Hesekiel 30 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Hesekiel 30:1-26

Misraim Ho Kwadwom

1Awurade asɛm baa me nkyɛn se: 2“Onipa ba, hyɛ nkɔm na ka se: ‘Sɛɛ na Otumfo Awurade se:

“ ‘Twa adwo na ka se,

“Ao da no!”

3Na da no abɛn,

Awurade da no abɛn,

omununkum da,

amanaman no atemmu bere.

4Afoa bi bɛsɔre atia Misraim,

na ahoyeraw bɛba Kus so.

Sɛ apirafo totɔ wɔ Misraim a

wɔbɛsoa nʼahonyade akɔ

na wɔabubu ne fapem agu fam.

5Kus ne Put, Lidia ne Arabia nyinaa, Libia ne bɔhyɛ asase no so nnipa ne Misraim bɛtotɔ wɔ afoa ano.

6“ ‘Sɛɛ na Awurade se:

“ ‘Misraim nnamfonom bɛtotɔ

na nʼahomaso ahoɔden bedi no huammɔ.

Efi Migdol kosi Aswan

wɔbɛtotɔ wɔ afoa a ɛwɔ ne mu no ano,

Otumfo Awurade asɛm ni.

7Wɔbɛdeda mpan

wɔ nsase a ada mpan mu,

na wɔn nkuropɔn bebubu aka

nkuropɔn a abubu ho.

8Afei wobehu sɛ mene Awurade no,

bere a mede ogya ato Misraim mu

na madwerɛw nʼaboafo nyinaa no.

9“ ‘Saa da no, asomafo de ahyɛn befi me nkyɛn akohunahuna Kus a ne tirim yɛ no dɛ no. Ne ho bɛyeraw no wɔ Misraim atemmuda no, na ampa ara ɛbɛba mu.

10“ ‘Sɛɛ na Otumfo Awurade se:

“ ‘Mede Misraim dɔm bebrebe no bɛba awiei

mɛfa Babiloniahene Nebukadnessar so.

11Ɔno ne nʼasraafo; amanaman no mu anuɔdenfo,

wɔde wɔn bɛba abɛsɛe asase no.

Wɔbɛtwe wɔn afoa atia Misraim

na wɔde afunu ahyɛ asase no so ma.

12Mɛma Nil mu nsu ayow

na matɔn asase no ama nnipa bɔne;

menam ananafo so

bɛsɛe asase no ne nea ɛwɔ mu nyinaa.

Me Awurade na maka.

13“ ‘Sɛɛ na Otumfo Awurade se:

“ ‘Mɛsɛe ahoni no

na mede Memfis nsɛsode ahorow no aba awiei.

Misraim rennya mmapɔmma bio,

na mɛma hu aba asase no so nyinaa.

14Mɛsɛe Misraim Atifi,

ato Soan mu gya

na matwe Tebes aso.

15Mehwie mʼabufuwhyew agu Pɛlusum so,

Misraim bammɔ dennen no,

na matwa Tebes nnipa bebrebe no agu.

16Mɛto Misraim mu gya;

Pɛlusum de ɔyaw bebubu ne mu.

Ahum bebu afa Tebes so;

na Memfis bedi abooboo da biara.

17Heliopolis ne Bubastis mmerante

bɛtotɔ wɔ afoa ano,

na nkuropɔn no ankasa bɛkɔ nnommum mu.

18Sum kabii beduru Tapanhes, da no

sɛ mibubu Misraim konnua no a;

hɔ na nʼahomaso ahoɔden bɛba awiei.

Omununkum bɛkata no so,

na ne nkuraa bɛkɔ nnommum mu.

19Ɛno nti mɛtwe Misraim aso,

na wobehu sɛ mene Awurade no.’ ”

20Afe a ɛto so dubaako no, ɔsram a edi kan no da a ɛto so ason no, Awurade asɛm baa me nkyɛn se: 21“Onipa ba, mabu Misraimhene Farao basa mu. Wɔnkyekyeree, na atoa bio; na wɔmfa nhyɛɛ ntama bamma mu na anya ahoɔden a ɔde beso afoa mu. 22Ɛno nti, Otumfo Awurade na ose: Mene Misraimhene Farao anya; mebubu nʼabasa abien no mu; basa a eye ne nea mu abu no, na mama afoa afi ne nsam atɔ fam. 23Mede Misraimfo bɛkɔ amanaman mu na mahwete wɔn agu nsase so. 24Mɛhyɛ Babiloniahene basa mu den na mede mʼafoa ahyɛ ne nsa, nanso Farao de, mebu nʼabasa mu, na wasi apini wɔ nʼanim sɛ obi a wapira opirabɔne. 25Mɛma Babiloniahene abasa mu ayɛ den, nanso Farao abasa bedwudwo asensɛn ne ho. Sɛ mede mʼafoa hyɛ Babiloniahene nsa na ɔma so tia Misraim a, wobehu sɛ mene Awurade no. 26Mede Misraimfo bɛkɔ amanaman mu na mahwete wɔn agu nsase no so. Ɛno na wobehu sɛ mene Awurade no.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ezekieli 30:1-26

Za Kulangidwa kwa Igupto

1Yehova anandiyankhula kuti: 2“Iwe mwana wa munthu, nenera ndipo ulengeze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena.

“ ‘Ufuwule mawu awa akuti,

‘Kalanga, tsiku lafika!’

3Pakuti tsiku layandikira,

tsiku la Yehova lili pafupi,

tsiku la mitambo yakuda,

tsiku lachiwonongeko cha mitundu ya anthu.

4Lupanga lidzabwera kudzalimbana ndi Igupto

ndipo mavuto adzafika pa Kusi.

Pamene anthu ambiri adzaphedwa mu Igupto,

chuma chake chidzatengedwa

ndipo maziko ake adzagumuka.

5Kusi, Puti, Ludi ndi Arabiya yense, Libiya ndiponso anthu a mʼdziko logwirizana naye adzaphedwa ndi lupanga pamodzi ndi Igupto.

6“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti:

“ ‘Onse othandiza Igupto adzaphedwa

ndipo kunyadira mphamvu zake kudzatheratu.

Adzaphedwa ndi lupanga

kuyambira ku Migidoli mpaka ku mzinda wa Asiwani,’ ”

ndikutero Ine Ambuye Yehova.

7“ ‘Dziko la Igupto lidzasanduka bwinja

kupambana mabwinja ena onse opasuka,

ndipo mizinda yake idzakhala yopasuka

kupambana mizinda ina yonse.

8Nditatha kutentha Igupto

ndi kupha onse omuthandiza,

pamenepo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.

9“ ‘Nthawi imeneyo ikadzafika, amithenga adzapita mofulumira kuchokera kwa Ine kukaopseza Kusi, iwowo osadziwako kanthu. Ndipo adzada nkhawa pa tsiku limene Igupto adzawonongedwa, chifukwa tsikulo lidzafika ndithu.

10“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndidzagwiritsa ntchito Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni

kuti ndithetse gulu lankhondo la Igupto.

11Iye ndi gulu lake lankhondo, mtundu wa anthu ankhanza kwambiri aja

adzabwera kudzawononga dzikolo.

Adzasolola malupanga awo kulimbana ndi Igupto

ndipo dziko lidzadzaza ndi mitembo.

12Ndidzawumitsa mtsinje wa Nailo

ndi kugulitsa dziko la Igupto kwa anthu oyipa.

Ndidzagwiritsa ntchito anthu achilendo kuti ndiwononge dzikolo

pamodzi ndi zonse zili mʼmenemo.

Ine Yehova ndayankhula.

13“ ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti,

“ ‘Ndidzawononga mafano

ndi kuthetsa milungu yosema ya ku Mefisi.

Simudzakhalanso mfumu mu Igupto,

ndipo ndidzaopseza dziko lonse.

14Ndidzasandutsa chipululu mzinda wa Patirosi,

ndi kutentha mzinda wa Zowani.

Ndidzalanga mzinda wa Thebesi.

15Ndidzakhuthulira ukali wanga pa mzinda wa Peluziumu,

linga lolimba la Igupto,

ndi kuwononga gulu lankhondo la Thebesi.

16Ndidzatentha ndi moto dziko la Igupto;

Peluziumu adzazunzika ndi ululu.

Malinga a Thebesi adzagumuka,

ndipo mzindawo udzasefukira ndi madzi.

17Anyamata a ku Oni ndi ku Pibeseti

adzaphedwa ndi lupanga

ndipo okhala mʼmizinda yake adzatengedwa ukapolo.

18Ku Tehafinehezi kudzakhala mdima

pamene ndidzathyola goli la Igupto;

motero kunyada kwake kudzatha.

Iye adzaphimbidwa ndi mitambo yakuda,

ndipo okhala mʼmizinda yake adzapita ku ukapolo.

19Kotero ndidzalanga dziko la Igupto,

ndipo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’ ”

Farao Watha Mphamvu

20Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi woyamba wa chaka chakhumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti: 21“Iwe mwana wa munthu, ndathyola dzanja la Farao mfumu ya Igupto. Taona, silinamangidwe kuti lipole, ngakhale kulilimbitsa ndi nsalu kuti lithe kugwiranso lupanga. 22Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti, Ine ndikudana ndi Farao mfumu ya Igupto. Ndidzathyola manja ake onse; dzanja labwino pamodzi ndi lothyokalo, ndipo lupanga lidzagwa mʼmanja mwake. 23Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. 24Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, ndipo mʼmanja mwake ndidzayikamo lupanga langa. Koma ndidzathyola manja a Farao, ndipo adzabuwula ngati wolasidwa koopsa pamaso pa mfumu ya ku Babuloniyo. 25Ndidzalimbitsa manja a mfumu ya ku Babuloni, koma manja a Farao adzafowoka. Motero anthu adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzayika lupanga langa mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ndipo adzaligwiritsa ntchito pothira nkhondo dziko la Igupto. 26Ndidzamwaza Aigupto pakati pa mitundu ya anthu, ndikuwabalalitsira ku mayiko ambiri. Motero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”