Yesaia 40 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Yesaia 40:1-31

Onyankopɔn Nkurɔfo Awerɛkyekye

1Monkyekye, monkyekye me nkurɔfo werɛ.

Saa na mo Nyankopɔn se.

2Monka asomdwoesɛm nkyerɛ Yerusalem,

na mompae mu nka nkyerɛ no se

ne som dennen no aba awiei,

wɔatua ne bɔne no so ka,

na wɔanya ne bɔne nyinaa so akatua mmɔho

afi Awurade nsam.

3Nne bi reteɛ mu se,

“Munsiesie ɔkwan mma Awurade

wɔ nweatam no so.

Monteɛ ɔtempɔn wɔ sare no so

mma yɛn Nyankopɔn.

4Obon biara bɛyɛ ma,

bepɔw ne nkoko nyinaa bɛkɔ fam,

asase a ɛyɛ abonkyiabonkyi no bɛyɛ tamaa,

na mmeae a ɛyɛ akɔntɔnkye no ayɛ tataw.

5Na Awurade anuonyam bɛda adi,

na nnipa nyinaa behu.

Efisɛ Awurade na waka!”

6Nne bi kae se, “Teɛ mu.”

Na mekae se, “Menteɛ mu nka dɛn?”

“Nnipa nyinaa te sɛ sare,

na wɔn anuonyam nyinaa te sɛ afuw so nhwiren.

7Sare hyew, na nhwiren twintwam

efisɛ Awurade ahomegu fa wɔn so.

Nokware, nnipa no yɛ sare.

8Sare hyew, na nhwiren twintwam,

nanso yɛn Nyankopɔn asɛm no tim hɔ daa.”

9Wo a wode asɛm pa reba Sion,

foro kɔ bepɔw tenten bi so.

Wo a wode asɛm pa reba Yerusalem,

ma wo nne so na teɛ mu,

ma so, nsuro;

ka kyerɛ Yuda nkurow se,

“Mo Nyankopɔn ni!”

10Hwɛ, Asafo Awurade de tumi reba,

na nʼabasa bedi hene ama no.

Hwɛ, nʼakatua ka ne ho,

na ɔde nʼabasobɔde nam.

11Ɔhwɛ ne nguankuw sɛ oguanhwɛfo.

Ɔboa nguantenmma no wɔ nʼabasa so

oturu wɔn ne koko so;

na nguan a wɔwɔ mma no, ɔka wɔn brɛoo.

12Hena na wasusuw obon mu nsu wɔ ne nsam

anaa ɔde ne nsateaa asusuw ɔsoro?

Hena na ɔde asase so mfutuma agu kɛntɛn mu,

anaa wakari mmepɔw wɔ nsania so

ne nkoko wɔ nsania apampaa so?

13Hena na wate Awurade ase,

anaa wakyerɛkyerɛ no sɛ ne fotufo?

14Hena na Awurade abisa no sɛ ɔnkyerɛ no biribi ase,

na hena na ɔkyerɛɛ no ɔkwan pa no?

Hena na ɔmaa no nimdeɛ

anaa ɔkyerɛɛ no nhumu kwan?

15Ampa ara aman no te sɛ nsu sope wɔ bokiti mu;

wɔde wɔn toto mfutuma a egu nsania so ho;

ɔkari nsupɔw te sɛnea ɛyɛ mfutuma muhumuhu.

16Lebanon nnɔɔso mma afɔremuka so gya,

na ne mmoa renso mma ɔhyew afɔrebɔde.

17Aman nyinaa nsɛ hwee wɔ nʼanim;

obu wɔn adehunu bi

a wɔnka hwee.

18Afei hena ho na wode Onyankopɔn bɛtoto?

Nsɛsode bɛn ho na wode no bɛto?

19Ohoni de, odwumfo na ɔyɛ,

na sikadwumfo de sikakɔkɔɔ agu ho

na wasiesie dwetɛ nkɔnsɔnkɔnsɔn ama no.

20Ohiani a ɔrentumi mfa saa ayɛyɛde yi mma no

kɔhwehwɛ dua a ɛremporɔw.

Ɔhwehwɛ odwumfo nyansafo

na wayɛ ohoni a ɛremmunum nhwe fam asi hɔ.

21Wunnim ana?

Wontee ana?

Wɔnnka nkyerɛɛ wo mfii mfiase no ana?

Efi bere a wɔbɔɔ asase no, wontee ase ana?

22Ɔte ahengua so wɔ asase dantaban no atifi

ɛso nnipa te sɛ tɛwtɛw

ɔtwe ɔsoro mu te sɛ bamkyinii,

na ɔtrɛw mu sɛ ntamadan tena mu.

23Ɔma ahemmea yɛ nnipahunu

na wiase yi sodifo nso, ɔbrɛ wɔn ase.

24Wɔtɛw wɔn ara pɛ,

woduaa wɔn ara pɛ,

wogyee ntin wɔ asase mu pɛ,

na wahome agu wɔn so ama wɔakisa,

na mframa abɔ wɔn kɔ te sɛ ntɛtɛ.

25“Hena ho na wode me bɛto?

Anaasɛ hena na ɔne me sɛ?” Ɔkronkronni no na ose.

26Momma mo ani so nhwɛ ɔsoro:

Hena na ɔbɔɔ eyinom nyinaa?

Nea oyiyi ɔsoro nsoromma mmaako mmaako,

na ɔbɔ obiara din frɛ no.

Nʼahoɔden ne ne tumi nti

wɔn mu baako mpo nyera.

27Adɛn na wunwiinwii, Yakob,

na woka se, Israel,

“Mʼakwan ahintaw Awurade;

na me Nyankopɔn abɔ mʼasɛm agu”?

28Wunnim ana?

Wontee ana?

Awurade yɛ daapem Nyankopɔn,

na ɔyɛ asase nyinaa yɛfo.

Ɔremmrɛ na ɔrentɔ beraw,

na ne nhumu nni nhwehwɛmu.

29Ɔma nea watɔ beraw ahoɔden

nea wayɛ mmerɛw nso, ɔto nʼahoɔden so.

30Mpo, mmabun brɛ, na wɔtɔ beraw,

na mmerante hintihintiw hwehwe ase;

31Nanso, wɔn a wɔn ani da Awurade so

benya ahoɔden foforo.

Wɔde ntaban sɛ akɔre de betu akɔ wim;

wobetu mmirika, na wɔrentɔ beraw.

Wɔbɛnantew, na wɔrentɔ piti.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 40:1-31

Mawu a Chitonthozo kwa Anthu a Mulungu

1Atonthozeni, atonthozeni anthu anga,

akutero Mulungu wanu.

2Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu

ndipo muwawuzitse

kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha,

tchimo lawo lakhululukidwa.

Ndawalanga mokwanira

chifukwa cha machimo awo onse.

3Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti,

“Konzani njira ya Yehova

mʼchipululu;

wongolani njira zake;

msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.

4Chigwa chilichonse achidzaze.

Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse;

Dziko lokumbikakumbika alisalaze,

malo azitundazitunda awasandutse zidikha.

5Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera,

ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona,

pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”

6Wina ananena kuti, “Lengeza.”

Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani?

“Pakuti anthu onse ali ngati udzu

ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.

7Udzu umanyala ndipo maluwa amafota

chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.”

Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.

8Udzu umanyala ndipo maluwa amafota,

koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”

9Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni,

kwera pa phiri lalitali.

Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu,

fuwula kwambiri,

kweza mawu, usachite mantha;

uza mizinda ya ku Yuda kuti,

“Mulungu wanu akubwera!”

10Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu,

ndipo dzanja lake likulamulira,

taonani akubwera ndi mphotho yake

watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.

11Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa:

Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake

ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake

ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.

12Kodi ndani akhoza kuyeza kuchuluka kwa madzi a mʼnyanja ndi chikhatho chake,

kapena kuyeza kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake?

Ndani akhoza kuyeza dothi lonse la dziko lapansi mʼdengu,

kapena kuyeza kulemera kwa

mapiri ndi zitunda ndi pasikelo?

13Ndani anapereka malangizo kwa Mzimu wa Yehova

kapena kumuphunzitsa Iye monga phungu wake?

14Kodi Yehova anapemphapo nzeru kwa yani kuti akhale wopenya,

kapena kuti aphunzire njira yoyenera ndi nzeru?

Iye anapempha nzeru kwa yani

ndi njira ya kumvetsa zinthu?

15Ndithudi mitundu ya anthu ili ngati dontho la madzi ochoka mu mtsuko.

Iwo akungoyesedwa ngati fumbi chabe pa sikelo;

mʼmanja mwa Yehova zilumba nʼzopepuka ngati fumbi.

16Nkhalango ya ku Lebanoni singakwanire nkhuni zosonkhera moto pa guwa lansembe,

ngakhale nyama zake sizingakwanire kupereka nsembe zopsereza.

17Pamaso pa Yehova mitundu yonse ya anthu ili ngati chinthu chopandapake;

Iye amayiwerengera ngati chinthu chopanda phindu

ndi cha chabechabe.

18Kodi tsono Mulungu mungamuyerekeze ndi yani?

Kodi mungamufanizire ndi chiyani?

19Likakhala fano, mʼmisiri ndiye analipanga

ndipo mʼmisiri wa golide amalikuta ndi golide

naliveka mkanda wasiliva.

20Mʼmphawi amene sangathe kupeza ngakhale chopereka nsembe chotere

amasankha mtengo umene sudzawola,

nafunafuna mʼmisiri waluso woti

amupangire fano limene silingasunthike.

21Kodi simukudziwa?

Kodi simunamve?

Kodi sanakuwuzeni kuyambira pachiyambi pomwe?

Kodi simunamvetsetse chiyambire cha dziko lapansi?

22Yehova amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba ndiye analenga dziko lapansi,

Iye amaona anthu a dziko lapansi ngati ziwala.

Ndipo anafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchinga,

nayikunga ngati tenti yokhalamo.

23Amatsitsa pansi mafumu amphamvu

nasandutsa olamula a dziko kukhala achabechabe.

24Inde, iwo ali ngati mbewu zimene zangodzalidwa kumene

kapena kufesedwa chapompano,

ndi kungoyamba kuzika mizu kumene

ndi pamene mphepo imawombapo nʼkuziwumitsa

ndipo kamvuluvulu amaziwulutsa ngati mankhusu.

25Woyera uja akuti, “Kodi mudzandiyerekeza Ine ndi yani?

Kapena kodi alipo wofanana nane?”

26Tayangʼanani mlengalenga ndipo onani.

Kodi ndani analenga zonsezi mukuzionazi?

Yehova ndiye amene amazitsogolera ngati gulu la ankhondo,

nayitana iliyonse ndi dzina lake.

Ndipo popeza Iye ali ndi nyonga zambiri,

palibe ndi imodzi yomwe imene inasowapo.

27Iwe Yakobo, chifukwa chiyani umanena

ndi kumadandaula iwe Israeli, kuti,

“Yehova sakudziwa mavuto anga,

Mulungu wanga sakusamala zomwe zikundichitikira ine?”

28Kodi simukudziwa?

Kodi simunamve?

Yehova ndiye Mulungu wamuyaya,

ndiyenso Mlengi wa dziko lonse lapansi.

Iye sadzatopa kapena kufowoka

ndipo palibe amene angadziwe maganizo ake.

29Iye amalimbitsa ofowoka

ndipo otopa amawawonjezera mphamvu.

30Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufowoka,

ndipo achinyamata amapunthwa ndi kugwa;

31koma iwo amene amakhulupirira Yehova

adzalandira mphamvu zatsopano.

Adzawuluka ngati chiwombankhanga;

adzathamanga koma sadzalefuka,

adzayenda koma sadzatopa konse.