Nnwom 94 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom 94:1-23

Dwom 94

1Awurade, Onyankopɔn a wotɔ were,

Onyankopɔn a wotɔ were, hyerɛn.

2Sɔre, asase so Temmufo,

tua ahantanfo ka sɛnea ɛfata wɔn.

3Awurade, enkosi da bɛn,

amumɔyɛfo nnye wɔn ani nkosi da bɛn?

4Wɔkasa ahantan so;

ahohoahoa ahyɛ abɔnefo nyinaa ma.

5Awurade, wɔdwerɛw wo nkurɔfo;

wɔhyɛ wʼagyapade so.

6Wokunkum akunafo ne ananafo;

na wodi ayisaa awu.

7Wɔka se, “Awurade nhu,

Yakob Nyankopɔn ayi nʼani.”

8Monhwɛ yiye, mo agyimifo a mowɔ nnipa no mu;

nkwaseafo, da bɛn na mubehu nyansa?

9Nea ɔbɔɔ aso no rente asɛm ana?

Nea ɔyɛɛ ani no renhu ade ana?

10Nea ɔteɛteɛ aman so no rentwe aso ana?

Nea ɔkyerɛkyerɛ onipa no nnim nyansa ana?

11Awurade nim onipa nsusuwii;

onim sɛ enkosi hwee.

12Awurade, nhyira ne onipa a woteɛteɛ no so,

onipa a wokyerɛ no wo mmara no;

13Woma ɔhome fi amanehunu nna mu,

kosi sɛ wobetu amoa ama amumɔyɛfo.

14Awurade rempo ne nkurɔfo;

na ɔrennyaw nʼagyapade hɔ da.

15Atemmu begyina treneeyɛ so bio,

na wɔn a wɔn koma mu tew nyinaa bedi so.

16Hena na ɔbɛsɔre atia amumɔyɛfo ama me?

Hena na ɔbɛsɔre atia abɔnefo ama me?

17Awurade ammoa me a,

anka mekɔɔ owu kommyɛ mu ntɛm so.

18Bere a mekae se, “Me nan rewatiri” no,

Awurade, wo dɔ no soo me mu.

19Bere a me dadwen dɔɔso no,

wʼawerɛkyekye maa me kra abotɔyam.

20Ahengua a porɔwee ahyɛ no mma no ne wo wɔ ayɔnkofa ana?

Ahengua a ne hyɛ nsɛm de amanehunu na ɛba no?

21Wɔka bɔ mu tia atreneefo

na wɔn a wodi bem no, wobu wɔn kumfɔ.

22Nanso Awurade yɛ mʼaban;

na me Nyankopɔn ayɛ ɔbotan a ne mu na minya ahintawee.

23Obetua wɔn nnebɔne no so ka

na wɔn amumɔyɛ nti wasɛe wɔn;

Awurade yɛn Nyankopɔn bɛsɛe wɔn.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 94:1-23

Salimo 94

1Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango,

Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.

2Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi;

bwezerani kwa odzikuza zowayenera.

3Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova,

mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?

4Amakhuthula mawu onyada;

onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.

5Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova;

amapondereza cholowa chanu.

6Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko;

amapha ana amasiye.

7Iwo amati, “Yehova sakuona;

Mulungu wa Yakobo salabadirako.”

8Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu;

zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?

9Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva?

Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?

10Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga?

Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?

11Yehova amadziwa maganizo a munthu;

Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.

12Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza,

munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;

13mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto,

mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.

14Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake;

Iye sadzasiya cholowa chake.

15Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo,

ndipo onse olungama mtima adzachitsata.

16Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa?

Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?

17Yehova akanapanda kundithandiza,

bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.

18Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,”

chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.

19Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga,

chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.

20Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu

umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?

21Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama

ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.

22Koma Yehova wakhala linga langa,

ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.

23Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo

ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo;

Yehova Mulungu wathu adzawawononga.