2 Samuel 22 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

2 Samuel 22:1-51

Dawid Ayeyi Dwom

1Bere a Awurade gyee Dawid fii nʼatamfo nyinaa ne Saulo nsam akyi no, ɔtoo saa dwom yi de yii Awurade ayɛ.

2Nsɛm a ɛwɔ dwom no mu ni:

Awurade yɛ me botan, mʼaban ne mʼagyenkwa;

3me Nyankopɔn yɛ me botan; ne mu na minya guankɔbea.

Ɔyɛ me kyɛm, me nkwagye mu ahoɔden,

mʼabandennen, mʼagyenkwa, nea ogye me fi basabasayɛ mu.

4“Misu frɛ Awurade; ɔno na ayeyi sɛ no,

efisɛ ogye me fi mʼatamfo nsam.

5Owu asorɔkye twaa me ho hyiae;

ɔsɛe yiri faa me so.

6Ɔda mu hama kyekyeree me;

mihyiaa owu mfiri.

7“Na mʼamanehunu mu no, misu frɛɛ Awurade.

Yiw, mefrɛɛ me Nyankopɔn pɛɛ mmoa.

Ɔtee me nne fii ne kronkronbea.

Me sufrɛ duu nʼasom.

8Na asase wosowee na ehinhimii;

ɔsoro fapem wosowee;

wɔwosowee, nʼabufuw nti.

9Wusiw fii ne hwene mu;

ogyaframa fii nʼanom;

na nnyansramma dɛw fii mu.

10Ofii ɔsoro baa fam;

na omununkum kabii duruu nʼanan ase.

11Ɔte kerubim so tui;

gyaagyaa ne ho wɔ mframa ntaban so.

12Ɔde sum kataa ne ho hyiae,

ɔde osu mununkum dii nʼanim kan.

13Hann kɛse hyerɛn wɔ nʼanim,

na anyinam pa fii mu.

14Awurade bobɔɔ mu fi ɔsoro;

Ɔsorosoroni no teɛɛ mu dennen.

15Ɔtow nʼagyan maa nʼatamfo hwetee;

anyinam twa ma wɔyɛɛ basaa.

16Awurade kasae,

na wiase nnyinaso no nyinaa daa hɔ.

Wotumi huu ɛpo ase,

na asase fapem ho daa hɔ.

17“Ofi ɔsoro baa fam besoo me mu;

ɔtwee me fii asu a emu dɔ mu.

18Ogyee me fii mʼatamfo a wɔyɛ den nsam,

atamfo a wokyi me na wɔn ho yɛ den pa ara sen me.

19Wɔbaa me so wɔ mʼamanehunu da,

nanso Awurade pagyaw me.

20Ɔde me baa baabi a bammɔ wɔ;

ogyee me, efisɛ nʼani kum me ho.

21Awurade atua me papayɛ so ka;

me bem a midi no, wahyɛ me anan mu.

22Efisɛ manantew Awurade akwan so;

mentwee me ho mfii me Nyankopɔn ho nkɔyɛɛ bɔne.

23Ne mmara nyinaa gu mʼanim;

mentwee me ho mfii ne nhyehyɛe ho.

24Me ho nni asɛm wɔ Onyankopɔn anim;

matwe me ho afi bɔne ho.

25Awurade tuaa me papayɛ so ka,

efisɛ minni fɔ wɔ nʼanim.

26“Woda wo ho adi sɛ ɔnokwafo kyerɛ wɔn a wodi nokware,

wɔn a wodi mu nso wo kyerɛ wɔn sɛ wodi mu.

27Wuyi wo kronkronyɛ kyerɛ ɔkronkronni,

nanso amumɔyɛfo de wukyi wɔn.

28Wugye ahobrɛasefo,

nanso wʼani kɔ ahantanfo so sɛ wobɛbrɛ wɔn ase.

29Wo Awurade, woyɛ me kanea.

Yiw, Awurade woma me sum dan hann.

30Wʼahoɔden mu, metumi aka asraafokuw agu;

me Nyankopɔn nti, mitumi foro ɔfasu.

31“Onyankopɔn de, nʼakwan yɛ pɛ;

Awurade bɔhyɛ nyinaa ba mu.

Ɔyɛ nkatabo

ma wɔn a wɔhwehwɛ bammɔ wɔ ne mu.

32Hena ne Onyankopɔn, gye sɛ Awurade?

Hena ne ɔbotantim no, gye sɛ yɛn Nyankopɔn?

33Onyankopɔn ne mʼaban a ɛyɛ den;

wagye me, na wama me kwan so ayɛ pɛ.

34Ɔma mʼanammɔn ho yɛ hare sɛ ɔforote de;

Ɔma me gyina sorɔnsorɔmmea.

35Osiesie me ma ɔko;

na me basa tumi kuntun kɔbere mfrafrae tadua.

36Woama me wo nkwagye kyɛm.

Wo mmoa ama mayɛ ɔkɛse.

37Woabɔ kwan tɛtrɛɛ ama mʼanan

sɛnea me nkotodwe rengurow.

38“Metaa mʼatamfo sɛee wɔn;

mannyina kosii sɛ wodii nkogu.

39Meyam wɔn, mebɔɔ wɔn hwee fam, na wɔantumi ansɔre;

wɔhwehwee ase wɔ mʼanan ase.

40Wohyɛɛ me ahoɔden maa ɔko;

woaka mʼatamfo ahyɛ mʼanan ase.

41Womaa wɔdan wɔn ani guanee,

na mesɛe wɔn a wɔtan me nyinaa.

42Wosu pɛɛ mmoa, nanso obiara ammegye wɔn.

Wosu frɛɛ Awurade, nanso wannye wɔn so.

43Meyam wɔn ma wɔyɛɛ sɛ asase so mfutuma;

mepraa wɔn guu suka mu sɛ wura.

44“Womaa me nkonimdi wɔ wɔn a wɔbɔ me kwaadu so.

Woahwɛ sɛ mɛyɛ amanaman sodifo;

na nnipa a minnim wɔn som me.

45Ananafo brɛ wɔn ho ase ma me;

wɔte me nka pɛ ara a, wɔde wɔn ho ma me.

46Wɔn nyinaa bɔ huboa,

na wɔde ahopopo fi wɔn nsraban mu ba.

47Awurade te ase! Ayeyi nka me botan,

ma wɔmma Onyankopɔn, me nkwagye botan so.

48Ɔno ne Onyankopɔn a ɔtɔ wɔn a wɔhaw me so were;

ɔka amanaman no hyɛ mʼase

49na ogye me fi mʼatamfo nsam.

Wode me si baabi a mʼatamfo nnu,

wugye me fi atutuwpɛfo a wotia me nsam.

50Awurade eyi nti, mɛkamfo wo wɔ amanaman mu, Ao Awurade.

Mɛto ayeyi dwom ama wo din.

51“Wode nkonimdi akɛse ama wo hene;

woda ɔdɔ a ɛnsa da adi kyerɛ nea woasra no ngo,

wode kyerɛ Dawid, ne nʼasefo afebɔɔ.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

2 Samueli 22:1-51

Nyimbo ya Mayamiko ya Davide

1Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli. 2Iye anati,

“Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.

3Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo,

chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa.

Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga.

Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.

4“Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando,

ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.

5“Mafunde a imfa anandizinga;

mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.

6Anandimanga ndi zingwe za ku manda;

misampha ya imfa inalimbana nane.

7“Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova;

ndinapemphera kwa Mulungu wanga.

Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga;

kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.

8“Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi,

maziko a miyamba anagwedezeka;

ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.

9Mʼmphuno mwake munatuluka utsi;

moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake,

makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.

10Iye anangʼamba thambo natsika pansi;

pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.

11Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka;

nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.

12Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake,

mitambo yakuda ya mlengalenga.

13Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake

munkachokera makala amoto alawilawi.

14Yehova anabangula kumwamba ngati bingu,

mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.

15Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake,

ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.

16Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera,

ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera,

Yehova atabangula mwaukali,

pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.

17“Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira;

anandivuwula mʼmadzi ozama.

18Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu,

adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.

19Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto,

koma Yehova anali thandizo langa.

20Iye anandipititsa kumalo otakasuka;

anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.

21“Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa;

molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.

22Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova;

ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.

23Malamulo ake onse ali pamaso panga,

sindinasiye malangizo ake.

24Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake

ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.

25Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa,

molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.

26“Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu,

kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,

27Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu,

koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.

28Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa,

koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.

29Inu Yehova, ndinu nyale yanga;

Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.

30Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo,

ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.

31“Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro;

mawu a Yehova alibe cholakwika.

Iye ndi chishango

kwa onse amene amathawira kwa iye.

32Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova?

Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?

33Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu

ndi kulungamitsa njira yanga.

34Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi;

Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.

35Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo;

manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.

36Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso;

mumawerama kuti mundikweze.

37Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino,

kuti mapazi anga asaterereke.

38“Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha;

sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.

39Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso;

Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.

40Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo;

munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.

41Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa;

ndipo ndinawononga adani anga.

42Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa.

Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.

43Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi;

ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.

44“Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu;

Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina.

Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.

45Alendo amadzipereka okha pamaso panga;

akangomva za ine, amandigonjera.

46Iwo onse anataya mtima;

anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.

47“Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa.

Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!

48Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango,

amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,

49amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga.

Inu munandikuza kuposa adani anga;

munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.

50Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina;

ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.

51“Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake,

amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake,

kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”