Nnwom 10 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nnwom 10:1-18

Dwom 10

1Adɛn, Awurade, na wugyina akyirikyiri saa?

Adɛn na wode wo ho ahintaw wɔ amanehunu mmere mu yi?

2Omumɔyɛfo de ahantan taataa mmɔborɔfo,

wɔn a ne nneyɛe mfiri yiyi wɔn no.

3Ɔde nea ne koma hwehwɛ hoahoa ne ho;

ohyira odifudepɛfo na oyi Awurade ahi.

4Ahantan nti omumɔyɛfo nhwehwɛ Awurade;

ne nsusuwii mu no Onyankopɔn nsi hwee.

5Nʼakwan nyinaa mu odi yiye;

ɔma ne ho so, na wo mmara mfa no ho;

na odi nʼatamfo nyinaa ho fɛw.

6Ɔka kyerɛ ne ho se: “Hwee remma minhinhim;

mʼani begye daa, na merenkɔ amanehunu mu da.”

7Nnome, atoro ne ahunahuna ahyɛ nʼanom ma;

Ɔhaw ne mmusu hyɛ ne tɛkrɛma ase.

8Ɔtɛw bɛn nkuraa no;

ofi ahintawee kum nea onnim hwee,

ohintaw hwɛ wɔn a ɔrehwehwɛ wɔn ayɛ wɔn bɔne no.

9Ɔte sɛ gyata a wahintaw;

ɔtɛw sɛ ɔbɛkyere mmɔborɔni;

ɔkyere wɔn twe wɔn ase de wɔn kɔ ne bon mu.

10Ɔdwerɛw wɔn a ɔkyere wɔn no ma wɔtɔ beraw;

na ɔde nʼahoɔden ka wɔn hyɛ.

11Ɔka kyerɛ ne ho se, “Onyankopɔn werɛ afi;

wayi nʼani afi so na onhu.”

12Sɔre, Awurade! Ma wo nsa so, Onyankopɔn.

Mma wo werɛ mfi wɔn a wonni aboafo.

13Adɛn nti na omumɔyɛfo yi Onyankopɔn ahi?

Adɛn nti na ɔka kyerɛ ne ho se,

“Ɔremfrɛ me akontaabu so?”

14Nanso wo, Onyankopɔn, wuhu amanehunufo haw;

na wayɛ wʼadwene sɛ wobɛhwɛ.

Mmɔborɔni de ne ho ma wo;

wo na woyɛ ayisaa boafo.

15Bubu omumɔyɛfo ne ɔbɔnefo aprɛw;

frɛ no na ommebu nʼamumɔyɛ ho nkontaa,

nʼamumɔyɛ a anka wɔrenhu no.

16Awurade yɛ ɔhene daa nyinaa;

amanaman no bɛyera nʼasase so.

17Awurade, wutie mmɔborɔfo adesrɛ;

wohyɛ wɔn nkuran, na wutie wɔn sufrɛ,

18na wudi ma ayisaa ne nea wɔhyɛ no so,

sɛnea ɛbɛyɛ a ɔdesani a ofi asase mu

renhunahuna bio.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 10:1-18

Salimo 10

1Nʼchifukwa chiyani Yehova mwayima patali?

Chifukwa chiyani mukudzibisa nokha pa nthawi ya mavuto?

2Mwa kunyada kwake munthu woyipa asaka wofowoka,

amene akodwa mʼnjira zimene iye wakonza.

3Iye amatamandira zokhumba za mu mtima wake;

amadalitsa aumbombo ndi kuchitira chipongwe Yehova.

4Mwa kunyada kwake woyipa safunafuna Mulungu;

mʼmaganizo ake wonse mulibe malo a Mulungu.

5Zinthu zake zimamuyendera bwino;

iye ndi wamwano ndipo malamulo anu ali nawo kutali;

amanyogodola adani ake onse.

6Iye amadziyankhulira kuti, “Palibe chimene chidzandigwedeze.

Ndidzakhala wokondwa nthawi zonse ndipo sindidzakhala pa mavuto.”

7Mʼkamwa mwake mwadzaza matemberero, mabodza ndi zoopseza;

zovutitsa ndi zoyipa zili pansi pa lilime lake.

8Iye amabisalira anthu pafupi ndi midzi,

kuchokera pobisalapo amapha anthu osalakwa,

amayangʼanayangʼana mwachinsinsi anthu oti awawononge.

9Amabisalira anthu ngati mkango pa zitsamba.

Amabisalira kuti agwire anthu opanda mphamvu;

amagwira anthu opanda mphamvu ndi kuwakokera mu ukonde wake.

10Anthuwo amawapondaponda ndipo amakomoka;

amakhala pansi pa mphamvu zake.

11Iye amati mu mtima mwake, “Mulungu wayiwala,

wabisa nkhope yake ndipo sakuonanso.”

12Dzukani Yehova! Onetsani dzanja lanu Inu Mulungu.

Musayiwale anthu opanda mphamvu.

13Nʼchifukwa chiyani munthu woyipa amachitira chipongwe Mulungu?

Chifukwa chiyani amati mu mtima mwake,

“Iye sandiyimba mlandu?”

14Komatu Inu Mulungu, mumazindikira mavuto ndi zosautsa,

mumaganizira zochitapo kanthu.

Wovutikayo amadzipereka yekha kwa Inu pakuti

Inu ndi mthandizi wa ana amasiye.

15Thyolani dzanja la woyipitsitsa ndi la munthu woyipa;

muzengeni mlandu chifukwa cha zoyipa zake

zimene sizikanadziwika.

16Yehova ndi Mfumu kwamuyaya;

mitundu ya anthu idzawonongeka kuchoka mʼdziko lake.

17Mumamva Inu Yehova, zokhumba za osautsidwa;

mumawalimbikitsa ndipo mumamva kulira kwawo.

18Kuteteza ana amasiye ndi oponderezedwa,

ndi cholinga chakuti munthu amene ali wa dziko lapansi asaopsenso.