Yesaia 6 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Yesaia 6:1-13

Yesaia Soma

1Afe a ɔhene Usia wui mu no, mihuu Awurade sɛ ɔte ahengua a ɛkorɔn na wapagyaw so na nʼatade mmuano ayɛ hyiadan mu hɔ ma. 2Na Serafim a wɔn mu biara wɔ ntaban asia wɔ nʼatifi. Wɔde ntaban no abien kata wɔn anim, na wɔde abien nso kata wɔn nan ho na wɔde abien nso tu. 3Na obiara teɛ mu kyerɛ ne yɔnko se,

“Kronkron! Kronkron! Kronkron ne Asafo Awurade;

Nʼanuonyam ahyɛ asase nyinaa so ma!”

4Wɔn nne nnyigyei maa apon ne abobow ano wosowee, na wusiw yɛɛ hyiadan mu hɔ ma.

5Meteɛɛ mu kae se, “Minnue! Memfata! Meyɛ onipa a mʼano ho ntew, na mete nnipa a wɔn ano ho ntew mu, na mʼani ahu Ɔhene, Awurade Asafo no yi.”

6Na Serafim no mu baako a okura nnyansramma, a ɔde ɔdaban kɔfa fii afɔremuka no so tu baa me nkyɛn. 7Ɔde eyi kaa mʼano kae se, “Hwɛ, eyi aka wʼanofafa, wɔayi wʼafɔdi na wɔatua wo bɔne so ka.”

8Afei, metee Awurade nne a ɛrebisa se, “Hena na mensoma no? Na hena na ɔbɛkɔ ama yɛn?”

Na mekae se, “Mini. Soma me!”

9Na ɔkae se, “Kɔ na kɔka kyerɛ saa nkurɔfo yi se,

“ ‘Ɔte de mobɛte, nanso morente ase;

Ɔhwɛ de mobɛhwɛ, nanso morenhu.’

10Efisɛ mo, moapirim mo koma;

moasisiw mo aso,

akatakata mo ani.

Ɛnyɛ saa a, anka mo ani behu ade,

na mo koma ate asɛm ase,

na moanu mo ho asan aba me nkyɛn, na masa mo yare.”

11Na mekae se, “Enkosi da bɛn, Awurade?”

Na obuae se,

“Enkosi sɛ nkuropɔn no bɛyɛ amamfo

a nnipa ntete so,

enkosi sɛ afi no bɛyɛ afituw

na mfuw no asɛe ayɛ pasaa,

12enkosi sɛ, Awurade bɛpam obiara akɔ akyirikyiri

na asase no ada mpan.

13Mpo, sɛ nkyɛmu du mu baako ka asase no so a

wɔbɛsɛe no bio.

Nso sɛnea dupɔn anaa odum

gyaw dunsin, bere a wɔatwa ato fam no,

saa ara na aba kronkron no bɛyɛ dunsin wɔ asase no so.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 6:1-13

Masomphenya a Yesaya

1Chaka chimene mfumu Uziya anamwalira, ndinaona Ambuye atakhala pa mpando waufumu, wautali ndi wokwezedwa, ndipo mkanjo wawo unali wautali; kotero kuti unadzaza mʼNyumba ya Yehova. 2Pamwamba pawo panayimirira Aserafi, aliyense anali ndi mapiko asanu ndi limodzi: awiri anaphimba nkhope zawo, awiri anaphimba mapazi awo, ndipo awiri ankawulukira. 3Ndipo Aserafiwo amafuwulirana kuti

“Woyera, woyera, woyera Yehova Wamphamvuzonse.

Dziko lonse lapansi ladzaza ndi ulemerero wake.”

4Chifukwa cha kufuwulako maziko a zitseko ndi ziwundo anagwedezeka ndipo mʼNyumba ya Yehova munadzaza utsi.

5Tsono ine ndinafuwula kuti, “Tsoka langa ine! Ndatayika! Pakuti ndine munthu wapakamwa poyipa, ndipo ndimakhala pakati pa anthu a pakamwa poyipa, ndipo ndi maso anga ndaona mfumu Yehova Wamphamvuzonse.”

6Pomwepo mmodzi mwa Aserafi aja anawulukira kwa ine ali ndi khala lamoto mʼdzanja lake, khala limene analichotsa ndi mbaniro pa guwa lansembe. 7Ndipo anandikhudza pakamwa panga ndi khala lamotolo nati, “Taona ndakhudza pa milomo yako ndi khalali; kulakwa kwako kwachotsedwa, machimo ako akhululukidwa.”

8Kenaka ndinamva mawu a Ambuye akuti, “Kodi ndidzatuma yani? Ndipo ndani adzapite mʼmalo mwathu?”

Ndipo ine ndinati, “Ndilipo. Tumeni!”

9Yehova anati, “Pita ndipo ukawawuze anthu awa:

“ ‘Kumva muzimva, koma osamvetsetsa;

kupenya muzipenya koma osaona kanthu.’

10Tsono anthu amenewa uwaphe mtima;

uwagonthetse makutu,

ndipo uwatseke mʼmaso.

Mwina angaone ndi maso awo,

angamve ndi makutu awo,

angamvetse ndi mitima yawo,

kenaka ndi kutembenuka mtima ndi kuchiritsidwa.”

11Pamenepo ine ndinati, “Zimenezo ndi mpaka liti Inu Ambuye?”

Ndipo Iyeyo anandiyankha kuti,

“Mpaka mizinda itasanduka mabwinja

nʼkusowa wokhalamo,

mpaka nyumba zitasowa anthu okhalamo,

mpaka dziko litasanduka chipululu ndithu,

12mpaka Yehova atasamutsira aliyense kutali,

dziko nʼkusiyidwa kwathunthu.

13Ndipo ngakhale chigawo chakhumi cha anthu chitatsala mʼdziko,

nachonso chidzawonongedwa.

Koma monga momwe mitengo ya muwanga ndi thundu

imasiyira chitsa pamene ayidula,

chonchonso mbewu yoyera idzatsalira ngati chitsa chotsala mʼdziko.”