Nnwom 39 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom 39:1-13

Dwom 39

Dawid dwom.

1Mekae se, “Mɛhwɛ mʼakwan yiye

na mamfa me tɛkrɛma anyɛ bɔne;

mɛto mʼano nnareka

bere a amumɔyɛfo bɛn me yi.

2Enti meyɛɛ komm

a manka asɛm papa biara mpo

nanso mʼapinisi mu yɛɛ den.

3Me koma ho guan no wɔ me mu.

Midwinnwen no, ogya dɛwee;

afei mede me tɛkrɛma kasae se:

4Awurade, ma minhu me nkwa awiei

ne me nna dodow;

ma minhu sɛnea me nkwa si twa mu ntɛm so.

5Woayɛ me nna sɛ nsateaa baako pɛ;

na me mfe dodow nyɛ hwee wɔ wʼani so.

Onipa nkwa yɛ ɔhome bi kɛkɛ.

6Onipa redi akɔneaba nyinaa no, ɔte sɛ sunsuma bi kwa;

ɔhaw ne ho nanso ɔyɛ kwa;

ɔboa ahonya ano na onnim nea ɛbɛyɛ ne de.

7“Afei Awurade, dɛn na merehwehwɛ?

Mʼanidaso wɔ wo mu.

8Gye me fi me bɔne nyinaa mu;

mma mennyɛ nkwaseafo aserewde.

9Meyɛɛ komm, na mammue mʼano,

efisɛ wo na woayɛ eyi.

10Yi wʼasotwe fi me so;

wo nsa ano amanehunu amene me.

11Woka nnipa anim, na wotwe wɔn aso wɔ wɔn bɔne ho;

wosɛe wɔn ahonya te sɛ nwewee;

onipa biara yɛ ɔhome kɛkɛ.

12Awurade, tie me mpaebɔ,

tie me sufrɛ;

nsiw wʼaso wɔ me su ho.

Me ne wo te hɔ sɛ ɔnanani,

sɛnea na mʼagyanom nyinaa te no.

13Yi wʼani fi me so na manya nkwa bio,

ansa na mafi ha a mente ase bio.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 39:1-13

Salimo 39

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kwa Yedutuni. Salimo la Davide.

1Ndinati, “Ndidzasamalira njira zanga

ndipo ndidzasunga lilime langa kuti ndisachimwe;

ndidzatseka pakamwa panga ndi chitsekerero

nthawi yonse imene woyipa ali pamaso panga.”

2Koma pamene ndinali chete

osanena ngakhale kanthu kalikonse kabwino

mavuto anga anachulukirabe.

3Mtima wanga unatentha mʼkati mwanga,

ndipo pamene ndinkalingalira, moto unayaka;

kenaka ndinayankhula ndi lilime langa:

4“Yehova ndionetseni mathero a moyo wanga

ndi chiwerengero cha masiku anga;

mundidziwitse kuti moyo wanga ndi wosakhalitsa motani.

5Inu mwachititsa kuti masiku anga akhale ochepa kwambiri,

kutalika kwa zaka zanga ndi kopanda phindu pamaso panu;

moyo wa munthu aliyense ndi waufupi.

Sela

6Munthu ali ngati chithunzithunzi chake pamene akuyenda uku ndi uku:

Iye amangovutika koma popanda phindu;

amadzikundikira chuma, osadziwa kuti chidzakhala chayani.

7“Koma tsopano Ambuye kodi ndifunanso chiyani?

Chiyembekezo changa chili mwa Inu.

8Pulumutseni ku zolakwa zanga zonse;

musandisandutse chonyozeka kwa opusa.

9Ine ndinali chete; sindinatsekule pakamwa panga

pakuti Inu ndinu amene mwachita zimenezi.

10Chotsani mkwapulo wanu pa ine;

ndagonjetsedwa ndi nkhonya ya dzanja lanu.

11Inu mumadzudzula ndi kulanga anthu chifukwa cha tchimo lawo;

mumawononga chuma chawo monga njenjete;

munthu aliyense ali ngati mpweya.

Sela

12“Imvani pemphero langa Inu Yehova,

mverani kulira kwanga kopempha thandizo;

musakhale chete pamene ndikulirira kwa Inu,

popeza ndine mlendo wanu wosakhalitsa;

monga anachitira makolo anga onse.

13Musandiyangʼane mwaukali, choncho ndidzatha kusangalala

ndisanafe ndi kuyiwalika.”