Yesaia 57 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Yesaia 57:1-21

1Atreneefo wu,

na obiara nnwen ho wɔ ne koma mu;

wɔfa nyamesurofo kɔ,

na obiara nte ase

sɛ wɔfa atreneefo kɔ

sɛnea wobeyi wɔn afi bɔne mu.

2Wɔn a wɔnantew tee no

wɔhyɛn asomdwoe mu;

wonya ahomegye bere a wɔadeda sɛ awufo.

3“Nanso mo, mommra ha, mo ɔbayifo mma,

mo nguaman ne mmea nguamanfo mma!

4Hena na moreserew no?

Hena na moredi ne ho fɛw

na morebɔ no adapaa yi?

Monnyɛ atuatewfo fekuw

ne atorofo asefo ana?

5Mode ɔpɛ mmoroso bɔ afɔre wɔ adum mu

ne dua biara a adennan ase;

mode mo mma bɔ afɔre wɔ aku a mu dɔ mu

ne abotan mpaapae ase.

6Anyame a wɔyɛ abo trontrom, a ɛwɔ aku a mu dɔ mu no,

wɔyɛ mo kyɛfa. Wɔn na mopɛ.

Yiw, moahwie nsa afɔrebɔde agu wɔn so

na mode aduan afɔrebɔde ama wɔn.

Eyinom nyinaa akyi, mingow me nsam ana?

7Moasiesie mo nnabea wɔ koko a ɛkorɔn so;

ɛhɔ na mokɔ kɔbɔ afɔre.

8Mo apon ne apongua akyi

na mo de mo abosonsom nsɛsode asisi.

Mufii mʼakyi koyii mo mpa so ntama,

mokɔdaa so na motrɛw mu;

mo ne wɔn a modɔ wɔn mpa yɛɛ apam,

na mohwɛɛ wɔn adagyaw mu.

9Mode ngo kɔɔ Molek nkyɛn

na momaa mo nnuhuam dɔɔso.

Mosomaa mo ananmusifo kɔɔ akyirikyiri;

mosian kɔɔ ɔda mu ankasa!

10Mo nneyɛe maa mo ɔbrɛ,

nanso moanka da se, ‘Yenni anidaso.’

Mopɛɛ ahoɔden foforo

enti moantɔ piti.

11“Hena na wama mo koma atu na wabɔ mo hu sɛɛ

a enti moanni me nokware,

na moankae me

anaa moannwene eyi ho wɔ mo koma mu yi?

So ɛnyɛ komm a mayɛ akyɛ no nti

na munsuro me no ana?

12Mɛda mo trenee ne mo nnwuma adi,

na so remma mo mfaso.

13Sɛ moteɛ mu pɛ mmoa a,

momma mo ahoni a moaboa ano no nnye mo!

Mframa bɛbɔ wɔn nyinaa akɔ,

home kɛkɛ bɛfa wɔn.

Nanso onipa a ɔde me yɛ ne guankɔbea no

bedi asase no so

na wafa me bepɔw kronkron no.”

Koma A Abubu No Awerɛkyekye

14Na wɔbɛka se:

“Monyɛ, monyɛ, munsiesie ɔkwan no!

Munyiyi akwanside mfi me nkurɔfo akwan mu.”

15Na oyi ne nea ɔkorɔn no,

nea ɔte ase daa a ne din yɛ kronkron no se:

“Mete beae a ɛkorɔn na ɛyɛ kronkron,

mene nea ɔwɔ ahonu na ɔyɛ honhom mu hiani nso te,

sɛ mɛkanyan honhom mu hiani no honhom,

na makanyan ne koma a abubu no.

16Meremmɔ sobo afebɔɔ,

na me bo remfuw daa,

sɛ anyɛ saa a onipa honhom bɛtɔ beraw wɔ mʼanim,

onipa ahome a me na mabɔ no.

17Ne nnebɔne adifudepɛ maa me bo fuwii;

metwee nʼaso, na mede abufuw yii mʼani,

nso ɔkɔɔ so yɛɛ nea ne koma pɛ.

18Mahu ne nneyɛe, nanso mɛsa no yare.

Mɛkyerɛ no kwan na makyekye ne werɛ,

19na mama ayeyi aba wɔn a wɔredi awerɛhow wɔ Israel no ano.

Asomdwoe, asomdwoe mmra wɔn a wɔwɔ akyirikyiri ne wɔn a wɔbɛn so,”

sɛɛ na Awurade se. “Na mɛsa wɔn yare.”

20Na amumɔyɛfo te sɛ po a ɛrehuru,

entumi nyɛ komm,

nʼasorɔkye yiyi dontori ne fi.

21“Amumɔyɛfo nni asomdwoe.” Sɛɛ na me Nyankopɔn se.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 57:1-21

1Anthu olungama amafa,

ndipo palibe amene amalingalira mu mtima mwake;

anthu odzipereka amatengedwa,

ndipo palibe amene amamvetsa chifukwa chake.

Anthu olungama amatengedwa

kuti tsoka lisawagwere.

2Iwo amene amakhala moyo wolungama

amafa mwamtendere;

amapeza mpumulo pamene agona mu imfa.

3“Bwerani kuno, anthu ochita zoyipa,

inu muli ngati zidzukulu za mkazi wachigololo ndi wadama!

4Kodi inu mukuseka yani?

Kodi mukumunena ndani

ndi kupotoza pakamwa panu?

Kodi inu si ana owukira,

zidzukulu za anthu abodza?

5Inu mumapembedza mafano pamene mumalobodoka ndi zilakolako zanu pakati pa mitengo ya thundu,

ndiponso pa tsinde pa mtengo uliwonse wa nthambi zambiri.

Mumapereka ana anu ngati nsembe mu zigwa

ndiponso mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.

6Mafano a pakati pa miyala yosalala ya mu zigwa ndiye chuma chanu. Inde, ndiye gawo lanu.

Mumapereka chopereka cha chakumwa kwa mafanowo,

ndipo mumaperekanso chopereka cha chakudya.

Kodi zimenezi

zingandichititse kuti ndikukomereni mtima?

7Inu munayiwala bedi lanu pa phiri lalitali ndi looneka kutali.

Mumapita kumeneko kukapereka nsembe zanu.

8Mʼnyumba mwanu mwayika

mafano kuseri kwa zitseko ndiponso pa mphuthu.

Mwandisiya Ine, mwavula zovala zanu.

Bedi lanu mwalikulitsa ndipo mwakwera ndi zibwenzi zanu,

ndiye mwazilipira kuti mugone nazo.

Kumene mwakwaniritsa zilakolako zanu zoyipa.

9Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta

ndi zonunkhira zochuluka.

Munachita kutumiza akazembe anu kutali;

inu ngakhale munapita ku manda kwenikweniko!

10Inu mumatopa ndi maulendo anu,

koma simunathe kunena kuti, ‘Nʼzopanda phindu.’

Munapezako kumeneko zokhumba zanu

nʼchifukwa chake simunalefuke.

11“Kodi ndani amene mwachita naye mantha ndi kumuopa,

kotero kuti mwakhala mukundinamiza,

ndipo Ine simundikumbukira nʼkomwe,

kapena kuganizirapo mʼmitima yanu za Ine?

Kodi mwaleka kundiopa chifukwa choti

ndakhala chete nthawi yayitali?

12Koma ndaonetsa poyera ntchito zanu zomwe mumati nʼzolungama,

ndi mafano anu kuti nʼzosathandiza.

13Pamene mufuwula kupempha thandizo,

mafano anu amene munasonkhanitsawo ndiyetu akupulumutseni!

Mphepo idzanyamula mafano anu onsewo,

mpweya chabe udzawulutsa mafanowo.

Koma munthu amene amadalira ine

adzalandira dziko lokhalamo.

Phiri langa lopatulika lidzakhala lakelake.”

Mpumulo kwa Anthu Osweka Mtima

14Ndipo panamveka mawu akuti,

“Undani, undani, konzani msewu!

Chotsani zotchinga pa njira yoyendamo anthu anga.”

15Pakuti Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse,

amene alipo nthawi zonse, amene dzina lake ndi Woyerayo,

akunena kuti, “Ndimakhala pamalo aulemu ndi opatulika,

koma ndimakhalanso ndi munthu wodzichepetsa ndi wosweka mtima

kuti odzichepetsawo ndiwalimbitse

ndi kuwachotsa mantha osweka mtima.

16Sindidzawatsutsa anthu mpaka muyaya

kapena kuwapsera mtima nthawi zonse,

popeza kuti ndinalenga anthu anga

ndi kuwapatsa mpweya wamoyo.

17Ine ndinakwiya kwambiri chifukwa cha tchimo lawo ladyera;

ndinawalanga ndi kuwafulatira mokwiya,

koma iwo anapitirirabe kuchita ntchito zawo zoyipa.

18Ndaona zochita zawo, komabe ndidzawachiritsa;

kuwapumulitsa ndi kuwapatsa mtendere,

19anthu olira a mu Israeli adzanditamanda ndi milomo yawo.

Anthu amene ali kutali ndi apafupi pomwe ndidzawapatsa mtendere,”

“Ndipo ndidzawachiritsa.”

Akutero Yehova.

20Koma anthu oyipa ali ngati nyanja yowinduka,

yosatha kukhala bata,

mafunde ake amaponya matope ndi ndere.

21“Palibe mtendere kwa oyipa,” akutero Mulungu wanga.