Nnwom 71 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom 71:1-24

Dwom 71

1Awurade, wo mu na maguan ahintaw;

mma mʼanim ngu ase da.

2Wo trenee no nti, yi me na gye me;

tie me na gye me nkwa.

3Yɛ me nkwagye botan,

faako a metumi akɔ daa;

hyɛ ma wommegye me nkwa,

na wone me botan ne mʼabandennen.

4Me Nyankopɔn, gye me fi amumɔyɛfo nsam,

gye me fi nnebɔneyɛfo ne atirimɔdenfo nsam.

5Na woayɛ mʼanidaso, Asafo Awurade,

mʼahotoso fi me mmabun bere mu.

6Mede me ho ato wo so fi awo mu;

wo na wuyii me fii me na yafunu mu.

Mɛkamfo wo daa.

7Mayɛ nsɛnkyerɛnne ama bebree,

nanso wo ne me guankɔbea dennen.

8Wo nkamfo ahyɛ mʼanom ma,

mekamfo wʼanuonyam da mu nyinaa.

9Ntow me nkyene bere a mabɔ akwakoraa;

mʼahoɔden sa wɔ me mu a, nnyaw me.

10Efisɛ mʼatamfo kasa tia me

wɔn a wɔtwɛn sɛ wobekum me no bɔ mu pam me ti so.

11Wɔka se, “Onyankopɔn agyaw no mu;

momma yentiw no na yɛnkyere no,

na obiara nni hɔ a obegye no.”

12Me Nyankopɔn, mfi me nkyɛn nkɔ akyiri;

Onyankopɔn, yɛ ntɛm bɛboa me.

13Ma wɔn a wɔbɔ me sobo no nsɛe wɔ animguase mu;

wɔn a wɔpɛ sɛ wopira me no

ma ahohora ne animguase nkata wɔn so.

14Nanso me de, menya anidaso daa;

mɛkɔ so akamfo wo.

15Mɛka wo trenee ho asɛm,

ne wo nkwagye da mu nyinaa,

nanso minnim ano.

16Otumfo Awurade, mɛba abɛpae mu aka wo nnwuma akɛse no;

mɛpae mu aka wo trenee, wo nko ara de no, akyerɛ.

17Onyankopɔn, efi me mmabun bere na wokyerɛkyerɛɛ me,

na ebesi nnɛ yi meka wʼanwonwade a woayɛ kyerɛ.

18Mpo sɛ mebɔ akwakoraa na mifuw dwen a,

Onyankopɔn, nnyaw me,

kosi sɛ mɛka wo tumi ho asɛm akyerɛ nkyirimma,

ne wo kɛseyɛ akyerɛ wɔn a wɔbɛba nyinaa.

19Onyankopɔn, wo trenee du ɔsorosoro,

wo a woayɛ nneɛma akɛse.

Onyankopɔn, hena na ɔte sɛ wo?

20Mmom woama mahu ɔhaw bebree a ɛyɛ yaw;

nanso wobɛma me nkwa bio;

na wubeyi me bio,

afi asase yam.

21Wobɛhyɛ me anuonyam bebree

na woakyekye me werɛ bio.

22Mede sanku bɛkamfo wo

me Nyankopɔn, wo trenee nti

mɛto wʼayeyi dwom wɔ sankuten so,

Israel Kronkronni.

23Mʼanofafa de anigye bɛteɛ mu

bere a meto dwom kamfo wo,

me a woagye me no.

24Me tɛkrɛma bɛka wo trenee nnwuma

da mu nyinaa,

efisɛ wɔn a wɔpɛ sɛ wɔhaw me no

kɔ animguase ne basaayɛ mu.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 71:1-24

Salimo 71

1Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo;

musalole kuti ndichititsidwe manyazi.

2Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu,

mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.

3Mukhale thanthwe langa lothawirapo,

kumene ine nditha kupita nthawi zonse;

lamulani kuti ndipulumuke,

pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.

4Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa,

kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.

5Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse,

chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.

6Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu;

Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga,

ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.

7Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri

koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.

8Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu,

kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.

9Musanditaye pamene ndakalamba;

musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.

10Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane;

iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.

11Iwo amati, “Mulungu wamusiya;

mutsatireni ndi kumugwira,

pakuti palibe amene adzamupulumutse.”

12Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu,

bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.

13Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi,

iwo amene akufuna kundipweteka

avale chitonzo ndi manyazi.

14Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse,

ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.

15Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu,

za chipulumutso chanu tsiku lonse,

ngakhale sindikudziwa muyeso wake.

16Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse.

Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.

17Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa,

ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa

18Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu

musanditaye Inu Mulungu,

mpaka nditalengeza mphamvu zanu

kwa mibado yonse yakutsogolo.

19Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba.

Ndani wofanana nanu Inu Mulungu,

amene mwachita zazikulu?

20Ngakhale mwandionetsa mavuto

ambiri owawa,

mudzabwezeretsanso moyo wanga;

kuchokera kunsi kwa dziko lapansi,

mudzandiukitsanso.

21Inu mudzachulukitsa ulemu wanga

ndi kunditonthozanso.

22Ndidzakutamandani ndi zeze

chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu,

ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe,

Inu Woyera wa Israeli.

23Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe

pamene ndidzayimba matamando kwa Inu

amene mwandiwombola.

24Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo

tsiku lonse,

pakuti iwo amene amafuna kundipweteka

achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.