Nnwom 21 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom 21:1-13

Dwom 21

Dawid dwom.

1Awurade, ɔhene di anigye wɔ wʼahoɔden mu.

Nʼani gye mmoroso wɔ nkonimdi a woma no nti!

2Woama no nea ne koma pɛ;

woamfa nʼabisade ankame no.

3Wode nhyira a edi mu hyiaa no

na wode sikakɔkɔɔ ankasa ahenkyɛw hyɛɛ no.

4Obisaa wo hɔ nkwa, na wode maa no,

nna tenten a enni awiei.

5Nkonimdi a woma no nti, nʼanuonyam so;

wode kɛseyɛ ne nidi adom no.

6Ampa ara, woama no nhyira a ɛnsa da

na woama no ahosɛpɛw wɔ wʼanim anigye mu.

7Ɔhene no de ne ho to Awurade so;

Ɔsorosoroni no nokware dɔ no nti,

ɔrenhinhim.

8Wo nsa bɛka wʼatamfo nyinaa;

wo nsa nifa beso wɔn a wokyi wo no mu.

9Bere a wubeyi wo ho adi no

wobɛyɛ wɔn sɛ fononoo a mu adɔ.

Awurade fi nʼabufuwhyew mu bɛmene wɔn,

na ne gya no ahyew wɔn.

10Wobɛtɔre wɔn ase wɔ asase so,

na wɔn asefo afi adesamma mu.

11Ɛwɔ mu sɛ wɔbɔ pɔw tia wo

na wɔyɛ nhyehyɛe bɔne, nanso wɔrenni nkonim;

12efisɛ wobɛma wɔasan wɔn akyi

bere a woatwe bɛmma akyerɛ wɔn so no.

13Yɛma wo so, Awurade, wɔ wʼahoɔden mu;

yɛbɛto nnwom na yɛakamfo wo kɛseyɛ.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 21:1-13

Salimo 21

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide.

1Inu Yehova, mfumu ikusangalala mu mphamvu yanu,

chimwemwe chake nʼchachikuludi pa kupambana kumene mumapereka!

2Inu mwayipatsa zokhumba za mtima wake

ndipo simunayimane zopempha za pa milomo yake.

Sela

3Inu munayilandira ndi madalitso ochuluka

ndipo munayiveka chipewa chaufumu chagolide weniweni pa mutu wake.

4Iye anakupemphani moyo, ndipo munamupatsa

masiku ochuluka kwamuyaya.

5Kudzera mʼzigonjetso zimene munapereka, ulemerero wake ndi waukulu;

Inu mwapereka pa iyo ulemerero ndi ufumu.

6Zoonadi Inu mwayipatsa madalitso amuyaya,

Inu mwayipatsa chisangalalo ndi chimwemwe chimene chili pamaso panu.

7Pakuti mfumu imadalira Yehova;

kudzera mʼchikondi chake chosatha cha Wammwambamwamba,

iyo sidzagwedezeka.

8Dzanja lanu lidzayimitsa adani anu onse;

dzanja lanu lamanja lidzagwira adani anu.

9Pa nthawi ya kuonekera kwanu

mudzawasandutsa ngʼanjo yamoto yotentha.

Mu ukali wake Yehova adzawameza,

ndipo moto wake udzawatha.

10Inu mudzawononga ana awo pa dziko lapansi,

zidzukulu zawo pakati pa anthu.

11Ngakhale iwo akukonzereni chiwembu mwa kuchenjera kwawo

sadzapambana;

12pakuti mudzawapirikitsa ndipo adzaonetsa misana yawo

pamene mudzawaloza ndi mivi yanu.

13Mukwezeke Inu Yehova mʼmphamvu yanu,

ife tidzayimba nyimbo ndi kutamanda mphamvu yanu.