Nnwom 31 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom 31:1-24

Dwom 31

Dawid dwom.

1Wo mu, Awurade na manya guankɔbea;

mma mʼanim ngu ase;

fi wo trenee mu gye me.

2Yɛ aso ma me,

bra ntɛm begye me;

yɛ me bammɔ botan,

aban a mʼatamfo nsa renka me.

3Sɛ woyɛ me botan ne mʼaban nti,

wo din nti di mʼanim na kyerɛ me kwan.

4Gye me fi afiri a wɔasum me no mu,

efisɛ wo ne me guankɔbea.

5Wo nsam na mede me kra hyɛ;

gye me bio, Awurade, Onyankopɔn nokwafo.

6Mikyi wɔn a wɔsom abosom huhuw;

mede me ho to Awurade so.

7Mʼani begye na madi ahurusi wɔ wo dɔ mu,

efisɛ wuhu mʼamanehunu,

na wunim me kra mu haw.

8Womfaa me nhyɛɛ ɔtamfo no nsa

mmom wode me nan asisi petee mu.

9Hu me mmɔbɔ, Awurade, efisɛ me ho yeraw me;

awerɛhow ama mʼani so ayɛ kusuu

ɔyaw ama me kra ne me honam ayɛ mmerɛw.

10Ɔyawdi retew me nkwa so,

na abooboo tew me mfe so;

ɔhaw nti mʼahoɔden kɔ fam,

na me nnompe nso ahodwow.

11Mʼatamfo nyinaa nti,

mayɛ ahohora wɔ me nnamfonom mu;

nnipa a wonim me suro me,

na wɔn a wohu me mmɔnten so guan.

12Obiara werɛ afi me te sɛ nea mawu;

mayɛ sɛ kuku a abɔ.

13Mete asomsɛm dodow a wɔka

ahunahuna atwa me ho ahyia.

Wɔrepam me ti so,

na wɔbɔ pɔw sɛ wobekum me.

14Nanso mede me ho ato wo so, Awurade;

meka se, “Woyɛ me Nyankopɔn.”

15Me mmere wɔ wo nsam

gye me fi mʼatamfo

ne wɔn a wɔtaa me no nsam.

16Tew wʼanim kyerɛ wo somfo;

gye me wɔ wo dɔ a enni huammɔ no mu.

17Mma mʼanim ngu ase, Awurade,

efisɛ masu afrɛ wo;

mmom, ma amumɔyɛfo anim ngu ase

na wɔnna wɔn nna mu komm.

18Mua atorofo ano,

efisɛ wɔde ahantan ne animtiaabu

kasa tia atreneefo.

19Wo papayɛ dɔɔso,

ɛno na woakora ama wɔn a wosuro wo no

ɛno na wode ma wɔn a woguan toa wo no

wɔ nnipa anim.

20Wode wɔn sie wʼanim bammɔ mu

fi nnipa nsusuwii bɔne ho;

wo tenabea hɔ na wode wɔn sie dwoodwoo

fi tɛkrɛma a ɛbɔ sobo ho.

21Ayeyi nka Awurade!

Sɛ wayi ne dɔ nwonwaso akyerɛ me

bere a na mewɔ kuropɔn a atamfo atwa ho ahyia no mu no.

22Mebɔɔ huboa no mekae se:

“Woayi wʼani afi me so!”

Nanso wotee me mmɔborɔsu

bere a mekotow srɛɛ wo no.

23Monnɔ Awurade mo a moyɛ nʼahotewfo nyinaa!

Awurade kora wɔn a wodi nokware so,

na ahomasofo de, otua wɔn ka pɛpɛɛpɛ.

24Monyɛ den na momma mo bo ntɔ mo yam,

mo a mowɔ anidaso wɔ Awurade mu nyinaa.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 31:1-24

Salimo 31

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Mwa Inu Yehova, ine ndimathawiramo;

musalole nʼkomwe kuti ndichititsidwe manyazi;

mundipulumutse chifukwa cha chilungamo chanu.

2Tcherani khutu lanu kwa ine,

bwerani msanga kudzandilanditsa;

mukhale thanthwe langa lothawirapo,

linga lolimba kundipulumutsa ine.

3Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa,

chifukwa cha dzina lanu tsogolereni ndi kundiwongolera.

4Ndimasuleni mu msampha umene anditchera

pakuti ndinu pothawirapo panga.

5Mʼmanja mwanu ndipereka mzimu wanga;

womboleni Yehova Mulungu wachoonadi.

6Koma ine ndimadana nawo amene amamamatira mafano achabechabe;

ine ndimadalira Yehova.

7Ndidzakondwa ndi kusangalala mʼchikondi chanu

popeza Inu munaona masautso anga

ndipo mumadziwa kuwawa kwa moyo wanga.

8Inu simunandipereke kwa mdani

koma mwayika mapazi anga pa malo otakasuka.

9Mundichitire chifundo Inu Yehova pakuti ndili pa mavuto;

maso anga akulefuka ndi chisoni,

mʼmoyo mwanga ndi mʼthupi mwanga momwe mukupweteka.

10Moyo wanga ukunyeka chifukwa cha kuwawidwa mtima

ndi zaka zanga chifukwa cha kubuwula;

mphamvu zanga zatha chifuwa cha masautso,

ndipo mafupa anga akulefuka.

11Chifukwa cha adani anga onse,

ndine wonyozeka kwambiri ndi anansi anga;

ndine chochititsa manyazi kwa abwenzi anga.

Iwo amene amandiona mu msewu amandithawa.

12Ine ndinayiwalika kwa iwo ngati kuti ndinamwalira;

ndakhala ngati mʼphika wosweka.

13Pakuti ine ndamva zonena zoyipa za anthu ambiri;

zoopsa zandizungulira mbali zonse;

iwo akukonza chiwembu kuti alimbane nane,

kuti atenge moyo wanga.

14Koma ndikudalira Inu Yehova;

ndikunena kuti, “Ndinu Mulungu wanga.”

15Masiku anga ali mʼmanja mwanu;

ndipulumutseni kwa adani anga

ndi kwa iwo amene akundithamangitsa.

16Walitsani nkhope yanu pa mtumiki wanu;

pulumutseni mwa chikondi chanu chosatha.

17Yehova musalole kuti ndichite manyazi,

pakuti ndalirira kwa Inu;

koma oyipa achititsidwe manyazi

ndipo agone chete mʼmanda.

18Milomo yawo yabodzayo ikhale chete,

pakuti chifukwa cha kunyada

ayankhula modzikuza kutsutsana ndi wolungama.

19Ndi waukulu ubwino wanu

umene mwawasungira amene amakuopani,

umene mumapereka anthu akuona

kwa iwo amene amathawira kwa Inu.

20Mu mthunzi wa pamalo popezeka panu muwabisa,

kuwateteza ku ziwembu za anthu;

mʼmalo anu okhalamo mumawateteza

kwa anthu owatsutsa.

21Matamando akhale kwa Yehova,

pakuti anaonetsa chikondi chake chodabwitsa kwa ine

pamene ndinali mu mzinda wozingidwa.

22Ndili mʼnkhawa zanga ndinati,

“Ine ndachotsedwa pamaso panu!”

Komabe Inu munamva kupempha chifundo kwanga

pamene ndinapempha thandizo kwa Inu.

23Kondani Yehova oyera mtima ake onse!

Yehova amasunga wokhulupirika

koma amalanga kwathunthu anthu odzikuza.

24Khalani ndi nyonga ndipo limbani mtima,

inu nonse amene mumayembekezera Yehova.