Nnwom 62 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom 62:1-12

Dwom 62

Dawid dwom.

1Me kra wɔ ahomegye wɔ Onyankopɔn nko ara mu;

me nkwagye fi ne nkyɛn.

2Ampa, ɔyɛ me botan ne me nkwagye;

ɔyɛ mʼabandennen, hwee renhinhim me da.

3Mobɛkɔ so ahyɛ onipa so akosi da bɛn,

mo nyinaa besum me ahwe fam ana?

Ɔfasu a akyea yi, ban a ɛrebu yi?

4Ampa, wɔayɛ adwene se wobetu no

afi ne dibea a ɛkorɔn no so;

wɔn ani gye atorodi ho.

Wɔde wɔn ano hyira

na wɔn koma mu de, wɔdome.

5Yiw me kra, gye wʼahome wɔ Onyankopɔn nko ara mu;

na ne mu na mʼanidaso wɔ.

6Ampa, ɔyɛ me botan ne me nkwagye;

ɔyɛ mʼabandennen, hwee renhinhim me.

7Me nkwagye ne mʼanuonyam gyina Onyankopɔn so;

ɔyɛ me botan a ɛkorɔn, ne me guankɔbea.

8Mo nnipa, momfa mo ho nto ne so daa;

monka mo koma mu nsɛm nyinaa nkyerɛ no,

efisɛ Onyankopɔn ne yɛn guankɔbea.

9Nnipa nyinaa te sɛ home;

akɛse ne nkumaa nyinaa nka hwee;

sɛ wɔkari wɔn wɔ nsania so a, wɔnka hwee;

wɔn nyinaa bɔ mu a wɔyɛ home nko.

10Mommfa mo ho nto asisi so

na monnhoahoa mo ho akorɔnne ho;

ɛwɔ mu sɛ mo ahonya dɔɔso de,

nanso mommfa mo koma nto so.

11Asɛm baako na Onyankopɔn aka,

nsɛm abien na mate sɛ,

wo, Onyankopɔn, na wowɔ ahoɔden,

12na wo, Awurade, na woyɛ adɔe,

ampa ara wubetua obiara ka

sɛnea nʼadwuma te.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 62:1-12

Salimo 62

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide.

1Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha;

chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.

2Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;

Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.

3Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti?

Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba,

ngati mpanda wogwedezeka?

4Iwo akufunitsitsa kumugwetsa

kuti achoke pa malo ake apamwamba.

Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza.

Ndi pakamwa pawo amadalitsa

koma mʼmitima yawo amatemberera.

5Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga;

chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.

6Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;

Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.

7Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu:

Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.

8Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu;

khuthulani mitima yanu kwa Iye,

pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu.

Sela

9Anthu wamba ndi mpweya chabe;

anthu apamwamba ndi bodza chabe;

ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe;

iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe

10Musadalire kulanda mwachinyengo

kapena katundu wobedwa;

ngakhale chuma chanu chichuluke,

musayike mtima wanu pa icho.

11Mulungu wayankhula kamodzi,

ine ndamvapo zinthu ziwiri;

choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,

12komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika.

Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu

molingana ndi ntchito zake.