Yeremia 9 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Yeremia 9:1-26

1Ao, sɛ me ti yɛ asuti,

na mʼaniwa yɛ nusu abura a!

Mɛtew nusu awia ne anadwo

ama me nkurɔfo a wɔakunkum wɔn no.

2Ao, sɛ mewɔ akwantufo asoɛe

wɔ nweatam no so a

anka megyaw me nkurɔfo hɔ

na mafi wɔn nkyɛn;

efisɛ wɔn nyinaa yɛ nguaman,

nnipakuw a wonni nokware.

3“Wosiesie wɔn tɛkrɛma

te sɛ agyan de di atoro;

Ɛnyɛ nokware so na wɔnam

di yiye wɔ asase yi so.

Wɔyɛ bɔne toatoa so;

na wonnye me nto mu,”

Awurade na ose.

4“Monhwɛ yiye wɔ mo nnamfonom ho;

munnye obiara nni wɔ mo abusua mu.

Efisɛ wɔn mu biara yɛ ɔdaadaafo,

na adamfo biara yɛ ɔsɛefo.

5Adamfo daadaa adamfo,

na wɔn mu biara nka nokware.

Wɔn tɛkrɛma akokwaw atorodi mu,

wɔde bɔneyɛ haw wɔn ho.

6Wote nnaadaa mfimfini;

na wɔn nnaadaa mu wɔmpɛ sɛ wogye me to mu,”

sɛnea Awurade se ni.

7Ɛno nti, sɛɛ na Asafo Awurade se,

“Hwɛ, mɛnan wɔn asɔ wɔn ahwɛ,

na dɛn bio na metumi ayɛ

esiane me nkurɔfo yi bɔne nti?

8Wɔn tɛkrɛma yɛ agyan a ano wɔ bɔre;

ɛka nnaadaasɛm.

Obiara kasa asomdwoe mu kyerɛ ne yɔnko,

nanso ne koma mu de, osum no afiri.

9Ɛnsɛ sɛ metwe wɔn aso wɔ eyi ho?”

Sɛɛ na Awurade se.

“Ɛnsɛ sɛ mʼankasa metɔ

ɔman a ɛte sɛɛ so were ana?

10Mesu na metwa adwo ama mmepɔw no,

mɛbɔ abubuw a ɛfa nweatam adidibea ho.

Ayɛ fo na obi mfa hɔ bio,

na wɔnte anantwi su wɔ hɔ.

Wim nnomaa no atutu kɔ

na mmoa no nso aguan kɔ.

11“Mɛyɛ Yerusalem mmubui siw,

sakraman atu;

na mɛma Yuda nkurow ada mpan

sɛnea obiara ntumi ntena hɔ.”

12Onipa bɛn na onim nyansa ara sɛ ɔbɛte eyi ase? Hena na Awurade akyerɛkyerɛ no a obetumi akyerɛ ase? Adɛn nti na wɔasɛe asase no ama ada mpan sɛ nweatam a obiara ntumi mfa so?

13Awurade kae se, “Esiane sɛ wɔapo me mmara a mehyɛ maa wɔn no nti, wɔanyɛ osetie amma me na wɔanni me mmara so. 14Mmom, wɔadi wɔn koma asoɔden akyi, wɔadi Baalnom akyi sɛnea wɔn agyanom kyerɛɛ wɔn no.” 15Ɛno nti, nea Asafo Awurade, Israel Nyankopɔn no se ni: “Hwɛ, mɛma saa nnipa yi adi aduan a ɛyɛ nwen na wɔanom nsu a wɔde awuduru afra. 16Mɛbɔ wɔn ahwete amanaman a wɔn anaa wɔn agyanom nnim so no so, na mede afoa bɛtaa wɔn kosi sɛ mɛsɛe wɔn.”

17Sɛnea Awurade tumfo se ni:

“Dwene ho! Frɛ mmea agyaadwotwafo no,

frɛ wɔn a wɔakwadaw mu pa ara.

18Ma wɔmmra ntɛm

mmesu ngu yɛn so

kosi sɛ yɛn ani so bɛtaa nusu

na nusu aguare yɛn.

19Wɔte agyaadwotwa nnyigyei fi Sion se,

‘Wɔasɛe yɛn!

Yɛn anim agu ase yiye!

Ɛsɛ sɛ yetu fi yɛn asase so

efisɛ yɛn afi abubu.’ ”

20Afei, mo mmea, muntie Awurade asɛm;

monyɛ aso mma nsɛm a efi nʼanom.

Monkyerɛ mo mmabea sɛnea wotwa dwo;

monkyerɛ mo ho mo ho abubuwbɔ.

21Owu aforo afa yɛn mfɛnsere mu

ahyɛn yɛn aban mu;

apam mmofra afi mmɔnten so

ne mmerante afi ɔman aguabɔbea.

22Ka se, “Sɛɛ Na Awurade se,

“ ‘Nnipa afunu bɛdeda hɔ

te sɛ sumina a egugu petee mu,

te sɛ aburow a nnɔbaetwafo atwa agu nʼakyi

a obiara mmoaboaa ano.’ ”

23Eyi ne nea Awurade se:

“Mma onyansafo mfa ne nyansa nhyehyɛ ne ho

anaa ɔhoɔdenfo mfa nʼahoɔden nhyehyɛ ne ho

anaa ɔdefo mfa nʼahonya nhyehyɛ ne ho.

24Mmom ma nea ɔhyehyɛ ne ho nhyehyɛ ne ho sɛ

ɔwɔ nhumu, na onim sɛ,

me ne Awurade a ɔyɛ adɔe,

na obu atɛntrenee na ɔyɛ adetrenee wɔ asase so,

efisɛ eyinom na ɛsɔ mʼani,”

sɛnea Awurade se ni.

25“Nna no reba,” Awurade na ose, “A mɛtwe wɔn a wɔatwa twetia wɔ honam fam nko ara no nyinaa aso: 26Misraimfo, Yudafo, Edomfo, Amonfo, Moabfo ne wɔn a wɔtete nweatam a ɛwɔ akyirikyiri nsase so nyinaa. Na nokware, saa aman yi nyinaa yɛ momonotofo na mpo Israelfi nyinaa yɛ koma mu momonotofo.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yeremiya 9:1-26

1Aa, ndikanakonda kuti mutu wanga ukanakhala chitsime cha madzi,

ndi maso anga ngati kasupe wa misozi!

Ndikanalira usana ndi usiku

kulirira anthu anga amene aphedwa.

2Ndani adzandipatsa malo

ogona mʼchipululu

kuti ndiwasiye anthu anga

ndi kuwachokera kupita kutali;

pakuti onse ndi achigololo,

ndiponso gulu la anthu onyenga.

3“Amapinda lilime lawo ngati uta.

Mʼdzikomo mwadzaza

ndi mabodza okhaokha

osati zoonadi.

Amapitirirabe kuchita zoyipa;

ndipo sandidziwa Ine.”

Akutero Yehova.

4“Aliyense achenjere ndi abwenzi ake;

asadalire ngakhale abale ake.

Aliyense amafuna kumudyera mʼbale wake masuku pa mutu.

Choncho aliyense amachitira bwenzi lake ugogodi.

5Aliyense amamunamiza mʼbale wake

ndipo palibe amene amayankhula choonadi.

Anapazoloweza pakamwa pawo kunena zabodza;

amalimbika kuchita machimo.

6Iwe wakhalira mʼchinyengo

ndipo ukukana kundidziwa Ine,”

akutero Yehova.

7Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Taonani, Ine ndidzawasungunula ngati chitsulo ndi kuwayesa.

Kodi ndingachite nawonso

bwanji chifukwa cha machimo awo?

8Lilime lawo lili ngati muvi wakuthwa;

limayankhula zachinyengo.

Aliyense ndi pakamwa pake amayankhula mawu achikondi kwa mnansi wake,

koma mu mtima mwake amakonzekera zomuchita chiwembu.

9Kodi ndilekerenji kuwalanga chifukwa cha zimenezi?

akutero Yehova.

‘Kodi ndisawulipsire

mtundu wotere wa anthu?’ ”

10Ndidzakhetsa misozi ndi kulira kwamphamvu chifukwa cha mapiri

ndipo ndidzadandaula chifukwa cha msipu wa ku chipululu.

Malo onsewo awonongeka ndipo palibe amene amapitako,

ndipo sikumveka kulira kwa ngʼombe.

Mbalame zamlengalenga zathawa

ndipo nyama zakuthengo zachokako.

11Ndipo Yehova anati, “Ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala bwinja,

malo okhalamo ankhandwe;

ndipo ndidzawononga mizinda ya Yuda

kotero kuti palibe munthu amene adzakhalemo.”

12Ine ndinati, “Kodi munthu wanzeru ndani woti nʼkumvetsa zimenezi? Kodi ndani amene Yehova anayankhula naye zimenezi kuti akafotokozere ena? Nʼchifukwa chiyani dziko lawonongeka ndi kusanduka chipululu, mʼmene anthu sadutsamo?”

13Yehova anati, “Nʼchifukwa chakuti anthuwa analeka kutsata malamulo anga amene ndinawapatsa; sanandimvere kapena kuwasamala. 14Mʼmalo mwake, anatsatira zolakwa za mʼmitima yawo; anapembedza Abaala ngati momwe makolo awo anawaphunzitsira.” 15Tsono chimene Ine Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli ndidzachite ndi anthu amenewa ndi ichi: “Ndidzawadyetsa chakudya cha ziphe ndi kuwamwetsa madzi a ndulu. 16Ndidzawabalalitsa pakati pa mitundu ya anthu imene iwowo kapena makolo awo sanayidziwe, ndipo ndidzawalondola ndi ankhondo mpaka nditawawononga.”

17Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Tsopano ganizirani! Muyitane akazi olira mwachisoni kuti abwere;

itanani akazi odziwa kulira bwino.”

18Anthu akuti, “Abwere mofulumira

kuti adzatilire

mpaka mʼmaso mwathu mutatuluka misozi

ndi kuti msidze zathu zinyowe ndi madzi.

19Kulira mwachisoni kukumveka kuchokera mu Ziyoni akuti,

‘Aa! Ife tawonongeka!

Tachita manyazi kwambiri!

Tiyenera kuchoka mʼdziko lathu

chifukwa atipirikitsa mʼnyumba zathu.’ ”

20Tsono inu amayi, imvani mawu a Yehova;

tcherani makutu anu kuti mumve mawu a Yehova.

Phunzitsani ana anu aakazi kulira mwachisoni;

aliyense aphunzitse mnzake nyimbo ya maliro.

21Imfa yatifikira kudzera mʼmazenera athu

ndipo yalowa mʼnyumba zathu zotetezedwa;

yapha ana athu mʼmisewu,

ndi achinyamata athu mʼmabwalo.

22Yehova anandiwuza kuti ndinene izi kuti,

“ ‘Mitembo ya anthu

idzakhala ili lambalamba ngati ndowe mʼminda,

ngati mapesi mʼmbuyo mwa wokolola,

popanda munthu woyitola.’ ”

23Yehova akuti,

“Munthu wanzeru asanyadire nzeru zake,

kapena munthu wamphamvu kunyadira nyonga zake,

kapena munthu wolemera kunyadira chuma chake,

24koma ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire chinthu ichi:

kuti iye amamvetsa za Ine ndipo amandidziwa,

kuti ndine Yehova, amene ndimakonda chifundo,

chilungamo ndiponso ungwiro pa dziko lapansi.

Zimenezi ndizo ndimakondwera nazo,”

akutero Yehova.

25“Nthawi ikubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzalanga onse amene anachita mdulidwe koma mu mtima sasamala nʼkomwe. 26Ndidzalanga anthu a ku Igupto, Yuda, Edomu, Amoni, Mowabu, ndiponso onse amene amakhala kutali ku chipululu. Mitundu ina yonseyi ndi yosachita mdulidwe, ngakhalenso Aisraeli nawonso sanachite mdulidwe wa mu mtima.”