Yesaia 38 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Yesaia 38:1-22

Hesekia Yare

1Saa nna no mu no, Hesekia yaree owuyare, na Amos babarima Odiyifo Yesaia kɔɔ ne nkyɛn kɔkae se, “Sɛnea Awurade se ni: Toto wʼakwan yiye, efisɛ worebewu; na wo ho renyɛ wo den bio.”

2Bere a Hesekia tee asɛm yi, otwaa nʼani hwɛɛ ɔfasu, bɔɔ Awurade mpae se, 3“Kae, Awurade, sɛnea manantew wʼanim nokware mu na mede me koma ayɛ nea ɛfata wɔ wʼanim.” Na Hesekia suu bebree.

4Na saa asɛm yi fii Awurade nkyɛn kɔɔ Yesaia hɔ se, 5“San kɔ Hesekia nkyɛn, na kɔka kyerɛ no se, ‘Sɛɛ na Awurade, wʼagya Dawid Nyankopɔn, ka: Mate wo mpaebɔ no, na mahu wo nisu. Mede mfe dunum bɛka wo nkwanna ho. 6Na megye wo ne kuropɔn yi afi Asiriahene nsam. Mɛbɔ kuropɔn yi ho ban.

7“ ‘Na eyi ne nsɛnkyerɛnne a Awurade bɛyɛ de adi ho adanse sɛ, obedi ne bɔhyɛ so: 8Mɛma owia ano sunsuma atwe akɔ nʼakyi anammɔn du wɔ Ahas antweri so.’ ” Ɛno nti, owiahyerɛn no kɔɔ nʼakyi anammɔn du.

9Nea Yudahene Hesekia kyerɛw wɔ ne yare ne nʼayaresa akyi ni:

10Mekae se, “Mʼasetena mu nnapa yi mu

ɛsɛ sɛ mefa owu apon mu

na wogye me mfe a aka yi ana?”

11Mekae se, “Merenhu Awurade Nyankopɔn bio

Awurade a ɔwɔ ateasefo asase so.

Merenhu adesamma bio,

anaa merenka wɔn a wɔte wiase yi ho bio.

12Wɔadwiriw me fi agu agye afi me nsam,

te sɛ, oguanhwɛfo ntamadan.

Matwa me nkwa so sɛnea ɔnwemfo

twa me fi asadua so;

awia ne anadwo wutwaa me nkwa so.

13Mede ntoboase twɛn kosii ahemadakye,

nanso wɔbobɔɔ me nnompe mu te sɛ gyata;

awia ne anadwo wutwaa me nkwa so.

14Misuu sɛ asomfena anaa asukɔnkɔn;

mitwaa adwo sɛ, aborɔnoma a ɔredi awerɛhow.

Mʼani yɛɛ siamoo bere a mehwɛɛ soro.

Mewɔ ɔhaw mu, Awurade, bra bɛboa me!”

15Na dɛn na metumi aka?

Wakasa akyerɛ me, na ɔno ankasa na wayɛ eyi.

Mede ahobrɛase bɛnantew mʼasetena nyinaa mu

me kra ahoyeraw yi nti.

16Awurade, ɛnam saa nneɛma yi so na nnipa nya nkwa

na me honhom nso nya nkwa wɔ mu.

Wode mʼakwahosan asan ama me

nam so ama manya nkwa.

17Yiw, ɛyɛ me yiyeyɛ nti

na mekɔɔ saa ahoyeraw yi mu.

Wo dɔ nti, wode me siei

na mankɔ ɔsɛe amoa mu;

na wode me bɔne nyinaa akyɛ me.

18Ɔda rentumi nkamfo wo;

owu rentumi nto wo ayeyi nnwom;

wɔn a wosian kɔ amoa mu no

rentumi nnya anidaso wɔ wo nokware mu bio.

19Ateasefo nko na wobetumi akamfo wo,

sɛnea mereyɛ nnɛ yi;

agyanom ka wo nokwaredi ho asɛm

kyerɛ wɔn mma.

20Awurade begye me nkwa,

na yɛde asanku bɛto nnwom

yɛn nkwanna nyinaa

Awurade fi.

21Na Yesaia kae se, “Momfa borɔdɔma nyɛ nku mfa nsra pɔmpɔ no so, na ne ho bɛtɔ no.”

22Na Hesekia bisae se, “Dɛn nsɛnkyerɛnne na ɛbɛda no adi sɛ, mɛkɔ Awurade asɔredan mu?”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesaya 38:1-22

Kudwala kwa Hezekiya

1Nthawi imeneyo Mfumu Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anati “Yehova akuti: Konza bwino nyumba yako, pakuti ukufa; suchira.”

2Hezekiya anatembenuka nayangʼana kukhoma, napemphera kwa Yehova kuti, 3“Inu Yehova, kumbukirani momwe ndayendera pamaso panu mokhulupirika ndi modzipereka ndipo ndakhala ndikuchita zabwino pamaso panu.” Ndipo Hezekiya analira mosweka mtima.

4Ndipo Yehova analamula Yesaya kuti: 5“Pita kwa Hezekiya ndipo ukamuwuze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa kholo lake Davide akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona; ndidzakuwonjezera zaka 15 pa moyo wako. 6Ndipo ndidzakupulumutsa, iwe pamodzi ndi mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya, Ine ndidzawuteteza mzindawu.

7“ ‘Ichi ndi chizindikiro cha Yehova kwa iwe kutsimikiza kuti Yehova adzachita zimene walonjeza: 8Chithunzithunzi chimene dzuwa likuchititsa pa makwerero a Ahazi ndidzachibweza mʼmbuyo makwerero khumi.’ ” Ndipo chithunzithunzi chinabwerera mʼmbuyo makwerero khumi.

9Ndakatulo ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda imene analemba atadwala ndi kuchira:

10Ine ndinaganiza kuti

ndidzapita ku dziko la akufa

pamene moyo ukukoma.

11Ndinaganiza kuti, “Sindidzaonanso Yehova,

mʼdziko la anthu amoyo,

sindidzaonanso mtundu wa anthu

kapena kukhala pamodzi ndi amene amakhala pa dziko lapansi lino.

12Nyumba yanga yasasuka

ndipo yachotsedwa.

Ngati tenti ya mʼbusa mwapindapinda moyo wanga,

ngati munthu wowomba nsalu;

kuyambira usana mpaka usiku mwakhala mukundisiya.

13Ndinkalira kupempha chithandizo usiku wonse mpaka mmawa;

koma Inu Yehova munaphwanya mafupa anga ngati mkango,

ndipo mwakhala mukundisiya.

14Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba,

ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula.

Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga.

Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”

15Koma ine ndinganene chiyani?

Yehova wayankhula nane, ndipo Iye ndiye wachita zimenezi.

Chifukwa cha kuwawa kwa mtima wanga,

ine ndidzayenda modzichepetsa masiku amoyo wanga onse.

16Ambuye, masiku anga ali mʼmanja mwanu.

Mzimu wanga upeza moyo mwa Inu.

Munandichiritsa ndi

kundikhalitsa ndi moyo.

17Ndithudi, ine ndinamva zowawa zotere

kuti ndikhale ndi moyo;

Inu munandisunga

kuti ndisapite ku dzenje la chiwonongeko

chifukwa mwakhululukira

machimo anga onse.

18Pakuti akumanda sangathe kukutamandani,

akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani.

Iwo amene akutsikira ku dzenje

sangakukhulupirireni.

19Amoyo, amoyo okha ndiwo amakutamandani,

monga mmene ndikuchitira ine lero lino;

abambo amawuza ana awo za

kukhulupirika kwanu.

20Yehova watipulumutsa.

Tiyeni tiyimbe ndi zoyimbira za zingwe

masiku onse a moyo wathu

mʼNyumba ya Yehova.

21Yesaya anati, “Anthu atenge mʼbulu wankhunyu ndipo apake pa chithupsacho ndipo Hezekiya adzachira.”

22Hezekiya nʼkuti atafunsa kuti, “Kodi chizindikiro chako nʼchiyani chotsimikiza kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova?”