Atamfo Atwa Yerusalem Ho Ahyia
1“Benyaminfo, munguan nkɔbɔ mo ho aguaa!
Munguan mfi Yerusalem!
Monhyɛn torobɛnto no wɔ Tekoa!
Munsi frankaa no wɔ Bet-Hakerem!
Efisɛ amanehunu bobɔw fi atifi fam,
ɔsɛe bi a ɛyɛ hu.
2Mɛsɛe Ɔbabea Sion,
ɔhoɔfɛfo sɔɔnɔ no.
3Nguanhwɛfo ne wɔn nguankuw bɛba abetia no;
wobesisi wɔn ntamadan atwa ne ho ahyia,
wɔn mu biara bɛhwɛ ne kyɛfa so.”
4“Munsiesie mo ho ne no nkɔko!
Monsɔre, momma yɛnkɔtow nhyɛ ne so owigyinae!
Nanso hwɛ, onwini redwo,
na anwummere sunsuma reware.
5Enti monsɔre, momma yɛnkɔtow nhyɛ ne so anadwo
na yɛnsɛe nʼaban ahorow!”
6Nea Asafo Awurade se ni:
“Muntwitwa nnua no ngu fam
na muntwa Yerusalem ho dantaban.
Ɛsɛ sɛ wɔtwe kuropɔn yi aso;
nhyɛso ahyɛ no ma.
7Sɛnea abura puw ne nsu no,
saa ara na opuw nʼamumɔyɛ.
Wɔte awurukasɛm ne ɔsɛe nka wɔ ne mu;
ne yare ne nʼapirakuru wɔ mʼanim daa.
8Fa kɔkɔbɔ, Yerusalem,
anyɛ saa metwe me ho afi wo ho
na mama wʼasase ada mpan
a obiara ntumi ntena so.”
9Nea Asafo Awurade se ni:
“Ma wonyiyi Israel nkae no mu yiye
sɛnea woyiyi bobe mu yiye no;
fa wo nsa fa mman no so bio,
sɛ obi a ɔretetew bobe aba.”
10Hena na metumi akasa akyerɛ no na mabɔ no kɔkɔ?
Hena na obetie me?
Wɔn aso asisiw
enti wɔnte asɛm.
Awurade asɛm yɛ akyiwade ma wɔn,
na wɔn ani nnye ho.
11Nanso Awurade abufuwhyew ahyɛ me ma,
na mintumi nkora so.
“Hwie gu mmofra a wɔwɔ mmɔnten so
ne mmerante a wɔahyia;
ɛbɛka okunu ne ɔyere,
mmasiriwa, wɔn a onyin ahunhuan wɔn no so.
12Wɔbɛdan wɔn afi ama afoforo,
wɔn mfuw ne wɔn yerenom bɛka ho;
sɛ meteɛ me nsa
wɔ wɔn a wɔte asase no so a,”
sɛnea Awurade se ni.
13“Efi akumaa so kosi ɔkɛse so,
wɔn nyinaa yɛ adifudepɛfo de pɛ ahonya;
adiyifo ne asɔfo te saa,
wɔn nyinaa yɛ asisifo.
14Wɔtoto me nkurɔfo apirakuru
te sɛnea ɛnyɛ hu.
Wɔka se, ‘Asomdwoe, asomdwoe’
wɔ mmere a asomdwoe nni hɔ.
15Wɔn ani wu wɔ wɔn animguase nneyɛe no ho ana?
Dabi da, wɔn ani nnwu koraa;
wonnim fɛre mpo.
Enti wɔbɛtotɔ wɔ atɔfo mu;
wɔbɛhwehwe ase, sɛ metwe wɔn aso a,”
sɛnea Awurade se ni.
16Eyi ne nea Awurade se,
“Munnyina nkwantanan no so na monhwɛ;
mummisa tete akwan no,
mummisa faako a ɔkwan pa no da na monnantew so,
na mubenya home ama mo akra.
Nanso mokae se, ‘yɛnnantew so.’
17Mede awɛmfo sisii mo so na mekae se,
‘Muntie torobɛnto nnyigyei no!’
Nanso mokae se, ‘Yɛrentie.’
18Ɛno nti monyɛ aso, mo amanaman;
mo a moyɛ nnansefo, monhwɛ,
monhwɛ nea ɛbɛto wɔn.
19Tie, wo asase:
Mede amanehunu reba saa nnipa yi so,
wɔn nneyɛe so aba,
efisɛ wɔantie me nsɛm
na wɔapo me mmara.
20Nnuhuam a efi Seba
anaa ahwerew pa a efi akyirikyiri asase so fa me ho bɛn?
Minnye wo hyew afɔre no nto mu,
wʼafɔrebɔ ahorow no nsɔ mʼani.”
21Ɛno nti, nea Awurade se ni:
“Mede akwanside begu saa nkurɔfo yi anim.
Agyanom ne mmabarima nyinaa behintiw wɔ so;
yɔnkonom ne nnamfonom bɛyera.”
22Sɛnea Awurade se ni:
“Monhwɛ, nsraadɔm bi reba,
wofi atifi fam asase so;
wɔrehwanyan wɔn
afi nsase ano.
23Wokurakura bɛmma ne mpeaw;
wɔn tirim yɛ den, na wonni ahummɔbɔ.
Wɔn nnyigyei te sɛ po asorɔkye.
Sɛ wɔtete wɔn apɔnkɔ so a,
wɔba te sɛ mmarima a wɔrekɔ ɔko.
Wɔrebɛtow ahyɛ wo so, Ɔbabea Sion.”
24Yɛate wɔn ho nsɛm,
na yɛn nsa sesa yɛn ho sɛ nea awuwu.
Awerɛhow akyekyere yɛn
yɛte yaw sɛ ɔbea a ɔreko awo.
25Mfi adi nkɔ wuram
na nnantew akwan no so,
efisɛ ɔtamfo no wɔ afoa,
na baabiara ayɛ hu.
26Me nkurɔfo, mumfura atweaatam
na mommunummunum wɔ nsõ mu,
momfa adwadwotwa yaayaw nni awerɛhow
sɛnea wosu ma ɔbabarima koro,
efisɛ ɔsɛefo no
bɛba yɛn so mpofirim.
27“Mayɛ wo obi a ɔsɔ agude hwɛ
na me nkurɔfo dadeben,
a wobɛhwɛ
na woasɔ wɔn akwan ahwɛ.
28Wɔn nyinaa yɛ atuatewfo a wɔyɛ den,
wɔnenam di nseku.
Wɔyɛ kɔbere ne dade;
wɔn nyinaa yɛ wɔn ade wɔ porɔwee kwan so.
29Afa no bɔ mframa dennen
de ogya nan sumpii no,
nanso ɔnan no yɛ ɔkwa.
Entumi nyiyii bɔne no mfii wɔn mu ɛ.
30Wɔfrɛ wɔn dwetɛ a wɔapo,
efisɛ Awurade apo wɔn.”
Kuzingidwa kwa Yerusalemu
1“Thawani, inu anthu a ku Benjamini!
Tulukani mu Yerusalemu!
Lizani lipenga ku Tekowa!
Kwezani mbendera ku Beti-Hakeremu!
Pakuti tsoka lalikulu likubwera kuchokera kumpoto,
ndipo chiwonongekocho nʼchachikulu.
2Kodi mzinda wa Ziyoni suli ngati msipu wokongola kwambiri,
kumene abusa amafikako ndi ziweto zawo?
3Abusa ndi nkhosa zawo adzabwera kudzalimbana nawo;
adzamanga matenti awo mowuzinga,
ndipo aliyense adzakhazika anthu ake pamalo pake.”
4Adzanena kuti, “Konzekani kuwuthira nkhondo mzindawo!
Nyamukani, kuti tiwuthire nkhondo mzindawu masana ano.
Koma tili ndi tsoka, dzuwa lapendeka,
ndipo zithunzithunzi za kumadzulo zikunka zitalika.
5Tsono nyamukani kuti tiwuthire nkhondo mzindawu usiku uno
ndi kuwononga malinga ake!”
6Yehova Wamphamvuzonse akuti,
“Dulani mitengo
ndipo mumange mitumbira yankhondo kulimbana ndi Yerusalemu.
Mzinda umenewu uyenera kulangidwa;
wadzaza ndi kuponderezana.
7Monga momwe chitsime chimatulutsira madzi
ndi mmenenso Yerusalemu amatulutsira zoyipa zake.
Chiwawa ndi chiwonongeko ndi zomwe zimamveka mu mzindamo;
nthenda yake ndi mabala ake ndimaziona nthawi zonse.
8Iwe Yerusalemu, tengapo phunziro,
kuopa kuti chikondi changa pa iwe chingakuchokere
ndi kusandutsa dziko lako kukhala bwinja
mopanda munthu wokhalamo.”
9Yehova Wamphamvuzonse anandiwuza kuti,
“Adani adzawakunkha ndithu anthu otsala a Israeli,
monga momwe amachitira populula mphesa.
Tsono iwe yesetsa kupulumutsa amene ungathe
monga mmene amachitira munthu wokolola mphesa.”
10Kodi ndiyankhule ndi yani ndi kumuchenjeza?
Ndinene mawu ochenjeza kwa yani kuti amve?
Makutu awo ndi otsekeka
kotero kuti sangathe kumva.
Mawu a Yehova ndi onyansa kwa iwo;
sasangalatsidwa nawo.
11Koma ine ndadzazidwa ndi mkwiyo wa Yehova,
ndipo ndatopa ndi kusunga mkwiyo wa Yehova.
Yehova anandiwuza kuti, “Tsono ndidzawutulutsira mkwiyo umenewu pa ana oyenda mʼmisewu
ndi pa achinyamata amene asonkhana pamodzi;
pakutinso mwamuna ndi mkazi wake adzatengedwa,
pamodzi ndi okalamba amene ali ndi zaka zochuluka.
12Nyumba zawo adzazipereka kwa ena,
pamodzi ndi minda yawo ndi akazi awo.
Ndidzatambasula dzanja langa kukantha
anthu okhala mʼdzikomo,”
akutero Yehova.
13“Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu,
onse ali ndi dyera lofuna kupeza phindu mwa kuba;
aneneri pamodzi ndi ansembe omwe,
onse amachita zachinyengo.
14Amapoletsa zilonda za anthu anga
pamwamba pokha.
Iwo amanena kuti, ‘Mtendere, mtendere,’
pamene palibe mtendere.
15Kodi amachita manyazi akamachita zonyansazo?
Ayi, sachita manyazi ndi pangʼono pomwe;
sadziwa ndi kugwetsa nkhope komwe.
Choncho iwo adzagwera pakati pa anzawo amene agwa kale;
adzagwa pansi tsiku limene ndidzawalange,”
akutero Yehova.
16Yehova akuti,
“Imani pa mphambano ndipo mupenye;
kumeneko ndiye kuli njira zakale,
funsani kumene kuli njira yabwino. Yendani mʼmenemo,
ndipo mudzapeza mpumulo wa miyoyo yanu.
Koma inu munati, ‘Ife sitidzayenda njira imeneyo.’
17Ine ndinakupatsani alonda oti akuyangʼanireni
ndipo ndinati, ‘Imvani kulira kwa lipenga!’
koma inu munati, ‘Sitidzamvera.’
18Nʼchifukwa chake imvani, inu anthu a mitundu ina;
yangʼanitsitsani, inu amene mwasonkhana pano,
chimene chidzawachitikire anthuwo.
19Imvani, inu anthu okhala pa dziko lapansi,
ndikubweretsa masautso pa anthu awa.
Zimenezi ndi mphotho ya ntchito zawo.
Iwowa sanamvere mawu anga
ndipo anakana lamulo langa.
20Kodi pali phindu lanji ngakhale mubwere ndi lubani kuchokera ku Seba,
kapena zonunkhira zina kuchokera ku dziko lakutali?
Nsembe zanu zopsereza Ine sindidzalandira;
nsembe zanu sizindikondweretsa.”
21Choncho Yehova akuti,
“Ndidzayika zokhumudwitsa pamaso pa anthu awa.
Abambo ndi ana awo aamuna onse adzapunthwa ndi kugwa;
anansi awo ndi abwenzi awo adzawonongeka.”
22Yehova akunena kuti,
“Taonani, gulu lankhondo likubwera
kuchokera kumpoto;
mtundu wa anthu amphamvu wanyamuka
kuchokera kumathero a dziko lapansi.
23Atenga mauta ndi mikondo;
ndi anthu ankhanza ndi opanda chifundo.
Phokoso lawo lili ngati mkokomo wa nyanja.
Akwera pa akavalo awo
ndipo akonzekera ngati anthu ankhondo,
kudzakuthirani nkhondo anthu a ku Ziyoni.”
24A ku Ziyoni akuti “Ife tamva mbiri yawo,
ndipo manja anthu alefukiratu.
Nkhawa yatigwira,
ndipo tikumva ululu ngati mayi pa nthawi yake yochira.
25Musapite ku minda
kapena kuyenda mʼmisewu,
pakuti mdani ali ndi lupanga,
ndipo ponseponse anthu akuchita mantha.
26Inu anthu anga, valani ziguduli
ndipo gubudukani pa phulusa;
lirani mwamphamvu
ngati munthu wolirira mwana wake mmodzi yekha,
pakuti mwadzidzidzi wowonongayo
adzabwera kudzatipha.
27“Iwe Yeremiya, ndakuyika kuti ukhale choyesera zitsulo.
Uwayese anthu anga
monga ungayesere chitsulo
kuti uwone makhalidwe awo.
28Onsewo ali ndi khalidwe lokanika ndi lowukira
ndipo akunka nanena zamiseche.
Iwo ndi olimba ngati mkuwa ndi chitsulo.
Onse amangochita zoyipa zokhazokha.
29Moto mu mvukuto ukuyaka kwambiri;
mtovu watha kusungunuka ndi moto.
Koma ntchito yosungunulayo sikupindula
chifukwa zoyipa sizikuchokapo.
30Iwo ali ngati siliva wotayidwa,
chifukwa Yehova wawakana.”