Habakuk 1 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Habakuk 1:1-17

1Eyi ne asɛm a odiyifo Habakuk nya fii Awurade nkyɛn wɔ anisoadehu mu.

Habakuk Anwiinwii

2Awurade, enkosi da bɛn na memfrɛ nsrɛ mmoa,

nanso wuntie me?

Meteɛ mu frɛ, “Akakabensɛm!”

nanso womma mmegye me.

3Adɛn na woma mehwɛ ntɛnkyew?

Adɛn nti na wotena bɔne ho?

Ɔsɛe ne akakabensɛm da mʼanim,

basabasayɛ ne abɛbrɛsɛ atwa me ho ahyia.

4Enti mmara nyɛ adwuma

na atɛntrenee nni baabiara,

atirimɔdenfo aka atreneefo ahyɛ,

enti wɔkyea atemmu.

Awurade Mmuae

5“Hwɛ aman no,

na wo ho bedwiriw wo!

Merebɛyɛ biribi wɔ wo bere so,

na sɛ wɔka kyerɛ wo a,

worennye nni.

6Merema Babiloniafo asɔre,

ɔman a wɔyɛ atirimɔdenfo ne ntɔkwapɛfo;

wobu fa asase nyinaa so,

na wɔfa tenabea a ɛnyɛ wɔn de.

7Wɔn ho yɛ hu na nnipa suro wɔn;

wɔyɛ wɔn koko so ade,

de pɛ anuonyam ma wɔn ho.

8Wɔn apɔnkɔ ho yɛ hare sen asebɔ,

na wɔn ho yɛ hu sen pataku a ɔnam anadwo,

wɔn apɔnkɔsotefo kɔ wɔn anim mmarima so,

wofi akyirikyiri nsase so,

na wɔbɔ hoo sɛ akorɔma a ɔrekɔkyere aboa.

9Wɔn nyinaa ba sɛ wɔrebɛyɛ basabasayɛ.

Wɔn dɔm pem kɔ wɔn anim te sɛ nweatam so mframa,

na wɔtase nneduafo sɛ nwea.

10Wodi ahene ho fɛw,

wɔka aman sodifo anim,

na wɔtwee nkuropɔn a ɛwɔ bammɔ dennen.

Wosisi dɔte mpie nam so kyekyere atamfo.

11Wɔbɔ hoo te sɛ mframa kɔ wɔn anim.

Afɔdifo a wɔn ahoɔden yɛ wɔn nyame.”

Habakuk Nwiinwii Bio

12Awurade, wunni hɔ fi tete ana?

Me Nyankopɔn, me Kronkronni, wo a wote ase daa.

Wo, Awurade, woapaw wɔn sɛ wommu atɛn;

wo, me Botantim, woahyɛ wɔn sɛ wɔntwe aso.

13Wʼaniwa yɛ kronkron a wuntumi nhwɛ nnebɔne;

wunnyigye nnebɔne so.

Na adɛn nti na wugyigye nnipa akɔntɔnkye so,

na dɛn nti na wayɛ komm wɔ bere a

atirimɔdenfo rememene atreneefo?

14Woama nnipa ayɛ sɛ nsumnam a ɛwɔ po mu,

te sɛ abɔde a ɛwɔ po mu a wonni sodifo.

15Ɔtamfo tirimɔdenfo no de darewa yi wɔn,

ogu nʼasau de buma wɔn,

na afei ɔsɛpɛw ne ho ma nʼani gye.

16Ne saa nti ɔbɔ afɔre ma nʼasau

na wahyew aduhuam ama no,

efisɛ asau yi so na ɔnam nya yiyedi,

na odi nʼakɔnnɔ aduan.

17Enti ɔnkɔ so nni nʼasau mu nam,

na ɔmfa atirimɔden nsɛe aman ana?

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Habakuku 1:1-17

1Uthenga umene mneneri Habakuku analandira mʼmasomphenya.

Dandawulo la Habakuku

2Kodi inu Yehova, ndidzakhala ndikukupemphani thandizo kwa nthawi yayitali motani,

koma wosayankha?

Kapena kufuwulira kwa inu kuti, “Chiwawa kuno!”

koma wosatipulumutsa?

3Chifukwa chiyani mukundionetsa zinthu zoyipa?

Chifukwa chiyani mukundionetsa mavutowa?

Ndikuona chiwonongeko ndi chiwawa;

pali ndewu ndi kukangana kwambiri.

4Kotero malamulo anu atha mphamvu,

ndipo chilungamo sichikugwira ntchito.

Anthu oyipa aposa olungama,

kotero apotoza chilungamo.

Yankho la Yehova

5“Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo penyetsetsani,

ndipo muthedwe nazo nzeru.

Pakuti ndidzachitadi zinthu pa nthawi yanu

zimene inu simudzazikhulupirira,

ngakhale wina atakufotokozerani.

6Pakuti taonani, Ine ndikuwutsa Ababuloni,

anthu ankhanza ndiponso amphamvu,

amene amapita pa dziko lonse lapansi

kukalanda malo amene si awo.

7Iwowa ndi anthu ochititsa mantha, ndipo ndi owopsa;

amadzipangira okha malamulo

ndi kudzipezera okha ulemu.

8Akavalo awo ndi aliwiro kwambiri kupambana akambuku

ndi owopsa kupambana mimbulu yolusa nthawi ya madzulo.

Okwerapo awo akuthamanga molunjika;

a pa akavalo awo ndi ochokera kutali,

akuwuluka ngati chiwombankhanga chofuna kugwira nyama;

9onse akubwera atakonzekera zachiwawa.

Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu

ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.

10Akunyoza mafumu

ndiponso kuchitira chipongwe olamulira.

Akupeputsa mizinda yonse yotetezedwa;

akumanga mitumbira ndi kulanda mizindayo.

11Kenaka amasesa mofulumira ngati mphepo nʼkumangopitirirabe,

anthu ochimwa, amene mphamvu zawo ndiye mulungu wawo.”

Dandawulo Lachiwiri la Habakuku

12Inu Yehova, kodi sindinu wachikhalire?

Mulungu wanga, Woyera wanga, ife sitidzafa.

Inu Yehova, munawasankha anthuwo kuti abweretse chiweruzo;

Inu Thanthwe, munawayika iwowo kuti atilange.

13Maso anu ndi oyera kwambiri safuna kuona choyipa;

Inu simulekerera cholakwa.

Chifukwa chiyani nanga mukulekerera anthu ochita zachinyengowa?

Chifukwa chiyani muli chete pamene anthu oyipa

akuwononga anthu olungama kupambana iwowo?

14Mwasandutsa anthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja,

ngati zolengedwa zamʼnyanja zimene zilibe wolamulira.

15Mdani wawo woyipa amakoka anthu onse ndi mbedza,

amawakola mu ukonde wake,

amawasonkhanitsa mu khoka lake;

kotero iyeyo amakondwa ndi kusangalala.

16Choncho iye amaperekera nsembe ukonde wake

ndiponso kufukizira lubani khoka lake,

popeza ukonde wakewo ndiye umamubweretsera moyo wapamwamba

ndipo amadya chakudya chabwino kwambiri.

17Kodi iye azipitirabe kugwiritsa ntchito makoka akewo,

kuwononga mitundu ya anthu mopanda chifundo?