani msonkhano wopatulika.

Sonkhanitsani akuluakulu

ndi anthu onse okhala mʼdziko

ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu

ndipo alirire Yehova.

15Kalanga ine tsikulo!

Pakuti tsiku la Yehova layandikira;

lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.

16Kodi chakudya chathu sichachotsedwa

ife tikuona?

Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu

simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?

17Mbewu zikunyala

poti pansi ndi powuma.

Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka;

nkhokwe zapasuka

popeza tirigu wauma.

18Taonani mmene zikulirira ziweto;

ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku

chifukwa zilibe msipu;

ngakhalenso nkhosa zikusauka.

19Kwa Inu Yehova ndilirira,

pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo,

malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.

20Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu;

timitsinje tonse taphwa

ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.