Nnwom 35 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom 35:1-28

Dwom 35

Dawid dwom.

1Awurade wo ne wɔn a wɔne me di asi no nni asi;

ko tia wɔn a wɔko tia me.

2Fa wo nkatabo ne wʼakode;

na sɔre bra bɛboa me.

3Twe peaw ne abonnua

wɔ wɔn a wɔtaa me no so.

Ka kyerɛ me kra se,

“Mene wʼagyenkwa.”

4Wɔn a wɔpɛ sɛ wokum me no,

ma wɔn anim ngu ase;

wɔn a wɔbɔ me sɛe ho pɔw no,

ma wɔmfa aniwu nsan wɔn akyi.

5Ma wɔnyɛ sɛ ntɛtɛ a mframa bɔ gu

wɔn a Awurade bɔfo repam wɔn no.

6Ma wɔn akwan so nnuru sum na ɛso ɛnyɛ toro,

na Awurade bɔfo ntaa wɔn.

7Esiane sɛ wɔde ɔtan sum me afiri kwa,

na wotuu amoa maa me a menyɛɛ wɔn hwee no nti

8ma ɔsɛe mmefu wɔn mu

na ɔtan no a wɔde hintaw no nyi wɔn,

na ma wɔnhwe amoa no mu nsɛe.

9Afei me kra ani begye wɔ Awurade mu

na wasɛpɛw ne ho wɔ ne nkwagye mu.

10Me nipadua nyinaa bɛteɛ mu aka se,

“Hena na ɔte sɛ wo, Awurade?

Wugye ohiani fi ahoɔdenfo nsam,

ne nea onni bi fi apoobɔfo nsam.”

11Adansekurumfo sɔre;

wobisa me nneɛma a minnim ho hwee ho asɛm.

12Wɔde bɔne tua papa a meyɛ so ka

na wɔma me kra yɛ basaa.

13Nanso bere a wɔyaree no, mifuraa atweaatam

na mede akɔnkyen brɛɛ me ho ase.

Bere a me mpaebɔ ho mmuae nnya mmae no,

14mekɔɔ so twaa adwo,

sɛnea meyɛ ma mʼadamfo anaa onuabarima.

Mede awerɛhow sii me ti ase

te sɛ nea meregyam me na.

15Nanso bere a mihintiw no wɔde anigye boaa wɔn ho ano;

afowfo twaa me ho hyiae a minnim,

na wodii me ho nseku a wɔantwa so da.

16Wɔde adwemmɔne dii me ho fɛw te sɛ nnipa a wonni nyamesu,

wɔtwɛree wɔn se guu me so.

17Awurade, wobɛhwɛ wɔn akosi da bɛn?

Gye me nkwa fi wɔn sɛe mu,

gye me nkwa a ɛsom bo no fi saa gyata yi nsam.

18Na mɛda wo ase wɔ guabɔ kɛse ase;

wɔ nnipa dodow mu na mɛkamfo wo.

19Mma mʼatamfo a wɔtan me kwa no

nhwɛ me haw nserew.

Mma wɔn a menyɛɛ wɔn hwee nanso wɔtan me no

mmfa adwene bɔne mmu me anikyiw.

20Wɔnnkasa asomdwoe so,

na mmom, wɔde ntwatoso

tia nnipa a wɔmpɛ wɔn ho asɛm wɔ asase yi so.

21Wɔhwɛ me haw ka se, “Yiw! Yiw,

yɛde yɛn ankasa ani ahu.”

22Awurade, woahu na mmua wʼano.

Ntwe wo ho nkɔ akyiri, Awurade.

23Nyan, sɔre na bɛbɔ me ho ban!

Ka bi ma me, me Nyankopɔn ne mʼAwurade.

24Di mʼasɛm ma me wɔ wo trenee no mu, Awurade me Nyankopɔn;

mma wɔnnhwɛ me haw nserew.

25Mma wɔnnwene nka se, “Yiw, nea yɛpɛ ni!”

anaa wɔnnka se, “Yɛanya no.”

26Ma wɔn a wɔhwɛ me haw serew me wɔ mʼahohiahia mu no

nyinaa anim ngu ase na wɔnyɛ basaa;

ma wɔn a wodi me so akokurokosɛm no

nhyɛ aniwu ne animguase atade.

27Ma wɔn a wodi ahurusi wɔ me bembu ho no

mfa anigye ne ahosɛpɛw nteɛ mu

bere nyinaa mu; ma wɔnka se, “Momma Awurade so,

ɔno na nʼani gye ne somfo yiyedi ho.”

28Me tɛkrɛma bɛka wo trenee,

ne wʼayeyi, da mu nyinaa.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 35:1-28

Salimo 35

Salimo la Davide.

1Inu Yehova, mulimbane nawo amene akulimbana nane;

mumenyane nawo amene akumenyana nane.

2Tengani chishango ndi lihawo;

dzukani ndipo bwerani mundithandize.

3Tengani mkondo ndi nthungo,

kulimbana ndi iwo amene akundithamangitsa.

Uzani moyo wanga kuti,

“Ine ndine chipulumutso chako.”

4Iwo amene akufunafuna moyo wanga

anyozedwe ndi kuchita manyazi;

iwo amene akukonza kuti moyo wanga uwonongeke

abwerere mʼmbuyo mochititsa mantha.

5Akhale ngati mankhusu owuluka ndi mphepo

pamene mngelo wa Yehova akuwapirikitsa.

6Njira yawo ikhale ya mdima ndi yoterera

pamene mngelo wa Yehova akuwathamangitsa.

7Popeza ananditchera ukonde popanda chifukwa

ndipo popanda chifukwa andikumbira dzenje,

8chiwonongeko chiwapeza modzidzimutsa

ukonde umene iwo abisa uwakole,

agwere mʼdzenje kuti awonongedwe.

9Pamenepo moyo wanga udzakondwera mwa Yehova

ndi kusangalala ndi chipulumutso chake.

10Thupi langa lidzafuwula mokondwera,

“Ndani angafanane nanu Yehova?

Mumalanditsa osauka kwa amene ali ndi mphamvu zambiri,

osauka ndi osowa kwa iwo amene amawalanda.”

11Mboni zopanda chisoni zinayimirira,

zinandifunsa zinthu zimene sindikuzidziwa.

12Iwo anandibwezera zoyipa pa zabwino

ndipo anasiya moyo wanga pa chisoni.

13Koma pamene iwo ankadwala, ine ndinavala chiguduli

ndi kudzichepetsa ndekha posala zakudya.

Pamene mapemphero anga anabwerera kwa ine osayankhidwa,

14ndinayendayenda ndi kulira maliro,

kumulira ngati bwenzi langa kapena mʼbale wanga.

Ndinaweramitsa mutu wanga mosweka mtima

kukhala ngati ndikulira amayi anga.

15Koma pamene ndinaphunthwa, iwo anasonkhana mosangalala;

ondithira nkhondo anasonkhana kutsutsana nane, ineyo osadziwa.

Iwo sanasiye kundiyankhulira mawu onyoza.

16Monga anthu osapembedza, iwo anandinyoza mwachipongwe;

anandikukutira mano awo.

17Ambuye, mpaka liti mudzakhala mukungoyangʼana?

Landitsani moyo wanga ku chiwonongeko chawo,

moyo wanga wopambana ku mikango.

18Ndidzakuyamikani mu msonkhano waukulu;

pakati pa gulu lalikulu la anthu ndidzakutamandani.

19Musalole adani anga onyenga

akondwere chifukwa cha masautso anga;

musalole kuti amene amadana nane popanda chifukwa

andiyangʼane chamʼmbali mondinyoza.

20Iwowo sayankhula mwamtendere,

koma amaganizira zonamizira

iwo amene amakhala mwabata mʼdziko.

21Iwo amandiseka mofuwula ndipo amati, “Haa! Haa!

Ndipo ndi maso athuwa ife taziona.”

22Yehova mwaona zimenezi; musakhale chete.

Ambuye musakhale kutali ndi ine.

23Dzukani, ndipo nyamukani kunditeteza!

Mulimbane nawo chifukwa cha ine, Mulungu wanga ndi Ambuye anga.

24Onetsani kusalakwa kwanga mwa chilungamo chanu, Inu Yehova Mulungu wanga.

Musalole kuti akondwere chifukwa cha mavuto anga.

25Musalole kuti aganize kuti, “Amati atani, zachitika monga momwe timafunira!”

Kapena kunena kuti, “Tamutha ameneyu basi.”

26Onse amene amakondwera ndi masautso anga

achite manyazi ndi kusokonezeka.

Onse amene amadzikweza kufuna kundipambana,

avekedwe manyazi ndi mnyozo ngati zovala.

27Koma amene amakondwera chifukwa chakuti ndine wosalakwa,

afuwule mwachimwemwe ndi chisangalalo.

Nthawi zonse azinena kuti, “Yehova akwezeke,

Iye amene amakondwera ndi kupeza bwino kwa mtumiki wake.”

28Pakamwa panga padzayankhula za chilungamo chanu

ndi za matamando anu tsiku lonse.