Nahum 3 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Nahum 3:1-19

Ninewe Nnome

1Nnome nka mogya kuropɔn

a atoro ne korɔn ahyɛ no ma

na amanehunufo mpa mu da!

2Apɔnkɔkafo abaa regyigye,

nteaseɛnam nhankare reyɛ kirididi

Apɔnkɔ rehuruhuruw

ne nteaseɛnam redankyidankyi.

3Apɔnkɔ ne wɔn sotefo ko kɔ wɔn anim;

afoa twa yerɛw yerɛw,

na mpeaw nso pa yerɛw yerɛw.

Atɔfo bebree,

awufo a bi deda bi so,

afunu a wontumi nkan wɔn dodow

a nnipa tiatia so.

4Eyi nyinaa fi oguamanfo bi akɔnnɔ,

ntafowayifo no nnaadaa dodow no.

Ɔno na ɔde nʼaguamammɔ tɔn amanaman

na ɔde ne ntafowayi tɔn nnipa.

5“Me ne wo nka,” sɛnea Asafo Awurade se ni,

“Mɛpagyaw wʼatade akɔ soro.

Mɛma amanaman ahu wʼadagyaw

na ahenni ahorow nso ahu wʼanimguase.

6Mede fi bɛsra wo ho,

mebu wo animtiaa

na mama nnipa ahwɛ wo.

7Obiara a obehu wo beguan afi wo ho aka se,

‘Ninewe adwiriw, na hena na obesu no?’

Ɛhe na menya obi akyekye wo werɛ?”

8Wuye sen Tebes a

ɛda Asubɔnten Nil ho a

nsu atwa ne ho ahyia ana?

Asubɔnten bɔ ne ho ban

na nsu yɛ ne fasu.

9Kus ne Misraim yɛ ne dɔm a wontumi nkan wɔn.

Put ne Libia ka nʼadomfo ho.

10Nanso wɔfaa no nnommum

twaa no asu.

Wɔtow ne nkokoaa hwehwee fam

ma wɔtetee wɔ mmɔnten so.

Wɔbɔɔ nʼadehye so ntonto,

na nʼatitiriw nso wɔde nkɔnsɔnkɔnsɔn guguu wɔn.

11Wo nso wobɛbow

Na wubehintaw wo ho

de akɔpɛ guankɔbea wɔ atamfo nkyɛn.

12Wʼaban nyinaa te sɛ borɔdɔma nnua

a asow aba foforo:

sɛ wɔwosow a

aba no tetew gu ma nea ɔrehwehwɛ bi adi.

13Hwɛ wʼakofo

wɔn nyinaa yɛ mmea!

Wʼasase so apon ano deda hɔ ma wʼatamfo;

ogya ahyew wʼapon no akyi adaban.

14Sesaw nsu sie ma bere a wɔatua mo ano no.

Yere wo bammɔ mu!

Wɔw dɔte no

na siesie ntayaa a wɔato no!

15Ɛhɔ na ogya bɛhyew wo;

afoa betwa wo ahwe fam,

wobedi wo nam sɛ mmoadabikuw.

Monnɔ sɛ tɛwtɛw,

mo ase mfɛe sɛ mmoadabi!

16Woama wʼaguadifo adɔɔso,

wɔn dodow asen ɔsoro nsoromma,

nanso wɔte sɛ mmoadabi a wɔbɔ asase no kwaterekwa

na afei wotu kɔ.

17Wʼawɛmfo te sɛ mmoadabi.

Wʼadwumayɛfo te sɛ mmoadabi akuw

a wɔsensam ban ho awɔw da.

Nanso sɛ owia pue a wotu kɔ,

na obi nnim faako a wɔkɔ.

18Asiriahene wo nguanhwɛfo retɔ nko.

Wʼanuonyamfo deda hɔ rehome.

Wo nkurɔfo abɔ apete wɔ mmepɔw no so

a wonni anoboaboafo.

19Aduru biara rentumi nkum wʼapirakuru no;

wo kuru no bekum wo.

Obiara a ɔte wo nka no

bɔ ne nsam wɔ wʼasehwe ho,

Na hena koraa na wʼatirimɔdensɛm

no bi nkaa no da?

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nahumu 3:1-19

Tsoka la Ninive

1Tsoka kwa mzinda wopha anthu,

mzinda wodzaza ndi mabodza,

mzinda wodzaza ndi anthu olanda zinthu anzawo,

mu mzinda mʼmene simusowa anthu osautsidwa nthawi zonse!

2Kulira kwa zikwapu,

mkokomo wa mikombero,

kufuwula kwa akavalo

ndiponso phokoso la magaleta!

3Kuthamanga kwa anthu okwera pa akavalo,

kungʼanima kwa malupanga

ndi kunyezimira kwa mikondo!

Anthu ambiri ophedwa,

milumilu ya anthu akufa,

mitembo yosawerengeka,

anthu akupunthwa pa mitemboyo.

4Zonsezi ndi chifukwa cha zilakolako za mkazi wachiwerewere,

wokopa anthu uja, mkazi wochita zamatsenga,

amene anakopa mitundu ya anthu ndi zachiwerewere zake,

ndiponso anthu a mitundu ina ndi zaufiti zake.

5Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Ine ndikutsutsana nawe.

Ndidzakuvula chovala chako.

Anthu a mitundu ina ndidzawaonetsa umaliseche wako

ndipo udzachita manyazi pamaso pa maufumu onse.

6Ndidzakuthira zonyansa,

ndidzakuchititsa manyazi

ndiponso kukusandutsa chinthu choseketsa.

7Onse amene adzakuona adzakuthawa ndipo adzati,

‘Ninive wasanduka bwinja,

adzamulira ndani?’

Kodi ndingamupeze kuti munthu woti nʼkukutonthoza?”

8Kodi ndiwe wopambana Tebesi,

mzinda wokhala mʼmbali mwa Nailo,

wozunguliridwa ndi madzi?

Mtsinjewo unali chitetezo chake,

madziwo anali linga lake.

9Mphamvu zake zinali Kusi ndi Igupto,

Puti ndi Libiya anali ena mwa abwenzi ake.

10Komabe anthu a ku Tebesi anagwidwa

ndipo anapita ku ukapolo.

Ana ake anawaphwanyitsa pansi

mʼmisewu yonse ya mu mzindamo.

Anachita maere ogawana anthu ake otchuka,

ndipo anthu ake onse amphamvu

anamangidwa ndi maunyolo.

11Iwenso Ninive udzaledzera;

udzabisala

ndipo udzafunafuna malo othawirako kuopa mdani.

12Malo ako onse otetezedwa ali ngati mitengo ya mkuyu

yokhala ndi zipatso zoyambirira kucha;

pamene agwedeza mitengoyo,

nkhuyuzo zimagwera mʼkamwa mwa wofuna kuzidya.

13Tayangʼana ankhondo ako,

onse ali ngati akazi!

Zipata za dziko lako zatsekukira adani ako;

moto wapsereza mipiringidzo yake.

14Tungani madzi woti mudzamwe nthawi ya kuzunguliridwa kwanu,

limbitsani chitetezo chanu!

Pondani dothi,

ikani mʼchikombole,

konzani khoma la njerwa!

15Kumeneko moto udzakupserezani;

lupanga lidzakukanthani

ndipo lidzakuwonongani ngati likuwononga ziwala.

Chulukanani ngati ziwala,

chulukanani ngati dzombe!

16Mwachulukitsa chiwerengero cha anthu a malonda anu

mpaka kupambana nyenyezi za mlengalenga,

koma iwo ngati dzombe akuwononga dziko

ndipo kenaka akuwuluka nʼkuchoka.

17Akalonga ako ali ngati dzombe,

akuluakulu ako ali ngati gulu la dzombe

limene lamatirira pa khoma nthawi yozizira,

koma pamene dzuwa latuluka limawuluka,

ndipo palibe amene amadziwa komwe lapita.

18Iwe mfumu ya ku Asiriya,

abusa ako agona tulo;

anthu ako olemekezeka amwalira.

Anthu ako amwazikira ku mapiri

popanda ndi mmodzi yemwe wowasonkhanitsa.

19Palibe chimene chingachize bala lako;

chilonda chako sichingapole.

Aliyense amene amamva za iwe

amawomba mʼmanja chifukwa cha kugwa kwako,

kodi alipo amene sanazilawepo

nkhanza zako zosatha?