Mmebusɛm 12 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Mmebusɛm 12:1-28

1Obiara a ɔpɛ ahohyɛso no pɛ nimdeɛ,

na nea okyi nteɛso no yɛ ogyimifo.

2Nnipa pa nya Awurade nkyɛn adom,

na Awurade bu amumɔyɛfo fɔ.

3Amumɔyɛsɛm rentumi mma onipa ase ntim,

na wɔrentumi ntu ɔtreneeni ase.

4Ɔyere a ɔwɔ suban pa yɛ ne kunu ahenkyɛw,

nanso ɔyere nimguasefo te sɛ porɔwee wɔ ne kunu nnompe mu.

5Atreneefo nhyehyɛe yɛ pɛ,

na amumɔyɛfo afotu yɛ nnaadaa.

6Amumɔyɛfo nsɛm da hɔ twɛn mogya,

na ɔtreneeni kasa yi wɔn fi mu.

7Wotu amumɔyɛfo gu na wɔyera,

nanso atreneefo fi gyina pintinn.

8Wɔkamfo onipa sɛnea ne nyansa te

na nnipa a wɔn adwene yɛ kɔntɔnkye de, wobu wɔn animtiaa.

9Eye sɛ wobɛyɛ wo ho sɛ ɔteta nanso wowɔ ɔsomfo,

sen sɛ wobɛyɛ wo ho sɛ obi, nanso wunni aduan.

10Ɔtreneeni ma ne nyɛmmoa nea wɔpɛ,

na amumɔyɛfo nneyɛe a eye pa ara yɛ atirimɔden.

11Nea ɔyɛ nʼasase so adwuma no benya aduan bebree,

na nea odi nsɛm huhuw akyi no nni adwene.

12Amumɔyɛfo pɛ abɔnefo asade,

nanso ɔtreneeni ase dɔ.

13Ɔbɔnefo anosɛm yi no sɛ afiri,

nanso ɔtreneeni nya ne ho tetew wɔ ahohia mu.

14Nneɛma pa fi onipa anom aba mu hyɛ no ma

sɛnea ne nsa ano adwuma ma no akatua no.

15Ɔkwasea akwan teɛ nʼani so,

na onyansafo tie afotu.

16Nkwaseafo bo nkyɛ fuw,

nanso mmadwemma bu wɔn ani gu animka so.

17Ɔdanseni nokwafo di adanse turodoo,

na nea odi adansekurum no twa nkontompo.

18Nsɛm hunu keka wowɔ te sɛ afoa

nanso onyansafo tɛkrɛma ma abodwo.

19Ano a ɛka nokware no tim hɔ daa,

na atoro tɛkrɛma renkyɛ koraa.

20Nnaadaa hyɛ wɔn a wodwen bɔne ho no koma mu,

na wɔn a wɔpɛ asomdwoe nya ahosɛpɛw.

21Ɔhaw biara rento ɔtreneeni,

nanso amanehunu mee amumɔyɛfo.

22Awurade kyi ano a etwa atoro,

na nʼani gye nnipa a wodi nokware ho.

23Ɔtreneeni mmɔ ne nimdeɛ ho dawuru

nanso ɔkwasea koma da agyimisɛm adi.

24Nsa a ɛyɛ adwuma no bedi tumi,

nanso akwadworɔ wie nkoasom mu.

25Koma a ɛpere ade ho ma onipa botow,

nanso nkuranhyɛsɛm bi hyɛ no den.

26Ɔtreneeni wɔ ntoboase wɔ ayɔnkofa mu,

nanso amumɔyɛfo kwan ma wɔfom.

27Onihawfo ntoto ne hanam,

nanso nsiyɛfo ahonyade som bo ma wɔn.

28Trenee kwan mu wɔ nkwa;

na owu nni saa kwan no so.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 12:1-28

1Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu,

koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.

2Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova,

koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.

3Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa,

koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.

4Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake,

koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.

5Maganizo a anthu olungama ndi owongoka,

koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.

6Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa,

koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.

7Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika,

koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.

8Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake,

koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.

9Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika,

kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.

10Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake,

koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.

11Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka,

koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.

12Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa,

koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.

13Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa;

koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.

14Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake

ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.

15Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino,

koma munthu wanzeru amamvera malangizo.

16Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo,

koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.

17Woyankhula zoona amapereka umboni woona,

koma mboni yabodza imafotokoza zonama.

18Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga,

koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.

19Mawu woona amakhala mpaka muyaya

koma mawu abodza sakhalitsa.

20Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo;

koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.

21Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama,

koma munthu woyipa mavuto samuthera.

22Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova,

koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.

23Munthu wochenjera amabisa nzeru zake,

koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.

24Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira,

koma aulesi adzakhala ngati kapolo.

25Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu,

koma mawu abwino amamusangalatsa.

26Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake,

koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.

27Munthu waulesi sapeza chimene akufuna,

koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.

28Mʼnjira yachilungamo muli moyo;

koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.