Nnwom 16 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom 16:1-11

Dwom 16

Dawid mpaebɔ.

1Bɔ me ho ban, me Nyankopɔn,

na wo mu na minya guankɔbea.

2Meka kyerɛɛ Awurade se,

“MʼAwurade ne wo;

minni ade pa biara ka wo ho.”

3Ahotefo a wɔwɔ asase no so de,

wɔne anuonyamfo a

mʼanigye wɔ wɔn mu.

4Wɔn a wodi anyame afoforo akyi no,

wɔn awerɛhow bɛdɔɔso.

Merengu mogya nsa mma saa anyame no

na meremfa mʼano mmɔ wɔn din.

5Awurade, wode me kyɛfa ne me kuruwa ama me;

woama me kyɛfa anya bammɔ.

6Mʼahye akɔdeda mmeae a eye ama me;

ampa ara mewɔ agyapade a ho yɛ anigye.

7Mɛkamfo Awurade a otu me fo;

na anadwo mpo, me koma kyerɛkyerɛ me.

8Mihu Awurade wɔ mʼani so daa nyinaa.

Esiane sɛ ɔwɔ me nsa nifa nti, merenhinhim da.

9Ɛno nti, me kra ani gye, na mede me tɛkrɛma di ahurusi;

me nipadua nso bɛhome asomdwoe mu,

10efisɛ, worennyaw me awufo mu.

Na woremma wo Kronkronni no mporɔw.

11Woakyerɛ me nkwagye kwan,

na wobɛma mʼani agye wɔ wʼanim,

na anigye a ɛrensa da wɔ wo nifa so.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 16:1-11

Salimo 16

Mikitamu ya Davide.

1Ndisungeni Inu Mulungu,

pakuti ine ndimathawira kwa Inu.

2Ndinati kwa Yehova, “Inu ndinu Ambuye anga;

popanda Inu, ine ndilibe chinthu chinanso chabwino.”

3Kunena za oyera mtima amene ali pa dziko,

amenewa ndi olemekezeka, amene ndimakondwera nawo.

4Anthu amene amathamangira kwa milungu ina

mavuto awo adzachulukadi.

Ine sindidzathira nawo nsembe zawo zamagazi

kapena kutchula mayina awo ndi pakamwa panga.

5Yehova, Inu mwandipatsa cholowa changa ndi chikho changa;

mwateteza kolimba gawo langa.

6Malire a malo anga akhala pabwino;

ndithudi, ine ndili cholowa chokondweretsa kwambiri.

7Ine ndidzatamanda Yehova amene amandipatsa uphungu;

ngakhale usiku mtima wanga umandilangiza.

8Ndayika Yehova patsogolo panga nthawi zonse.

Popeza Iyeyo ali kudzanja langa lamanja,

sindidzagwedezeka.

9Choncho mtima wanga ndi wosangalala ndipo pakamwa panga pakukondwera;

thupi langanso lidzakhala pabwino,

10chifukwa Inu simudzandisiya ku manda,

simudzalola kuti woyera wanu avunde.

11Inu mwandidziwitsa njira ya moyo;

mudzandidzaza ndi chimwemwe pamaso panu,

ndidzasangalala mpaka muyaya pa dzanja lanu lamanja.