Nnwom 38 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom 38:1-22

Dwom 38

Dawid dwom. Adesrɛ.

1Awurade, nka mʼanim wɔ wʼabufuw mu

na ntwe mʼaso wɔ wʼabufuwhyew mu.

2Wo bɛmma hwirew me mu,

na wo nsa adwerɛw me.

3Wʼabufuwhyew no nti ahoɔden biara nni me mu;

me bɔne nti, me nnompe ahodwow.

4Mʼafɔdi amene me

te sɛ adesoa a mu yɛ duru dodo.

5Mʼakuru bɔn na aporɔw

esiane me bɔne mu agyimisɛm nti.

6Makotow na wɔabrɛ me ase;

da mu nyinaa menantenantew twa agyaadwo.

7Mʼakyi dompe mu yaw boro so:

ahoɔden biara nni me nipadua mu.

8Mabrɛ na mapɛtɛw koraa.

Me koma mu yaw ma misi apini.

9Awurade, nea merehwɛ anim nyinaa da wʼanim;

mʼapinisi nhintaw wo.

10Me koma bɔ kitirikitiri, na mʼahoɔden asa

mpo mʼaniwa aduru sum.

11Mʼapirakuru nti me nnamfonom ne me yɔnkonom mmɛn me;

mʼafipamfo twe wɔn ho fi me ho.

12Wɔn a wɔpɛ sɛ wokum me no sum me mfiri,

wɔn a wɔpɛ sɛ wɔhaw me no di me sɛe ho nkɔmmɔ

da mu nyinaa wodwen nnaadaasɛm ho.

13Mete sɛ ɔsotifo a ɔnte asɛm,

mete sɛ mum a ontumi nkasa.

14Mayɛ sɛ obi a ɔnte asɛm,

nea nʼano ntumi mma mmuae.

15Awurade, meretwɛn wo;

Awurade me Nyankopɔn, wubegye me so.

16Mekae se, “Mma wɔn ani nnye;

anaa wɔmma wɔn ho so bere a mʼanan awatiri no.”

17Mereyɛ mahwe ase,

na me yaw da so wɔ me mu.

18Meka me mfomso kyerɛ;

me bɔne hyɛ me so.

19Bebree na wɔyɛ mʼatamfo;

wɔn a wɔtan me kwa no dɔɔso.

20Wɔn a wɔde bɔne tua me papa so ka no,

bɔ me ahohora bere a mereyɛ papa.

21Awurade nnyaw me.

Me Nyankopɔn, nkɔ akyiri!

22Bra ntɛm bɛboa me,

Awurade, mʼAgyenkwa.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 38:1-22

Salimo 38

Salimo la Davide. Kupempha.

1Yehova musandidzudzule mutapsa mtima

kapena kundilanga muli ndi ukali.

2Pakuti mivi yanu yandilasa,

ndipo dzanja lanu latsika ndipo landifikira.

3Chifukwa cha ukali wanu mulibe thanzi mʼthupi langa;

mafupa anga alibe mphamvu chifukwa cha tchimo langa.

4Kulakwa kwanga kwandipsinja

ngati katundu wolemera kwambiri kuposa mphamvu zanga.

5Mabala anga akuwola ndipo akununkha

chifukwa cha uchitsiru wa moyo wanga wauchimo.

6Ine ndapindika msana ndipo ndawerama kwambiri;

tsiku lonse ndimangolira.

7Msana wanga wagwidwa ndi ululu wosasimbika,

mulibe thanzi mʼthupi langa.

8Ndilibe mphamvu ndipo ndakunthidwa kwathunthu;

ndikubuwula ndi ululu wa mumtima.

9Zokhumba zanga zonse zili poonekera pamaso panu Ambuye,

kusisima kwanga sikunabisike kwa Inu.

10Mtima wanga ukugunda, mphamvu zanga zikutha;

ngakhale kuwala kwachoka mʼmaso mwanga.

11Abwenzi anga ndi anzanga akundipewa chifukwa cha mabala anga;

anansi anga akhala kutali nane.

12Iwo amene akufunafuna moyo wanga atchera misampha yawo,

oti andipwetekewo amayankhula za kuwonongeka kwanga;

tsiku lonse amakonza zachinyengo.

13Ine ndili ngati munthu wosamva amene sangamve,

monga wosayankhula, amene sangathe kutsekula pakamwa pake;

14Ndakhala ngati munthu amene samva,

amene pakamwa pake sipangathe kuyankha.

15Ndikudikira Inu Yehova;

mudzayankha, Inu Ambuye Mulungu wanga.

16Pakuti Ine ndinati, “Musawalole kuti akondwere

kapena kudzikweza okha pa ine pamene phazi langa laterereka.”

17Pakuti ndili pafupi kugwa,

ndipo ndikumva kuwawa nthawi zonse.

18Ndikuvomereza mphulupulu zanga;

ndipo ndavutika ndi tchimo langa.

19Ambiri ndi adani anga amphamvu;

amene amandida popanda chifukwa alipo ochuluka kwambiri.

20Iwo amene amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino

amandinyoza pamene nditsatira zabwino.

21Inu Yehova, musanditaye;

musakhale kutali ndi ine Mulungu wanga.

22Bwerani msanga kudzandithandiza,

Inu Ambuye Mpulumutsi wanga.