Ɔsɛnkafo 6 – AKCB & CCL

Akuapem Twi Contemporary Bible

Ɔsɛnkafo 6:1-12

1Mahu bɔne foforo bi wɔ owia yi ase a ɛhyɛ nnipa so yiye: 2Onyankopɔn ma onipa ahonyade, adenya ne anuonyam sɛnea biribiara a ne koma pɛ no ɛremmɔ no, nanso Onyankopɔn amma no kwan sɛ ɔmfa nnye nʼani, na ɔhɔho mmom na ɔde gye nʼani. Eyi yɛ ahuhude, ɔhaw a ɛyɛ yaw.

3Onipa betumi anya mma ɔha na wanyin akyɛ; nanso ne mfe dodow yi akyi no, nʼahonya no amma nʼani annye na ne sie nso anyɛ fɛ a, ɔpɔn ba so wɔ mfaso sen no. 4Ne ba no yɛ ade hunu, sum mu na ɔkɔ, na sum akata ne din so. 5Ɛwɔ mu sɛ wanhu owia na onnim hwee de, nanso obenya ahomegye bebree sen nea saa ɔbarima no benya, 6mpo sɛ ɔtena ase mfe apem mmɔho na wamfa nʼahonyade annye nʼani a, wɔn nyinaa nkɔ faako ana?

7Onipa brɛ nyinaa yɛ nʼano ntia,

nanso nʼakɔnnɔde mmee no da.

8Na dɛn na onyansafo wɔ de sen ɔkwasea?

Sɛ ohiani yɛ nʼakwan yiye wɔ afoforo anim a

mfaso bɛn na obenya?

9Nea aniwa hu no

ye sen nea akɔnnɔ kyin hwehwɛ.

Eyi nso yɛ ahuhude,

ɛte sɛ wotaa mframa.

10Nea ɛwɔ hɔ biara, wɔato din dedaw,

na sɛnea onipa te nso, wonim dedaw;

onipa biara rentumi ne nea ɔwɔ ahoɔden

sen no nnye eyi ho akyinnye.

11Nsɛm dɔɔso a,

mu ntease sua,

na so wɔ mfaso ma onipa ana?

12Na hena na onim nea eye ma onipa wɔ ne nkwanna kakraa bi a ɛyɛ ahuhude na ɔfa mu kɔ sɛ sunsuma no mu? Hena na obetumi aka nea ebesi wɔ owia yi ase akyerɛ no bere a ɔkɔ no?

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 6:1-12

1Ine ndinaona choyipa china pansi pano, ndipo chimasautsa anthu kwambiri: 2Mulungu amapereka chuma, zinthu ndi ulemu kwa munthu, kotero kuti munthuyo sasowa kanthu kalikonse kamene akukalakalaka, koma Mulungu samulola kuti adyerere zinthuzo, ndipo mʼmalo mwake amadyerera ndi mlendo. Izi ndi zopandapake, ndi zoyipa kwambiri.

3Ngakhale munthu atabereka ana 100 ndi kukhala ndi moyo zaka zambiri; komatu ngakhale atakhala zaka zambiri chotani, ngati iye sangadyerere chuma chake ndi kuyikidwa mʼmanda mwaulemu, ine ndikuti mtayo umamuposa iyeyo. 4Mtayo umangopita pachabe ndipo umapita mu mdima, ndipo mu mdimamo dzina lake limayiwalika. 5Ngakhale kuti mtayowo sunaone dzuwa kapena kudziwa kanthu kalikonse, koma umapumula kuposa munthu uja, 6ngakhale munthuyo atakhala ndi moyo zaka 2,000, koma ndi kulephera kudyerera chuma chake. Kodi onsewa sapita malo amodzi?

7Ntchito yonse ya munthu imathera pakamwa pake,

komatu iye sakhutitsidwa ndi pangʼono pomwe.

8Kodi munthu wanzeru

amaposa motani chitsiru?

Kodi munthu wosauka amapindula chiyani

podziwa kukhala bwino pamaso pa anthu ena?

9Kuli bwino kumangoona zinthu ndi maso

kusiyana ndi kumangozilakalaka mu mtima.

Izinso ndi zopandapake,

nʼkungodzivuta chabe.

10Chilichonse chimene chilipo anachitchula kale dzina,

za mmene munthu alili nʼzodziwika;

sangathe kutsutsana ndi munthu

amene ali wamphamvu kupambana iyeyo.

11Mawu akachuluka

zopandapake zimachulukanso,

nanga munthu zimamupindulira chiyani?

12Pakuti ndani amene amadziwa chomwe ndi chabwino pa moyo wa munthu, pakuti moyo wake ndi wa masiku ochepa ndi opandapake, umangopitira ngati mthunzi. Ndani amene angamufotokozere zimene zidzachitika pansi pano iye atapita?