Ɔsɛnkafo 7 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Ɔsɛnkafo 7:1-29

Nimdeɛ

1Din pa yɛ sen aduhuam papa,

na owuda yɛ sen awoda.

2Eye sɛ obi bɛkɔ ayi ase

sen sɛ ɔbɛkɔ aponto ase,

efisɛ owu yɛ onipa biara nkrabea

na ɛsɛ sɛ ateasefo hyɛ eyi nsow.

3Awerɛhow ye sen ɔserew,

efisɛ anim a ayɛ mmɔbɔmmɔbɔ de koma mu nsiesie pa ba.

4Onyansafo koma wɔ ayi ase,

nanso nkwaseafo koma wɔ ahosɛpɛwfo fi.

5Eye sɛ wobetie onyansafo animka

sen sɛ wobetie nkwaseafo dwom.

6Sɛnea nsɔe turuturuw wɔ ɔsɛn ase no

saa ara na nkwaseafo serew te.

Eyi nso yɛ ahuhude.

7Asisi ma onyansafo dan ɔkwasea,

na kɛtɛasehyɛ sɛe koma.

8Asɛm awiei ye sen ne mfiase,

na ntoboase ye sen ahantan.

9Mma wo koma nsɔre ntɛmntɛm,

na abufuw da nkwaseafo srɛ so.

10Nka se, “Adɛn nti na tete nna no ye sen nnɛ mmere yi?”

Onyansafo mmisa nsɛm sɛɛ.

11Nimdeɛ, ɛyɛ ade pa sɛ agyapade ara pɛ,

so wɔ mfaso ma wɔn a wohu owia.

12Sɛnea nimdeɛ yɛ bammɔ no,

saa ara na sika nso te;

nanso nhumu ho ade a eye ne sɛ:

nea ɔwɔ nimdeɛ no bɔ ne nkwa ho ban.

13Dwene nea Onyankopɔn ayɛ ho:

Hena na obetumi ateɛ

nea wɔama akyea?

14Mmere pa mu, ma wʼani nnye;

nanso mmere bɔne mu, hu sɛ

Onyankopɔn na wayɛ ne nyinaa.

Ɛno nti onipa rentumi nhu

nea ɛbɛto no daakye.

15Me nkwanna a ɛyɛ ahuhude yi mu, mahu nneɛma abien:

Ɔtreneeni a owu wɔ ne trenee mu,

ne omumɔyɛfo a ɔtena ase kyɛ wɔ nʼamumɔyɛ mu.

16Nyɛ wo ho ɔtreneeni ntra so,

na nyɛ wo ho onyansafo mmoro so;

adɛn nti na wosɛe wo ho?

17Nyɛ omumɔyɛfo ntra so,

na nyɛ ɔkwasea nso,

adɛn nti na ɛsɛ sɛ wuwu ansa na wo bere aso.

18Eye sɛ wubeso baako no mu den

nanso nnyaa nea aka no mu.

Onipa a osuro Onyankopɔn no besiw nneyɛe mmoroso nyinaa ano.

19Nimdeɛ ma onyansafo baako tumi bebree

sen kuropɔn mu asodifo du.

20Onipa treneeni biara nni asase so a

ɔyɛ papa na ɔnyɛ bɔne da.

21Mfa nea nnipa ka nyinaa nyɛ asɛm,

anyɛ saa a wobɛte sɛ wo somfo redome wo,

22na wunim wɔ wo koma sɛ

wo nso woadome nkurɔfo mpɛn bebree.

23Mede nimdeɛ asɔ eyinom nyinaa ahwɛ, na mekae se,

“Masi mʼadwene pi sɛ mɛyɛ onyansafo”

nanso na eyi boro me so.

24Sɛnea nimdeɛ te biara,

ɛwɔ akyiri na emu dɔ,

hena na obetumi ahwehwɛ ahu?

25Afei meyɛɛ mʼadwene sɛ mɛte ase,

ayɛ nhwehwɛmu na mapɛɛpɛɛ nimdeɛ ne sɛnea nneɛma nhyehyɛe te

na mate amumɔyɛ mu agyimisɛm ase,

ne nkwaseasɛm mu adammɔsɛm nso.

26Mahu nea ɛyɛ nwene sen owu;

ɔbea a ɔyɛ afiri;

ne koma yɛ nnaadaa

na ne nsa yɛ mpokyerɛ.

Onipa a ɔsɔ Onyankopɔn ani no renkɔ ne ho

nanso ɔbɔnefo de ɔbɛtɔ nʼafiri mu.

27Ɔsɛnkafo no se, “Hwɛ eyi ne nea mahwehwɛ ahu:

“Mekekaa nneɛma bobɔɔ so pɛɛ sɛ mihu sɛnea nneɛma nhyehyɛe te,

28mereyɛ nhwehwɛmu,

na minhu hwee no,

mihuu ɔbarima treneeni baako wɔ mmarima apem mu,

nanso manhu ɔbea treneeni biara wɔ wɔn mu.

29Eyi nko ara na mahu:

Onyankopɔn yɛɛ adesamma atreneefo,

nanso nnipa adan wɔn ho hwehwɛ nhyehyɛe foforo.”

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 7:1-29

Nzeru

1Mbiri yabwino ndi yopambana mafuta onunkhira bwino,

ndipo tsiku lomwalira ndi lopambana tsiku lobadwa.

2Kuli bwino kupita ku nyumba yamaliro

kusiyana ndi kupita ku nyumba yamadyerero:

Pakuti imfa ndiye mathero a munthu aliyense;

anthu amoyo azichisunga chimenechi mʼmitima mwawo.

3Chisoni nʼchabwino kusiyana ndi kuseka,

pakuti nkhope yakugwa ndi yabwino chifukwa imakonza mtima.

4Mtima wa munthu wanzeru nthawi zonse umalingalira za imfa,

koma mitima ya zitsiru imalingalira za chisangalalo.

5Kuli bwino kumva kudzudzula kwa munthu wanzeru

kusiyana ndi kumvera mayamiko a zitsiru.

6Kuseka kwa zitsiru kuli ngati

kuthetheka kwa moto kunsi kwa mʼphika,

izinso ndi zopandapake.

7Kuzunza ena kumasandutsa munthu wanzeru kukhala chitsiru,

ndipo chiphuphu chimawononga mtima.

8Mathero ake a chinthu ndi abwino kupambana chiyambi chake,

ndipo kufatsa nʼkwabwino kupambana kudzikuza.

9Usamafulumire kukwiya mu mtima mwako,

pakuti mkwiyo ndi bwenzi la zitsiru.

10Usamafunse kuti, “Nʼchifukwa chiyani masiku amakedzana anali abwino kupambana masiku ano?”

pakuti si chinthu chanzeru kufunsa mafunso oterewa.

11Nzeru ngati cholowa, ndi chinthu chabwino

ndipo imapindulitsa wamoyo aliyense pansi pano.

12Nzeru ndi chitetezo,

monganso ndalama zili chitetezo,

koma phindu la chidziwitso ndi ili:

kuti nzeru zimasunga moyo wa munthu amene ali nazo nzeruzo.

13Taganizirani zimene Mulungu wazichita:

ndani angathe kuwongola chinthu

chimene Iye anachipanga chokhota?

14Pamene zinthu zili bwino, sangalala;

koma pamene zinthu sizili bwino, ganizira bwino:

Mulungu ndiye anapanga nthawi yabwinoyo,

ndiponso nthawi imene si yabwinoyo.

Choncho munthu sangathe kuzindikira

chilichonse cha mʼtsogolo mwake.

15Pa moyo wanga wopanda phinduwu ndaona zinthu ziwiri izi:

munthu wolungama akuwonongeka mʼchilungamo chake,

ndipo munthu woyipa akukhala moyo wautali mʼzoyipa zake.

16Usakhale wolungama kwambiri

kapena wanzeru kwambiri,

udziwonongerenji wekha?

17Usakhale woyipa kwambiri,

ndipo usakhale chitsiru,

uferenji nthawi yako isanakwane?

18Nʼkwabwino kuti utsate njira imodzi,

ndipo usataye njira inayo.

Munthu amene amaopa Mulungu adzapewa zinthu ziwiri zonsezi.

19Nzeru zimapereka mphamvu zambiri kwa munthu wanzeru

kupambana olamulira khumi a mu mzinda.

20Palibe munthu wolungama pa dziko lapansi

amene amachita zabwino zokhazokha ndipo sachimwa.

21Usamamvetsere mawu onse amene anthu amayankhula,

mwina udzamva wantchito wako akukutukwana,

22pakuti iwe ukudziwa mu mtima mwako

kuti nthawi zambiri iwenso unatukwanapo ena.

23Zonsezi ndinaziyesa ndi nzeru zanga ndipo ndinati,

“Ine ndatsimikiza mu mtima mwanga kuti ndikhale wanzeru,”

koma nzeruyo inanditalikira.

24Nzeru zimene zilipo,

zili kutali ndipo ndi zozama kwambiri,

ndani angathe kuzidziwa?

25Kotero ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe,

ndifufuze ndi kumafunafuna nzeru ndi mmene zinthu zimakhalira

ndipo ndinafunanso kudziwa kuyipa kwa uchitsiru

ndiponso kupusa kwake kwa misala.

26Ndinapeza kanthu kowawa kupambana imfa,

mkazi amene ali ngati khoka,

amene mtima wake uli ngati khwekhwe,

ndipo manja ake ali ngati maunyolo.

Munthu amene amakondweretsa Mulungu adzathawa mkaziyo,

koma mkaziyo adzakola munthu wochimwa.

27Mlaliki akunena kuti, “Taonani, chimene ndinachipeza ndi ichi:

“Kuwonjezera chinthu china pa china kuti ndidziwe mmene zinthu zimachitikira,

28pamene ine ndinali kufufuzabe

koma osapeza kanthu,

ndinapeza munthu mmodzi wolungama pakati pa anthu 1,000,

koma pakati pawo panalibepo mkazi mmodzi wolungama.

29Chokhacho chimene ndinachipeza ndi ichi:

Mulungu analenga munthu, anamupatsa mtima wolungama,

koma anthu anatsatira njira zawozawo zambirimbiri.”