Hosea 12 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Hosea 12:1-14

1Efraim de mframa ayɛ aduan;

odi apuei mframa akyi daa

na odi atoro yɛ akakabensɛm bebree.

Ɔne Asiria yɛ apam

na ɔde ngo kɔ Misraim.

2Awurade wɔ sobo de bɔ Yuda;

ɔbɛtwe Yakob aso wɔ nʼakwan ho

na watua no ne nneyɛe so ka.

3Ɔyafunu mu na osoo ne nua nantin;

onyinii no, ɔne Onyankopɔn peperee so.

4Ɔne ɔbɔfo tentam dii ne so nkonim;

ɔde nusu srɛɛ ne nkyɛn adom.

Ohuu no wɔ Bet-El

ne no kasaa wɔ hɔ.

5Asafo Awurade Nyankopɔn,

Awurade ne ne din a ahyeta!

6Ɛsɛ sɛ wosan kɔ wo Nyankopɔn nkyɛn.

Tena ɔdɔ ne trenee mu,

na twɛn wo Nyankopɔn daa.

7Oguadini de asisi nsania yɛ nʼadwuma;

nʼani gye asisi ho.

8Efraim hoahoa ne ho sɛ,

“Meyɛ ɔdefo; manya me ho.

Mʼahonya nyinaa mu wɔrenhu

amumɔyɛ biara wɔ me ho.”

9“Mene Awurade wo Nyankopɔn,

a miyii wo fii Misraim.

Mɛma woakɔtena ntamadan mu bio

sɛnea na woyɛ wɔ wʼaponto afahyɛ nna mu no.

10Mekasa kyerɛɛ adiyifo,

memaa wɔn anisoadehu bebree

na mefaa wɔn so kaa mmebusɛm.”

11Gilead yɛ otirimɔdenfo ana?

Emu nnipa no yɛ ahuhufo!

Wɔde anantwi bɔ afɔre wɔ Gilgal ana?

Wɔn afɔremuka bɛyɛ te sɛ abo

a wɔahɔre no siw wɔ asase a wɔafuntum so.

12Yakob guan kɔɔ Aramfo asase so;

Israel som de nyaa ɔyere,

ɔhwɛɛ nguan de tuaa ti nsa.

13Awurade nam odiyifo so

yii Israel fii Misraim,

ɔnam odiyifo so hwɛɛ no.

14Nanso Efraim ahyɛ no abufuw yayaayaw;

nʼAwurade bɛma ne mogyahwiegu ho afɔdi ada no so

na obetua nʼanimtiaabu no so ka.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Hoseya 12:1-14

1Efereimu amadya mpweya;

tsiku lonse amasaka mphepo ya kummawa

ndipo amachulukitsa mabodza ndi chiwawa.

Amachita mgwirizano ndi Asiriya

ndipo amatumiza mphatso za mafuta a olivi ku Igupto.

2Yehova akuyimba mlandu Yuda;

Iye adzalanga Yakobo molingana ndi makhalidwe ake,

adzamulanga molingana ndi ntchito zake.

3Akali mʼmimba mwa amayi ake, Yakobo anagwira chidendene cha mʼbale wake;

iye atakula analimbana ndi Mulungu.

4Yakobo analimbana ndi mngelo ndipo anapambana;

analira napempha kuti amukomere mtima.

Mulungu anakumana naye ku Beteli

ndipo anayankhula naye kumeneko,

5Yehova Mulungu Wamphamvuzonse,

Yehova ndiye dzina lake lotchuka!

6Koma inu muyenera kubwerera kwa Mulungu wanu;

pitirizani chikondi ndi chiweruzo cholungama,

ndipo muzidikira Mulungu wanu nthawi zonse.

7Munthu wamalonda amagwiritsa ntchito masikelo achinyengo;

iyeyo amakonda kubera anthu.

8Efereimu amadzitama ponena kuti,

“Ndine wolemera kwambiri; ndili ndi chuma chambiri.

Palibe amene angandiloze chala

chifukwa cha kulemera kwanga.”

9“Ine ndine Yehova Mulungu wako

amene ndinakutulutsa mu Igupto.

Ndidzakukhazikaninso mʼmatenti,

monga munkachitira masiku aja pa nthawi ya zikondwerero zanu.

10Ndinayankhula ndi aneneri,

ndinawaonetsa masomphenya ambiri,

ndipo ndinawawuza mafanizo kudzera mwa iwo.”

11Kodi Giliyadi ndi woyipa?

Anthu ake ndi achabechabe!

Kodi amapereka nsembe za ngʼombe zazimuna ku Giligala?

Maguwa awo ansembe adzakhala ngati milu ya miyala

mʼmunda molimidwa.

12Yakobo anathawira ku dziko la Aramu,

Israeli anagwira ntchito kuti apeze mkazi,

ndipo anaweta nkhosa kuti akwatire mkaziyo.

13Yehova anagwiritsa ntchito mneneri kuti atulutse Israeli mu Igupto;

kudzera mwa mneneriyo Iye anawasamalira.

14Koma Efereimu wamukwiyitsa kwambiri.

Nʼchifukwa chake Yehova adzawalanga ndi imfa.

Adzawalanga chifukwa anamuchititsa manyazi kwambiri.