Nnwom 69 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom 69:1-36

Dwom 69

Dawid dwom.

1Ao, Onyankopɔn, gye me nkwa

na nsu no abɛdeda me kɔn mu.

2Meremem wɔ dontori a mu dɔ mu,

wɔ baabi a mʼanan nnya sibea.

Madu bun mu

na nsu abu afa me so.

3Mafrɛ abrɛ rehwehwɛ mmoa.

Me mene mu ayow.

Mʼani so ayɛ kusuu,

na merehwehwɛ me Nyankopɔn.

4Wɔn a wɔtan me kwa no

dɔɔso sen me ti so nwi;

wɔn a wɔtan me kwa no dɔɔso,

wɔn a wɔhwehwɛ sɛ wɔbɛsɛe me no.

Wɔhyɛ me sɛ mennan

nea minnwiae no mma.

5Wo, Onyankopɔn, nim me nkwaseasɛm;

mʼafɔdi nhintaw wo.

6Awurade, Awurade Tweduampɔn,

mma wɔn a wɔn ani da wo so no,

anim ngu ase esiane me nti, Awurade, Asafo Awurade;

Israel Nyankopɔn,

mma wɔn a wɔhwehwɛ wo no

anim ngu ase esiane me nti.

7Wo nti migyina animka ano,

na aniwu kata mʼanim.

8Mete sɛ ɔhɔho wɔ me nuanom mu,

mete sɛ ɔmamfrani wɔ me na mmabarima mu,

9na wo fi ho mmɔdemmɔ hyɛ me so,

wɔn a wɔbɔ wo ahohora no animtiaabu bɛda me so.

10Sɛ mitwa adwo na midi mmuada a

wɔbɔ me ahohora;

11sɛ mifura atweaatam a

nnipa de me yɛ aserewde.

12Wɔn a wɔtete ɔpon no ano no serew me,

na akɔwensafo de me din to dwom.

13Nanso mɛbɔ wo mpae, Awurade,

wɔ wʼadom bere mu;

wɔ wʼadɔe kɛse no nti, Ao, Onyankopɔn,

fa wo nokware nkwagye no gye me so.

14Yi me fi dontori no mu,

mma memmem wɔ mu;

gye me fi wɔn a wɔtan me no nsam,

ne nsu bun mu.

15Mma nsu nnyiri mmfa me

anaa bun mmene me

anaa amoa nkata me so.

16Awurade, gye me so fi wʼadɔe a eye no mu;

wʼadom nti, dan bɛhwɛ me.

17Mfa wʼanim nhintaw wo somfo;

gye me so ntɛm, na mewɔ ɔhaw mu.

18Twiw bɛn me na gye me;

gye me nkwa, mʼatamfo nti.

19Wunim sɛnea wɔkasa tia me, gu mʼanim ase na wotiatia mʼanim;

wʼani tua mʼatamfo nyinaa.

20Kasatia ahyɛ me koma so

ama mayɛ sɛ obi a onni ɔboafo;

mepɛɛ awerɛkyekye, nanso mannya bi,

mepɛɛ ɔwerɛkyekyefo, nanso manhu bi.

21Wɔde bɔnwoma guu mʼaduan mu,

osukɔm dee me no, wɔmaa me nsa nwenweenwen.

22Ma wɔn didipon a esi wɔn anim nyi wɔn sɛ afiri;

ma ɛnyɛ akatua ne afide mma wɔn.

23Ma wɔn ani so nyɛ wɔn kusuu na wɔanhu ade,

na ma wɔn akyi nkuntun afebɔɔ.

24Hwie wʼabufuwhyew gu wɔn so;

na ma wʼabufuw huhuhuhu no mmra wɔn so.

25Ma wɔn fi nyɛ amamfo;

mma obiara ntena wɔn ntamadan mu.

26Wɔtaa wɔn a wupira wɔn no,

wɔka wɔn a wupira wɔn no yawdi ho asɛm.

27Fa amumɔyɛ mu amumɔyɛ ho sobo bɔ wɔn;

mma wonnya wo nkwagye mu kyɛfa.

28Pepa wɔn din fi nkwa nhoma no mu,

mfa wɔn din nka atreneefo de ho.

29Mewɔ ɔyaw ne ahohiahia mu;

Onyankopɔn, ma wo nkwagye no mmɔ me ho ban.

30Mede dwonto beyi Onyankopɔn din ayɛ

na mede aseda ahyɛ no anuonyam.

31Eyi bɛsɔ Awurade ani yiye asen nantwi,

asen nantwinini a otua mmɛn na ɔwɔ tɔte.

32Mmɔborɔni behu na nʼani agye,

mo a mohwehwɛ Onyankopɔn no koma benya nkwa.

33Awurade tie wɔn a ade ahia wɔn,

na ommu ne nkurɔfo nneduafo animtiaa.

34Ma ɔsoro ne asase nkamfo no,

po ne nea ɛkeka ne ho wɔ mu nyinaa,

35efisɛ Onyankopɔn begye Sion nkwa

na wakyekye Yuda nkuropɔn no bio.

Afei nnipa bɛtena mu na ayɛ wɔn de;

36Nʼasomfo asefo na wɔbɛfa hɔ,

na wɔn a wɔdɔ ne din no bɛtena hɔ.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 69:1-36

Salimo 69

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Potsata mayimbidwe a “Akakombo.”

1Pulumutseni Inu Mulungu,

pakuti madzi afika mʼkhosi

2Ine ndikumira mʼthope lozama

mʼmene mulibe popondapo.

Ndalowa mʼmadzi ozama;

mafunde andimiza.

3Ndafowoka ndikupempha chithandizo;

kummero kwanga kwawuma gwaa,

mʼmaso mwanga mwada

kuyembekezera Mulungu wanga.

4Iwo amene amadana nane popanda chifukwa

ndi ochuluka kuposa tsitsi la kumutu kwanga;

ambiri ndi adani anga popanda chifukwa,

iwo amene akufunafuna kundiwononga.

Ndikukakamizidwa kubwezera

zomwe sindinabe.

5Mukudziwa uchitsiru wanga, Inu Mulungu,

kulakwa kwanga sikuli kobisika kwa Inu.

6Iwo amene amadalira Inu

asanyozedwe chifukwa cha ine,

Inu Ambuye Wamphamvuzonse.

Iwo amene amafunafuna Inu

asachititsidwe manyazi chifukwa cha ine,

Inu Mulungu wa Israeli.

7Pakuti ndimapirira kunyozedwa chifukwa cha Inu,

ndipo manyazi amaphimba nkhope yanga.

8Ndine mlendo kwa abale anga,

munthu wakudza kwa ana aamuna a amayi anga;

9pakuti changu chochitira nyumba yanu chandiphetsa

ndipo chipongwe cha iwo amene amanyoza Inu chandigwera.

10Pamene ndikulira ndi kusala kudya,

ndiyenera kupirira kunyozedwa;

11pomwe ndavala chiguduli,

anthu amandiseweretsa.

12Iwo amene amakhala pa chipata amandinena,

ndipo ine ndine nyimbo ya zidakwa.

13Koma ndikupempha kwa Inu Ambuye,

pa nthawi yanu yondikomera mtima;

mwa chikondi chanu chachikulu

Inu Mulungu, mundiyankhe pondipulumutsa.

14Mundilanditse kuchoka mʼmatope,

musalole kuti ndimire,

pulumutseni ine kwa iwo

amene amadana nane, kuchoka mʼmadzi ozama.

15Musalole kuti chigumula chindimeze,

kuya kusandimeze

ndipo dzenje lisatseke pakamwa pake kundimiza.

16Ndiyankheni Inu Yehova mwa ubwino wanu wa chikondi chanu;

mwa chifundo chanu chachikulu tembenukirani kwa ine.

17Musabisire nkhope yanu mtumiki wanu,

ndiyankheni msanga, pakuti ndili pa mavuto.

18Bwerani pafupi ndi kundilanditsa;

ndiwomboleni chifukwa cha adani anga.

19Inu mukudziwa momwe ndanyozedwera,

kunyozedwa ndi kuchititsidwa manyazi; adani anga onse ali pamaso panu.

20Mnyozo waswa mtima wanga

ndipo wandisiya wopanda thandizo lililonse;

ndinafunafuna ena woti andichitire chisoni,

koma panalibe ndi mmodzi yemwe woti anditonthoze, sindinapeze ndi mmodzi yemwe.

21Iwo anayika ndulu mʼchakudya changa

ndi kundipatsa vinyo wosasa chifukwa cha ludzu.

22Chakudya chomwe chayikidwa patsogolo pawo chikhale msampha;

chikhale chobwezera chilango ndiponso khwekhwe.

23Maso awo adetsedwe kotero kuti asaonenso

ndipo misana yawo ipindike mpaka kalekale.

24Khuthulirani ukali wanu pa iwo;

mkwiyo wanu woyaka moto uwathe mphamvu.

25Malo awo akhale wopanda anthu

pasapezeke ndi mmodzi yemwe wokhala mʼmatenti awo.

26Pakuti iwo amazunza amene inu munamuvulaza

ndi kuyankhula zowawa kwa amene munawapweteka.

27Awonjezereni kulakwa pa kulakwa kwawo,

musalole kuti akhale ndi gawo pa chipulumutso chanu.

28Iwo afufutidwe mʼbuku la amoyo

ndipo asalembedwe pamodzi ndi olungama.

29Ndikumva zowawa ndi kuzunzika;

lolani chipulumutso chanu, Inu Mulungu, chinditeteze.

30Ine ndidzatamanda dzina la Mulungu mʼnyimbo,

ndidzalemekeza Iye ndi chiyamiko.

31Izi zidzakondweretsa Yehova kupambana ngʼombe,

kupambananso ngʼombe yayimuna, pamodzi ndi nyanga ndi ziboda zake.

32Wosauka adzaona ndipo adzasangalala,

Inu amene mumafunafuna Mulungu, mitima yanu ikhale ndi moyo!

33Yehova amamvera anthu osowa

ndipo sanyoza anthu ake omangidwa.

34Kumwamba ndi dziko lapansi zitamanda Iye,

nyanja ndi zonse zomwe zimayenda mʼmenemo,

35pakuti Mulungu adzapulumutsa Ziyoni

ndi kumanganso mizinda ya Yuda,

anthu adzakhala kumeneko ndipo dzikolo lidzakhala lawo;

36ana atumiki ake adzalitenga kukhala cholowa chawo,

ndipo iwo amene amakonda dzina lake adzakhala kumeneko.