Yesaia 44 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Yesaia 44:1-28

Israel, Nea Wɔapaw No

1“Na afei tie, Yakob me somfo,

Israel, nea mapaw no.

2Sɛɛ na Awurade se,

nea ɔnwen wo, na ɔyɛɛ wo wɔ awotwaa mu,

ɔno na ɔbɛboa wo:

Nsuro Yakob, me somfo,

Yeshurun, a mapaw no.

3Na mehwie nsu agu asase a awo no so,

ne nsuten wɔ asase kesee so;

mehwie me Honhom agu wo mma so,

ne me nhyira agu wʼasefo so.

4Wobefifi sɛnea sare fifi wɔ mmoa adidibea,

te sɛ mpampuro a ɛwɔ asuten ho.

5Obi bɛka se, ‘Meyɛ Awurade de’;

ɔfoforo bɛfrɛ ne ho se Yakob;

afoforo bɛkɔ so akyerɛw wɔn nsa ho se, ‘Awurade de,’

na wɔafa din Israel.

Ɛyɛ Awurade, Ɛnyɛ Ahoni

6“Sɛɛ na Awurade

Israelhene ne Ogyefo, Asafo Awurade se:

Mene odikanfo ne okyikafo;

Onyankopɔn biara nni hɔ sɛ me.

7Hena na ɔne me sɛ? Ma ɔmpae mu nka.

Ma ɔnka na ɔnkyerɛ wɔ mʼanim

nea asisi fi bere a migyee me tete nkurɔfo sii hɔ,

ne nea ɛrebɛba.

Yiw, ma ɔnhyɛ nea ɛreba ho nkɔm.

8Mommma mo ho mpopo, munnsuro.

Mampae mu anka eyi, manhyɛ ho amfi teteete ana?

Mone me nnansefo. Onyankopɔn foforo bi ka me ho ana?

Dabi, Ɔbotan foforo bi nni hɔ; minnim baako mpo.”

9Wɔn a wɔyɛ ahoni nyinaa nka hwee,

na nneɛma a ɛsom wɔn bo no so nni mfaso.

Wɔn a anka wɔkasa ma wɔn no ani afura;

wonnim wɔn ankasa animguase ho hwee.

10Hena na ɔbɔ onyame na ogu ohoni,

a ne so mma no mfaso biara?

11Ɔno ne wɔn a wɔte sɛ no nyinaa anim begu ase;

adwumfo nyɛ hwee sɛ nnipa.

Momma wɔn nyinaa mmɔ mu nsɔre nnyina,

ehu ne animguase na ɛbɛka wɔn.

12Ɔtomfo fa nʼatonnade

ɔde hyehyɛ nnyansramma mu;

ɔde asae bobɔ so yɛ no ohoni,

ɔde nʼabasa mu ahoɔden mmoroso na ɛyɛ;

ɔkɔm de no na ɔyɛ mmrɛw;

ɔnnom nsu nti ɔtɔ beraw.

13Duadwumfo de hama susuw

na ɔde kyerɛwdua sensan;

na ɔde pɛe yiyi ho

afei ɔde kɔmpaase hyɛ no agyirae.

Osen na ɛyɛ sɛ onipa sɛso,

ɛyɛ sɛ onipa wɔ nʼanuonyam nyinaa mu,

sɛ wɔde besi abosonnan mu.

14Otwitwaa sida,

anaasɛ ebia ɔfaa kwabɔhɔre anaa odum.

Ɔma enyinii wɔ kwae mu,

anaa oduaa ɔpepaw, na osu ma enyinii.

15Ɛyɛ nea onipa de sɔ ogya;

ɔde bi ka ne ho hyew,

ɔde bi sɔ ogya to brodo.

Nanso ɔde bi sen onyame na ɔsɔre no;

ɔyɛ ohoni na ɔkotow no.

16Ɔde dua no mu fa sɔ ogya;

so na ɔnoa nʼaduan,

ɔtoto ne nam wɔ so na wawe amee.

Afei ɔka ne ho hyew na ɔka se,

Aa! mahu ogya; me ho ayɛ me hyew.

17Nkae no ɔde yɛ onyame, ne ohoni;

ɔkotow no na ɔsɔre no.

Ɔbɔ no mpae se,

“Gye me; wo ne me nyame.”

18Wonnim hwee, na wɔnte hwee ase;

wɔatare wɔn ani so nti wonhu ade,

wɔato wɔn adwene mu nti wɔnte hwee ase.

19Obiara nna nnwen ho,

obiara nni nimdeɛ anaa nhumu a ɔde bɛka se,

“Mede fa sɔɔ ogya;

na mpo metoo brodo wɔ ne nnyansramma so;

metotoo nam wɔ so wee.

Ɛsɛ sɛ mede nkae no yɛ akyiwade ana?

Ɛsɛ sɛ mekotow gyentia ana?”

20Saa onipa no di nsõ, nnaadaa koma ma no to kwan;

ɔrentumi nnye ne ho, anaa nka se,

“Nea mikura wɔ me nsa nifa yi nyɛ atoro ana?”

21“Kae saa nneɛma yi, Yakob,

efisɛ, woyɛ me somfo, Israel.

Me na meyɛɛ wo, woyɛ me somfo;

Ao Israel, me werɛ remfi wo.

22Mapra wo mfomso agu te sɛ omununkum

ne wo bɔne te sɛ anɔpa bosu.

San bra me nkyɛn,

efisɛ magye wo.”

23Momfa ahosɛpɛw nto dwom, ɔsorosoro,

na Awurade na wayɛ eyi.

Mommɔ ose, asase ase.

Momma nnwonto so, mo mmepɔw,

mo kwae ne emu nnua nyinaa,

na Awurade agye Yakob,

wada nʼanuonyam adi wɔ Israel.

Wɔbɛtena Yerusalem

24“Sɛɛ na Awurade se,

wo Gyefo a ɔnwen wo wɔ awotwaa mu no:

“Mene Awurade,

nea wayɛ nneɛma nyinaa,

nea ɔno nko ara trɛw ɔsoro mu

nea ɔno nko ara twee asase mu,

25nea ɔsɛe atoro adiyifo nsɛnkyerɛnne

na ɔma nkɔmhyɛfo yɛ nkwaseafo,

nea otutu anyansafo adenim gu

na ɔdan no nkwaseasɛm,

26nea ɔma nʼasomfo nsɛm ba mu

nea ɔhyɛ nʼasomafo nkɔmhyɛ mu ma,

“nea ɔka fa Yerusalem ho se, ‘Wɔbɛtena mu,’

ne Yuda nkurow ho se, ‘Wɔbɛkyekye,’

ne mmubui ho se, ‘Mɛyɛ no foforo,’

27nea ɔka kyerɛ asubun se, ‘Yow,

na mɛma wo nsuwa ayoyow,’

28nea ɔka wɔ Kores ho se, ‘Ɔyɛ me guanhwɛfo

na obewie nea mepɛ nyinaa yɛ;

ɔbɛka afa Yerusalem ho se, “Ma wɔnkyekyere bio,”

na waka afa asɔredan no ho se, “Ma wɔnto ne fapem.” ’ ”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 44:1-28

Israeli Wosankhidwa wa Yehova

1Yehova akuti, “Mvera tsopano, iwe Yakobo, mtumiki wanga,

Israeli, amene ndinakusankha.

2Yehova

amene anakupanga iwe, anakuwumba iwe mʼmimba ya amayi ako,

ndi amene adzakuthandiza iwe. Iye akuti,

Usachite mantha, iwe Yakobo, mtumiki wanga,

Yesuruni, amene ndinakusankha.

3Pakuti ndidzathira madzi pa nthaka yowuma,

ndi kuyendetsa mitsinje mʼdziko lowuma;

ndidzatumiza Mzimu wanga pa ana anu,

ndi kutsitsa madalitso anga pa zidzukulu zanu.

4Iwo adzakula ngati udzu wothirira bwino

ndi ngati bango lomera mʼmbali mwa mitsinje ya madzi oyenda.

5Wina adzanena kuti, ‘Ine ndine wa Yehova;’

wina adzadzitcha yekha wa banja la Yakobo;

winanso adzalemba pa dzanja lake, ‘Wa Yehova’

ndipo adzadzitcha wa banja la Israeli.

Yehova, Osati Mafano

6“Yehova Mfumu

ndi Mpulumutsi wa Israeli, Yehova Wamphamvuzonse akuti:

Ine ndine woyamba ndi wotsiriza;

palibenso Mulungu wina koma Ine ndekha.

7Ndani nanga angafanane ndi Ine? Muloleni kuti ayankhule.

Muloleni andifotokozere ndi kundiyalira bwino lomwe

zimene zinachitika kuyambira pamene ndinkakhazikitsa anthu anga akalekale,

ndi ziti zimene zidzachitike;

inde, muloleni alosere zimene zikubwera.

8Musanjenjemere, musachite mantha.

Kodi sindinakuwuzeni zimenezi ndi kuzilosera kalekale lomwe?

Inu ndinu mboni zanga. Kodi aliponso Mulungu wina kupatula Ine?

Ayi, palibe Thanthwe linanso limene sindikulidziwa.”

9Onse amene amapanga mafano ngachabe,

ndipo milungu imene amayilemekeza ndi yopanda phindu.

Iwo amene amapembedza mafano ndi wosaona;

ndipo sazindikira kanthu. Choncho adzawachititsa manyazi.

10Ndani amasema mulungu ndi kuwumba fano,

limene silingamupindulire?

11Iye pamodzi ndi anzake onse adzawachititsa manyazi;

amisiri a mafano ndi anthu chabe.

Aloleni onse asonkhane ndi kuyima pabwalo la milandu;

onse adzaopsedwa ndipo adzachita manyazi.

12Mmisiri wa zitsulo amatenga chitsulo

ndipo amachiyika pa makala amoto;

ndi dzanja lake lamphamvu

amachisula pochimenya ndi nyundo.

Pambuyo pake mʼmisiri uja amamva njala natha mphamvu;

iye samwa madzi, ndipo amalefuka.

13Mmisiri wa matabwa nayenso amayeza mtengo ndi chingwe

ndipo amajambula chithunzi ndi cholembera;

amasema bwinobwino ndi chipangizo chake

ndipo amachiwongola bwino ndi chida chake.

Amachipanga ngati munthu,

munthu wake wokongola

kuti aliyike mʼnyumba yake yachipembedzo.

14Amagwetsa mitengo ya mkungudza,

mwinanso amatenga mtengo wa payini kapena wa thundu

nʼkudzisankhira mtengo wabwino pakati pa mitengo ya mʼnkhalango,

ndipo amadzala mtengo wa payini ndi kuwuleka kuti ukule ndi mvula.

15Mitengoyo munthu amachitako nkhuni;

nthambi zina amasonkhera moto wowotha,

amakolezera moto wophikira buledi

ndi mbali ina ya mtengowo amapangira mulungu ndipo amapembedza;

iye amapanga fano ndi kumaligwadira.

16Chigawo china cha mtengowo amasonkhera moto

wowotcherapo nyama imene

amadya, nakhuta.

Iye amawotha motowo ndipo amanena kuti,

“Aa! Ndikumva kutentha; pano pali moto.”

17Chigawo chotsala amapanga kamulungu, fano lake limenelo;

amaligwadira ndi kulipembedza.

Amapemphera kwa fanolo ndipo amanena kuti,

“Iwe ndiwe mulungu wanga, ndipulumutse.”

18Anthu otere sadziwa kanthu, samvetsa kanthu kalikonse;

maso awo ndi omatirira ndipo sangathe kuona,

ndipo mitu yawo ndi yogontha kotero sangathe kumvetsa.

19Palibe amene amayima nʼkulingalira.

Palibe wanzeru kapena womvetsa zinthu bwino woti nʼkunena kuti,

chigawo china cha mtengowo ndinasonkhera moto;

pa makala ake ndinaphikira buledi,

ndinawotchapo nyama ndipo ndinadya.

Chigawo chotsalachi ndipangire chinthu chonyansachi.

Kodi ndidzagwadira mtengo?

20Munthu wotere ali ngati wodya phulusa, maganizo ake opusa amusocheretsa;

motero kuti sangathe kudzipulumutsa yekha kapena kudzifunsa kuti,

“Kodi chinthu chili mʼmanja mwangachi si chabodza?”

21Yehova akuti, “Iwe Yakobo, kumbukira zinthu izi

popeza kuti ndiwe mtumiki wanga, iwe Israeli.

Ine ndinakupanga iwe, ndiwe mtumiki wanga;

iwe Israeli, sindidzakuyiwala.

22Ndachotsa zolakwa zako ngati mitambo,

ndi machimo ako ngati nkhungu ya mmawa.

Bwerera kwa Ine,

popeza ndakupulumutsa.”

23Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga, pakuti Yehova wachita zimenezi;

fuwula, iwe dziko lapansi.

Imbani nyimbo, inu mapiri,

inu nkhalango ndi mitengo yonse,

chifukwa Yehova wawombola Yakobo,

waonetsa ulemerero wake mwa Israeli.

Anthu Adzakhalanso mu Yerusalemu

24Yehova Mpulumutsi wanu, amene

anakuwumbani mʼmimba ya amayi anu akuti:

“Ine ndine Yehova,

amene anapanga zinthu zonse,

ndinatambasula ndekha zinthu zakuthambo,

ndinayala ndekha dziko lapansi.

25Ndine amene ndinalepheretsa mipingo ya anthu onyenga,

ndipo ndimapusitsa owombeza mawula.

Ndimasokoneza anthu a nzeru,

ndi kuonetsa kuti nzeru zawo nʼzopusa.

26Ndine amene ndimatsimikiza mawu a atumiki ake

ndi kukwaniritsa zimene analosera amithenga ake.

“Ndine amene ndinanena za Yerusalemu kuti mudzakhalanso anthu.

Ndinanenanso za mizinda ya Yuda kuti idzamangidwanso.

Za mabwinja awo ndinanena kuti ndidzawawutsanso.

27Ndine amene ndinawuza nyanga yayikulu kuti, ‘Uma’

ndipo ndidzawumitsa mitsinje yako.

28Ndine amene ndinanena kwa Koresi kuti, ‘Iye ndiye mʼbusa wanga,’

ndipo adzachita zonse zimene ndikufuna;

iye adzalamula kuti, ‘Yerusalemu amangidwenso’

ndi kuti, ‘Maziko a Nyumba ya Mulungu ayikidwenso.’ ”